Psalm 13
For the director of music. A psalm of David.
1Lord, how long must I wait? Will you forget me forever?
How long will you turn your face away from me?
2How long must I struggle with my thoughts?
How long must my heart be sad day after day?
How long will my enemies keep winning the battle over me?
3Lord my God, look at me and answer me.
Give me new life, or I will die.
4Then my enemies will say, “We have beaten him.”
They will be filled with joy when I die.
5But I trust in your faithful love.
My heart is filled with joy because you will save me.
6I will sing praise to the Lord.
He has been so good to me.
Salimo 13
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?
Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2Ndidzalimbana ndi maganizo anga
ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?
Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.
Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”
ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;
mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6Ine ndidzayimbira Yehova
pakuti wandichitira zokoma.