Zekariya 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 7:1-14

Chiweruzo Cholungama ndi Chifundo, Osati Kusala Zakudya

1Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya. 2Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova 3pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”

4Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti, 5“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine? 6Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha? 7Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’ ”

8Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti, 9“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni. 10Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’

11“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve. 12Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.

13“ ‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 14‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’ ”

New Russian Translation

Захария 7:1-14

Пост лицемеров

1На четвертом году правления царя Дария, в четвертый день девятого месяца, месяца кислева7:1 7 декабря 518 г. до н. э., было слово Господне к Захарии. 2Народ Вефиля послал Сарецера и Регем-Мелеха вместе с их людьми искать у Господа расположения 3и спросить у священников дома Господа Сил и у пророков: «Скорбеть ли мне и поститься ли в пятом месяце, как я делаю это уже много лет?».

4И было ко мне слово Господне:

5– Спроси у всего народа страны и у священников: «Когда вы постились и скорбели последние семьдесят лет в пятом и седьмом месяце, то для Меня ли вы постились? 6А когда вы ели и пили, то не для самих ли себя вы пировали? 7Не те ли это слова, которыми Господь взывал через прежних пророков, когда Иерусалим с окрестными городами был населен и покоился в мире и Негев с западными предгорьями был обитаем?»

8И было к Захарии слово Господне:

9– Так говорит Господь Сил: «Судите справедливо; будьте милостивы и сострадательны друг к другу. 10Не притесняйте вдову и сироту, чужеземца и бедняка. Не замышляйте зло друг против друга».

11Но они отказались внимать; они упрямо повернулись спиной и заткнули уши, чтобы не слышать. 12Они сделали свои сердца твердыми, как кремень, чтобы не слушать Закона и слов, которые Господь Сил посылал Своим Духом через прежних пророков. И поэтому Господь Сил сильно разгневался. 13«Когда Я7:13 Букв.: «Он». звал их, они не слушали; поэтому, когда они будут звать, Я тоже не стану слушать, – говорит Господь Сил. – 14Я ураганом развеял их среди народов, которых они не знали. Страна после них осталась в таком запустении, что через нее перестали ездить. Так они привели прекрасную землю в запустение».