Yoswa 2 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 2:1-24

Rahabe ndi Anthu Ozonda Dziko

1Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.

2Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.” 3Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”

4Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera. 5Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.” 6Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo. 7Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.

8Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga 9ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu. 10Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu. 11Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi. 12Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga. 13Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”

14Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”

15Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe. 16Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”

17Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi 18tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno. 19Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu. 20Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”

21Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.

22Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza. 23Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira. 24Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

Bibelen på hverdagsdansk

Josvabogen 2:1-24

Rahab skjuler spionerne

1Fra israelitternes lejr ved Shittim på Moabs sletter havde Josva i al hemmelighed sendt to spioner af sted over floden for at undersøge landet, især Jeriko. De tog af sted og kom til et hus i Jeriko, hvor der boede en kvinde ved navn Rahab, som var prostitueret. Der fik de lov til at overnatte.

2Men da Jerikos konge fik at vide, at der var kommet nogle israelitter til byen den aften for at udspionere landet, 3sendte han straks nogle af sine folk til Rahabs hus: „Udlever de mænd, som er i dit hus,” beordrede de. „De er spioner.”

4Rahab havde allerede skjult mændene, så hun svarede: „Der kom ganske rigtig to mænd til mit hus, men jeg vidste ikke, hvor de kom fra. 5De er her ikke længere, for de forlod byen inden solnedgang, da byporten skulle lukkes. Jeg ved ikke, hvor de tog hen, men hvis I skynder jer, kan I sikkert nå at indhente dem.” 6Rahab havde ført mændene op på det flade tag og gemt dem under noget hør, hun havde liggende til tørre deroppe.

7Kongens mænd skyndte sig af sted i retning af Jordanflodens vadesteder, og byporten blev lukket forsvarligt, så snart de var taget af sted.

8Imens gik Rahab op på taget for at tale med mændene, inden de lagde sig til at sove. 9„Jeg ved, at Herren har givet jer vores land,” sagde hun. „Vi er alle sammen frygtelig bange for jer. 10Vi har jo hørt, hvordan Herren åbnede en vej for jer gennem Det Røde Hav, dengang I forlod Egypten. Vi ved også, hvordan det gik amoritterkongerne Sihon og Og på den anden side af Jordanfloden, da I ødelagde deres land og udryddede befolkningen. 11Så det er ikke underligt, at vi har tabt modet. Ingen tør kæmpe imod jer, når de ved, at Herren, jeres Gud, er den øverste Gud i Himlen og på jorden. 12-13Derfor vil jeg bede jer om én ting: Sværg ved jeres Guds hellige navn, at I vil hjælpe mig og min familie, ligesom jeg nu hjælper jer. Giv mig et sikkert tegn på, at I vil skåne mig og min mor og far, mine brødre og søstre og deres familier, så vi ikke skal dø, når I erobrer Jeriko.”

14„Liv for liv!” svor mændene. „Hvis du ikke forråder os, vil vi sørge for, at du og din familie bliver skånet, når Herren giver os sejr over jeres land.”

15Rahabs hus var bygget i ét med bymuren og havde et vindue, der vendte udad. Hun tog nu et reb og gjorde klar til at fire dem ned på ydersiden af bymuren. 16„Gå væk fra floden og op i bjergene,” sagde hun til dem, „og gem jer der i tre dage, indtil jeres forfølgere giver op og kommer tilbage til byen. Så kan I roligt vende hjem.”

17-18Inden spionerne forsvandt, sagde de: „Den ed, du har fået os til at sværge, gælder kun, hvis du binder den her røde snor fast i vinduet, og hvis I alle holder jer inden døre. 19Hvis nogen forlader huset her, er det deres egen skyld, hvis de mister livet. Men vi står inde for, at der ikke vil ske noget med dem, der bliver i huset. 20Hvis du forråder os, er vi løst fra vores løfte.”

21„Det er i orden,” svarede hun. Derpå firede hun dem ned, og de forsvandt i mørket, mens hun bandt den røde snor fast i vinduet.

22Spionerne flygtede nu op i bjergene, hvor de blev i tre dage, mens deres forfølgere søgte efter dem overalt og siden vendte tilbage til byen med uforrettet sag. 23Derefter gik de ned fra bjergene, vadede over Jordanfloden og fortalte Josva, hvordan det var gået. 24„Herren har givet os hele landet,” sagde de. „Befolkningen er så bange for os, at de ryster af skræk.”