1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
tsopano wasanduka kapolo.
2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
onse akhala adani ake.
3Yuda watengedwa ku ukapolo,
kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
ndipo alibe kwina kothawira.
4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5Adani ake asanduka mabwana ake;
odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
pamaso pa mdani.
6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
owathamangitsa.
7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8Yerusalemu wachimwa kwambiri
ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
ndipo akubisa nkhope yake.
9Uve wake umaonekera pa zovala zake;
iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
pakuti mdani wapambana.”
10Adani amulanda
chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
amene Inu Mulungu munawaletsa
kulowa mu msonkhano wanu.
11Anthu ake onse akubuwula
pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
chifukwa ine ndanyozeka.”
12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
pa tsiku la ukali wake?
13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
wolefuka tsiku lonse.
14“Wazindikira machimo anga onse
ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15“Ambuye wakana
anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
anamwali a Yuda.
16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira
ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
chifukwa mdani watigonjetsa.
17“Ziyoni wakweza manja ake,
koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18“Yehova ndi wolungama,
koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
agwidwa ukapolo.
19“Ndinayitana abwenzi anga
koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
kuti akhale ndi moyo.
20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21“Anthu amva kubuwula kwanga,
koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
ndipo mtima wanga walefuka.”
凄惨的耶路撒冷
1从前人烟稠密的城,
现在何其荒凉!
从前扬威万邦的强国,
现在竟像寡妇一样。
从前在诸省做公主的,
现在却沦为奴婢。
2她在夜间痛哭,泪流满面。
情人中没有一个前来安慰。
朋友都出卖她,与她为敌。
3犹大饱受苦难和奴役,
被掳往远方,流落异邦,
找不到安居之所。
她在走投无路之际被追敌擒获。
4通往锡安1:4 “锡安”又称“耶路撒冷”。的道路满目凄凉,
因为无人前去过节。
她的城门冷落,
她的祭司悲叹,
她的少女哀伤,她痛苦不已。
5敌人做了她的主人,
兴旺发达。
因为她作恶多端,
耶和华叫她饱受困苦,
她的孩子被敌人掳去。
6锡安的尊荣消逝,
她的首领像找不到草吃的鹿,
无力逃脱敌人的追赶。
7在困苦流离中,
耶路撒冷想起昔日的荣华。
如今,她的人民落在敌人手中,
无人援救。
仇敌看见她,都嘲笑她的灭亡。
8耶路撒冷罪大恶极,
沦为污秽之物。
从前尊重她的人看见她赤身裸体,就蔑视她。
她只能哀叹、退避。
9她的裙子沾满污秽,
她未曾想过自己的结局。
她的败落无比凄惨,
无人安慰。
她哭喊道:“耶和华啊,
仇敌已经获胜,
求你垂顾我的苦难!”
10敌人伸手夺去她的一切珍宝。
她目睹外族人闯入圣殿——那是耶和华禁止他们进入的地方。
11她的人民呻吟着四处觅食,
用珍宝换取粮食维生。
耶路撒冷的哀叹
她说:“耶和华啊,求你眷顾我,
因为我被人蔑视。
12“路人啊,你们都无动于衷吗?
你们看看,
耶和华向我发烈怒,降祸于我,
还有谁比我更痛苦呢?
13“祂从高天降下火来,
焚烧我的骨头;
祂在我脚前设下网罗,
使我返回;
祂使我凄凉孤寂,终日痛苦。
14“我的罪恶连接成轭,
祂亲手把它们编在一起,
绑在我的颈项上,
使我筋疲力尽。
主把我交给我无力抵挡的敌人。
15“主藐视我所有的勇士,
召集军队攻击我,
打垮我的青年。
主践踏犹大人1:15 “犹大人”希伯来文是“犹大的纯洁少女”。,
如同在榨酒池踩踏。
16“我为此哭泣,
泪流满面,
却无人安慰、鼓励我。
我的儿女凄凉孤苦,
因为仇敌已经得胜。”
17锡安伸手求助,却无人理睬。
耶和华已命四周邻国与雅各为敌。
耶路撒冷在他们当中成了污秽之物。
18“但耶和华是公义的,
因为我违背了祂的命令。
万国啊,请听我的话,
看看我的痛苦!
我的年轻男女都被掳去。
19“我向情人们求助,
他们却欺骗我。
我的祭司和长老在觅食求生时,
倒毙在城中。
20“耶和华啊,
看看我是多么痛苦!
我的内脏搅动,
我的心灵翻腾,
因为我背叛了你。
街上有屠杀,
家中有死亡。
21“人们听见我的哀叹,
却无人安慰我。
敌人看见你降给我的灾难,
都幸灾乐祸。
愿你应许的审判之日来临,
叫他们像我一样受苦!
22“愿他们的恶行都摆在你眼前!
你怎样因我的罪恶而惩罚我,
愿你也照样惩罚他们!
我叹息不绝,心中哀伤。”