Deuteronomo 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 1:1-46

Mose Akumbutsa Aisraeli za ku Horebu

1Awa ndi mawu amene Mose anayankhula kwa Aisraeli onse mʼchipululu kummawa kwa Yorodani, ku Araba moyangʼanana ndi Sufi, pakati pa Parani ndi Tofeli, Labani, Heziroti ndi Dizahabu. 2(Kuyenda kuchokera ku Horebu kukafika ku Kadesi Barinea kudzera njira ya ku Phiri la Seiri ndi ulendo wa masiku khumi ndi limodzi).

3Mʼchaka cha makumi anayi, pa tsiku loyamba la mwezi 11, Mose anafotokozera Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamula zokhudza iwowo. 4Apa nʼkuti atagonjetsa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni, ndipo pa Ederi anagonjetsa Ogi mfumu ya ku Basani, amene amalamulira mu Asiteroti.

5Chakummawa kwa Yorodani mʼchigawo cha Mowabu, Mose anayamba kufotokozera lamulo ili kunena kuti:

6Ku Horebu, Yehova Mulungu wathu anati kwa ife, “Mwakhalitsa pa phiri lino. 7Sasulani msasa ndipo pitani ku dziko la mapiri la Aamori. Pitani kwa anthu onse oyandikana nawo ku Araba, ku mapiri, mʼmbali mwa mapiri a ku madzulo, ku Negevi ndiponso mʼmbali mwa nyanja, ku dziko la Akanaani ndi ku Lebanoni mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 8Taonani, Ine ndakupatsani dziko ili. Lowani ndi kulilanda dziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo komanso kwa zidzukulu zawo.”

Kukhazikitsa Atsogoleri

9Pa nthawi imeneyi ine ndinati kwa inu, “Inu ndinu katundu olemera kwambiri woti sindingathe kumunyamula ndekha. 10Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani kotero kuti lero lino ndinu ochuluka ngati nyenyezi za kumwamba. 11Yehova Mulungu wa makolo anu wachulukitsa chiwerengero chanu ndipo wakudalitsani monga momwe analonjezera! 12Koma nanga ndekha ndidzasenza bwanji zovuta ndi zipsinjo zanu komanso milandu yanu? 13Sankhani amuna ena anzeru, ozindikira ndi amene mumawalemekeza kuchokera ku mtundu uliwonse wa mitundu yanu, ndipo ndidzawayika kuti akulamulireni.”

14Inu munandiyankha kuti, “Maganizo amenewa ndi abwino kuwachita.”

15Choncho ndinatenga anthu otsogolera mafuko anu, anzeru ndi omwe mumawalemekeza, ndipo ndinawayika kuti azikulamulirani mʼmagulu a 1,000, ena 100, ena makumi asanu ndi ena khumi, kuti akhalenso ngati akapitawo a mafuko. 16Ndipo pa nthawi imeneyo ndinawawuza olamula anu kuti, “Muzimva milandu ya pakati pa abale anu ndi kuweruza mosakondera, kaya mlanduwo uli pakati pa Aisraeli okhaokha kapena mmodzi wa iwo ndi mlendo. 17Osamayangʼana nkhope poweruza koma muzimvetsera aangʼono ndi aakulu omwe chimodzimodzi. Musamaope munthu aliyense, pakuti chiweruzo ndi cha Mulungu. Muzindibweretsera mlandu uliwonse wovuta ndipo ndidzaumva.” 18Ndipo nthawi imeneyo ndinakuwuzani chilichonse chimene munayenera kuchita.

Atumizidwa Kukazonda Dziko

19Tsono monga Yehova Mulungu wathu anatilamulira, tinanyamuka kuchoka ku Horebu ndi kupita cha ku dziko lamapiri la Aamori kudzera ku chipululu chachikulu ndi choopsa chija munachionachi, kotero kuti tinakafika ku Kadesi Barinea. 20Ndipo ndinati kwa inu, “Mwafika ku dziko la mapiri la Aamori, limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa. 21Taonani, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dzikoli. Pitani ndi kulitenga monga Yehova, Mulungu wa makolo anu anakuwuzirani. Musaope kapenanso kugwa mphwayi.”

22Tsono nonse munabwera kwa ine ndi kuti, “Tiyeni titumize anthu ayambe apita kuti akazonde dzikolo ndi kutibweretsera mawu pa za njira yomwe tidzere ndi za mizinda imene tikafikireko.”

23Ndinaona kuti maganizo amenewa anali abwino, choncho ndinasankha anthu khumi ndi awiri, mmodzi ku fuko lililonse. 24Iwo ananyamuka napita mʼdziko la mapiri, ndipo anafika ku Chigwa cha Esikolo ndi kukazonda dzikolo. 25Pobwerera anatitengerako zipatso za mʼdzikomo ndipo anatipatsa mawu akuti, “Dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa ndi labwino.”

Awukira Yehova

26Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu. 27Inu munanyinyirika mʼmatenti anu nʼkumati, “Mulungu amatida nʼchifukwa chake anatitulutsa ku Igupto kuti atipereke mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge. 28Tigwire mtengo wanji? Abale athu anatitayitsa mtima. Iwo akuti, ‘Anthuwo ndi amphamvu ndi aatali kuposa ife, mizindayo ndi yayikulu ndipo mipanda yake ndi yayitali yofika kumwamba. Ife tinaonanso Aanaki kumeneko.’ ”

29Ndipo ine ndinati kwa inu, “Musachite mantha kapena kuwaopa. 30Yehova Mulungu wanu, amene akukutsogolerani, adzakumenyerani nkhondo monga muja anachitira ku Igupto inu mukuona, 31ndi mʼchipululu muja. Kumeneko munaona mmene Yehova Mulungu wanu anakunyamulirani monga abambo anyamulira mwana wawo, njira yonse yomwe munayenda mpaka munafika pamalo ano.”

