Malaki 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 1:1-14

1Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.

Ndamukonda Yakobo, Ndamuda Esau

2Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’ ”

Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo, 3koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”

4Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.”

Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya. 5Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’

Nsembe Zosayenera

6“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’

7“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’

“Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka. 8Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

9“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

10“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu. 11Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

12“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’ 13Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova. 14“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’ ”

New Russian Translation

Малахия 1:1-14

1Пророческое слово Господа к Израилю через Малахию1:1 С еврейского языка это имя переводится как «Мой вестник»..

Иаков предпочтен Эдому

2– Я возлюбил вас, – говорит Господь, – а вы говорите: «В чем Ты проявил любовь к нам?» Разве Исав не был братом Иакова? – возвещает Господь. – Но Я полюбил Иакова, 3а Исава возненавидел. Я предал его нагорья опустошению и бросил его надел шакалам пустыни.

4Если Эдом говорит: «Мы разгромлены, но отстроим разрушенное», то Господь Сил1:4 Евр.: «ЙГВГ Цеваот»; так же и в других местах книги. говорит: «Они отстроят, а Я разрушу. Их назовут Нечестивым Краем, народом, на который Господь прогневался навеки. 5Вы сами увидите это и скажете: „Господь велик и за пределами Израиля!“»

Негодные жертвоприношения

6– Сын почитает отца, а слуга – своего господина. Если Я Отец, то где почтение ко Мне? Если Я Господин, то где ко Мне уважение? – говорит вам, священники, бесчестящие Мое имя, Господь Сил.

Вы говорите: «Чем мы бесчестим Твое имя?». 7Вы кладете на Мой жертвенник оскверненную пищу.

Вы говорите: «Чем мы Тебя осквернили?» Вы считаете, что столом Господа можно пренебрегать. 8Когда вы приносите в жертву слепых животных, разве это не преступление? Когда вы приносите хромое и больное, разве это не преступление? Предложи-ка это своему правителю! Будет он тобою доволен? Будет он к тебе благосклонен? – говорит Господь Сил.

9Молите Бога, чтобы Он нас помиловал!

– За такие жертвы из ваших рук будет ли Он к вам благосклонен? – говорит Господь Сил. – 10Запер бы лучше кто-либо из вас двери храма, чтобы вы не жгли напрасно на Моем жертвеннике огня! Вы Мне неугодны, – говорит Господь Сил, – Я не приму дар из ваших рук.

11От восхода солнца до заката Мое имя будет великим среди народов. На всяком месте Моему имени будут приносить благовония и чистые дары, потому что Мое имя будет великим среди народов, – говорит Господь Сил.

12А вы бесчестите его, говоря, что стол Владыки нечист, а пищей для него можно пренебрегать. 13Вы говорите: «Какое бремя!» – и воротите от него нос, – говорит Господь Сил.

Когда вы приводите краденый, хромой или больной скот и приносите его в жертву, почему Я должен принимать такую жертву из ваших рук? – говорит Господь. – 14Проклят обманщик, у которого в стаде есть хороший самец, которого он клянется дать, а потом приносит в жертву Владыке животное с изъяном1:14 См. Лев. 22:18-20.. Ведь Я – великий Царь, – говорит Господь Сил, – и Мое имя чтится среди народов.