Zekariya 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 9:1-17

Chiweruzo pa Adani a Israeli

Ulosi

1Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki

ndi mzinda wa Damasiko

pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli

ali pa Yehova—

2ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,

komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.

3Ndipo Turo anadzimangira linga;

wadziwunjikira siliva ngati fumbi,

ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.

4Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho

ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,

ndipo adzapserera ndi moto.

5Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;

Gaza adzanjenjemera ndi ululu,

chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.

Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa

ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.

6Mu Asidodi mudzakhala mlendo,

ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.

7Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,

chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.

Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,

adzasanduka atsogoleri mu Yuda,

ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.

8Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga

ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.

Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,

pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.

Kubwera kwa Mfumu ya Ziyoni

9Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!

Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!

Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,

yolungama ndi yogonjetsa adani,

yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,

pa mwana wamphongo wa bulu.

10Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu

ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,

ndipo uta wankhondo udzathyoka.

Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.

Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,

ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

11Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,

ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.

12Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;

ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.

13Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,

ndipo Efereimu ndiye muvi wake.

Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,

kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,

ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.

Kuoneka kwa Yehova

14Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;

mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.

Ambuye Yehova adzaliza lipenga;

ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,

15ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.

Iwo adzawononga

ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.

Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;

magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi

pa ngodya za guwa lansembe.

16Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa

pakuti anthu ake ali ngati nkhosa.

Adzanyezimira mʼdziko lake

ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.

17Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!

Tirigu adzasangalatsa anyamata,

ndi vinyo watsopano anamwali.

New Russian Translation

Захария 9:1-17

Суд над врагами Израиля

1Пророческое слово от Господа против земли Хадраха9:1 Хадрах – многие предполагают, что это может быть Хатарикка – город и страна, лежавшие севернее Хамата (см. ст. 2) и упоминаемые в ассирийских клинописях.,

оно касается и Дамаска –

так как на Господа смотрят все люди

и все роды Израиля9:1 Или: «Так как Господь смотрит на всех людей и на все роды Израиля»., –

2касается и Хамата, который граничит с Дамаском9:2 Букв.: «с ней».,

и Тира с Сидоном, хотя они так мудры.

3Тир себе выстроил крепость;

накопил серебра, как пыли,

и золота, как уличной грязи.

4Но Владыка отнимет у него добро,

бросит в море его богатства,

а сам он сгорит дотла.

5Ашкелон увидит и устрашится,

и сожмется от страха Газа,

и Экрон вместе с ними:

погибла его надежда.

Не станет в Газе царя,

и Ашкелон опустеет.

6Ашдод заселится чужестранцами;

Я сломлю гордость филистимлян.

7Я исторгну из уст их кровь,

из зубов их – запретную пищу.

Уцелевшие из них будут поклоняться нашему Богу,

они станут одним из кланов Иуды,

а Экрон уподобится иевусеям9:7 Уподобится иевусеям – вероятно здесь говорится о том, что хотя вначале иевусеи и были врагами Бога, все же позже они вошли в состав израильского народа и стали участниками благословений Бога. См. 2 Пар. 3:1..

8Свой дом окружу Я охранным дозором

от грабительских свор.

Никакой обидчик к ним впредь не явится,

ведь ныне Я Сам на страже.

Будущий Царь Сиона

9Возликуй великим ликованием, дочь Сиона!

Кричи от радости, дочь Иерусалима!

Вот, Царь твой идет к тебе, погляди,

торжествующий, победоносный,

кроткий, верхом на ослице и на осленке,

сыне вьючного животного9:9 Эти слова являются пророчеством об Иисусе Христе (см. Мат. 21:5; Ин. 12:15)..

10Он истребит9:10 Так в одном из древних переводов; букв.: «Я истреблю». колесницы в Ефреме

и коней боевых в Иерусалиме,

и лук боевой будет сломан.

Он возвестит мир народам.

Его владычество будет от моря до моря

и от реки Евфрата – до краев земли.

11– Что до тебя, то ради Моего завета с тобой, скрепленного кровью,

Я освобожу твоих пленников из безводного рва.

12Возвращайтесь в свою крепость,

узники, у которых теперь есть надежда9:12 Букв.: «узники надежды».;

сегодня Я возвещаю, что воздам тебе

вдвое больше, чем ты потерял.

13Я как лук натяну Иудею,

а стрелой положу Ефрема.

Я подниму твоих сыновей, Сион,

против твоих сыновей, Греция,

и буду воевать тобой, словно мечом.

Явление Господа

14Тогда явится над ними Господь,

и сверкнет Его стрела, словно молния.

В рог затрубит Владыка Господь

и будет идти в южных бурях.

15Господь Сил их защитит,

и они одолеют и истребят пращников9:15 Возможный текст; букв.: «пращные камни»..

Они напьются крови и будут шуметь,

как от вина9:15 В одном из древних переводов: «будут кровь их пить, как вино»., наполнятся ею, словно чаши,

из которых кропят углы жертвенника.

16Господь, их Бог, спасет их в тот день,

ведь они – овцы Его стада.

Как драгоценные камни в венце,

они будут сверкать на Его земле.

17Как прекрасны и хороши они будут!

От зерна расцветут юноши,

а девушки от молодого вина.