Za Kumanga Nyumba ya Yehova
1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”
3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.
Повеление Господа о восстановлении храма
1На втором году правления царя Дария1:1 Дарий I Великий (Гистасп) правил Персидской империей с 522 по 486 гг. до н. э., в первый день шестого месяца1:1 29 августа 520 г. до н. э., Зоровавелю, сыну Шеалтиила, наместнику Иудеи, и Иисусу, сыну Иоседека, первосвященнику, было слово Господа через пророка Аггея:
2– Так говорит Господь Сил: «Этот народ говорит: „Еще не настало время строить дом Господа“».
3И было слово Господа через пророка Аггея:
4– А вам разве время жить в хороших домах, когда этот дом лежит в развалинах?
5Поэтому так говорит Господь Сил:
– Подумайте о своих путях. 6Вы посеяли много, а собрали мало. Вы едите, но не наедаетесь. Вы пьете, но не напиваетесь. Вы одеваетесь, но не в силах согреться. Вы трудитесь лишь для того, чтобы положить заработанное в дырявый кошелек.
7Так говорит Господь Сил:
– Подумайте о своих путях. 8Поднимитесь в горы, принесите дерева и постройте дом. Он будет Мне угоден, и Я прославлюсь, – говорит Господь. – 9Вы ждали многого, но получилось мало. А то, что вы принесли домой, Я развеял. За что? – возвещает Господь Сил. – За Мой дом, который лежит в развалинах, в то время как каждый из вас заботится лишь о своем доме. 10Поэтому небо над вами удержало росу, а земля удержала свой урожай. 11Я наслал засуху на поля и нагорья, на зерно, молодое вино и масло, на произведения земли, на людей, на скот и на труд ваших рук.
12И Зоровавель, сын Шеалтиила, с первосвященником Иисусом, сыном Иоседека, и со всем остальным народом послушались голоса Господа, их Бога, и слов пророка Аггея, потому что его послал Господь, их Бог. И народ устрашился Господа.
13Аггей, вестник Господа, передал народу весть от Господа:
– Я с вами, – возвещает Господь.
14И Господь пробудил дух наместника Иудеи Зоровавеля, сына Шеалтиила, дух первосвященника Иисуса, сына Иоседека, и дух всего остального народа. Они пришли и начали трудиться в храме Господа Сил, их Бога, 15в двадцать четвертый день шестого месяца второго года правления царя Дария1:15 21 сентября 520 г. до н. э..