Zekariya 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 8:1-23

Yehova Alonjeza Kudalitsa Yerusalemu

1Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena. 2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”

3Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”

4Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake. 5Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”

6Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo. 8Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”

9Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’ 10Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa. 11Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

12“Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa. 13Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”

14Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova, 15“Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha. 16Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu; 17musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.

18Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane. 19Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”

20Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe, 21ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’ 22Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”

23Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’ ”

New Russian Translation

Захария 8:1-23

Божьи обещания Иерусалиму

1Было ко мне слово Господа Сил:

2– Так говорит Господь Сил: Крепко возревновал Я о Сионе; Моя ревность о нем пылает, как огонь.

3Так говорит Господь: Я вернусь на Сион и буду жить в Иерусалиме. Иерусалим назовут городом истины, и гора Господа Сил назовется святой горою.

4Так говорит Господь Сил: Снова старики и старушки будут сидеть на улицах Иерусалима со старческой тростью в руках. 5Улицы города наполнятся мальчиками и девочками, играющими там.

6Так говорит Господь Сил: Если это покажется в то время невозможным для остатка народа, то должно ли это быть невозможным и для Меня? – возвещает Господь Сил.

7Так говорит Господь Сил: Я вызволю Мой народ из восточных и западных стран. 8Я верну их, чтобы им жить в Иерусалиме; они будут Моим народом, а Я буду их Богом, верным и праведным.

9Так говорит Господь Сил: Вы, кто ныне слышит из уст пророков эти слова, которые были сказаны, когда закладывались основания дома Господа Сил, пусть ваши руки будут сильными, чтобы храм был построен. 10До этого времени человеку за труд не платили, скот не кормили. Никому из странствующих не было покоя от врагов, потому что Я обратил всех людей друг против друга. 11Но с остатком народа Я не стану больше поступать, как прежде, – возвещает Господь Сил. – 12Семена будут спокойно прорастать, виноградная лоза принесет плод, земля даст урожай, и небеса будут сочиться росой. Все это Я отдам во владение остатку народа. 13Вы были проклятием среди народов, дом Иуды и дом Израиля, но Я спасу вас, и вы станете благословением. Не бойтесь; пусть ваши руки будут сильными.

14Так говорит Господь Сил: Я решил покарать вас и не миловать, когда ваши отцы вызвали Мой гнев, – говорит Господь Сил, – 15но теперь Я решил снова сделать Иерусалиму и Иудее добро. Не бойтесь. 16Вот что вам следует делать: говорите друг другу правду, судите в своих судах истинным судом – тем, который приносит мир, 17не замышляйте зла против своего ближнего и не любите клясться ложно. Все это Я ненавижу, – возвещает Господь.

18Было ко мне слово Господа Сил:

19– Так говорит Господь Сил: Посты в четвертом, пятом, седьмом и десятом месяцах8:19 Эти посты были установлены в память о следующих событиях: в четвертом месяце – врагами была пробита брешь в Иерусалимской стене (4 Цар. 25:3-4); в пятом – пал Иерусалим и был разрушен храм (4 Цар. 25:8-9); в седьмом – был убит Гедалия, назначенный Навуходоносором правитель Иудеи (4 Цар. 25:25); в десятом – начало осады Иерусалима вавилонянами (4 Цар. 25:1). станут у дома Иуды веселыми и радостными торжествами и светлыми праздниками: так что любите истину и мир.

20Так говорит Господь Сил: Еще придут многие народы и жители многих городов, 21и жители одного города пойдут в другой и скажут: «Пойдемте скорее просить Господа о милости и искать Господа Сил! А сам я уже иду». 22Многочисленные народы и сильные племена придут в Иерусалим искать Господа Сил и просить Господа о милости.

23Так говорит Господь Сил: В те дни по десять человек из всех языков и народов схватят за край одежды одного иудея и скажут: «Позволь нам идти с тобой, ведь мы слышали, что с вами Бог!»