32Ngakhale zinali choncho, simunadalire Yehova Mulungu wanu 33amene anakutsogolerani pa ulendo wanu, ndi moto nthawi ya usiku ndi mtambo nthawi ya masana, kukufunirani malo woti mumange msasa ndi kukuonetsani njira yoti muyendemo.

34Yehova atamva zimene munanena anakwiya nalumbira kuti, 35“Palibe ndi mmodzi yemwe mwa mʼbado woyipawu amene adzaona dziko labwino limene ndinalumbira kupatsa makolo anu, 36kupatula Kalebe mwana wa Yefune. Iye adzaliona, ndipo ndidzamupatsa iye ndi adzukulu ake, dziko limene adzapondamo popeza anatsata Yehova ndi mtima wake wonse.”

37Chifukwa cha inu, Yehova anakwiyiranso ine ndipo anati, “Iwenso sudzalowa mʼdzikomo. 38Koma Yoswa mwana wa Nuni amene amakuthandiza, adzalowa mʼdzikomo. Umulimbikitse chifukwa adzatsogolera Israeli kukalandira dzikolo. 39Ndipo angʼonoangʼono amene munati adzagwidwa ukapolo, ana anu amene sanadziwe kusiyanitsa chabwino ndi choyipa, amenewo adzalowa mʼdzikolo. Ndidzalipereka kwa iwo ndipo lidzakhala lawo. 40Koma inu, tembenukani nyamukani kulowera cha ku chipululu kutsatira njira ya ku Nyanja Yofiira.”

41Ndipo inuyo munati, “Tachimwa pamaso pa Yehova. Tipita ndi kukachita nkhondo monga Yehova Mulungu wathu watilamulira.” Choncho aliyense wa inu anavala zankhondo, ndi kuganiza kuti nʼkosavuta kupita mʼdziko la mapiri lija.

42Koma Yehova anandiwuza kuti, “Awuze anthuwa kuti, ‘Musapite kukachita nkhondo chifukwa Ine sindidzakhala nanu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu.’ ”

43Choncho ndinakuwuzani koma simunamve. Inu munawukira lamulo la Yehova ndipo mwamwano munayenda kulowa mʼdziko la mapiri. 44Aamori amene ankakhala mʼmapiriwo anatuluka kukakumana nanu ndipo anakuthamangitsani ngati gulu la njuchi ndipo anakukanthani kuchokera ku Seiri, njira yonse mpaka ku Horima. 45Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni. 46Pamenepo munakhala ku Kadesi masiku ambiri kwa nthawi yayitali ndithu.

Bibelen på hverdagsdansk

5. Mosebog 1:1-46

Indledning

1I denne bog er de ord nedskrevet, som Moses talte til Israels folk, mens de opholdt sig på Moabs ubeboede sletter øst for Jordanfloden, omkranset af byerne Suf, Paran, Tofel, Laban, Hatzerot og Di-Zahab. 2Stedet ligger 11 dagsrejser fra Horebs bjerg1,2 I 5. Mosebog og til dels i 2. Mosebog omtales Guds bjerg i Sinaiørkenen som Horebs bjerg i stedet for Sinaibjerget. via Kadesh-Barnea og Seirs bjerge, 3og det var nu 40 år siden, israelitterne rejste fra Egypten. På den første dag i den 11. måned i det 40. år holdt Moses følgende tale. 4Det var efter, at han havde overvundet amoritterkongen Sihon fra Heshbon og i Edrei havde slået kong Og af Bashan fra Ashtarot. 5I talen nævnes de love, som Herren havde befalet ham at give videre til Israels folk.

Tilbageblik på vandringen fra Sinai til det lovede land

6„Herren, vores Gud, talte til os ved Horebs bjerg,” begyndte Moses. „Dengang sagde han til os: ‚Nu er det på tide, at I forlader dette bjerg 7og går ind og erobrer amoritternes bjergland og nabofolkenes landområder i Arabadalen1,7 Araba er navnet på den del af Rift Valley, som går fra Eilat ved Det Røde Hav til Libanons bjerge. Gennem denne dalsænkning flyder Jordanfloden og her ligger Galilæasøen og Det Døde Hav. , i Negev ørkenen, i kana’anæernes højland, bakkeskråningerne mod vest og kystområderne, ja helt op til Eufratfloden mod nord, inklusive Libanons land. 8Gå ind og tag hele det land i besiddelse, som jeg lovede jeres forfædre, Abraham, Isak og Jakob.’

9Dengang sagde jeg til Israels folk: ‚Jeg kan ikke bære så stort et ansvar alene. 10Herren har gjort jer til et stort folk, så talrige som stjernerne på himlen. 11Må Herren, jeres fædres Gud, gøre jer 1000 gange så talrige, som I er nu, og velsigne jer, sådan som han har lovet. 12Men det er en uoverkommelig opgave for mig at være alene om at afgøre jeres retssager og stridsspørgsmål. 13Derfor skal hver enkelt stamme udvælge nogle vise, erfarne og forstandige mænd, som jeg kan indsætte som jeres ledere.’

14Det forslag accepterede de, 15hvorefter jeg indsatte de mænd, der blev valgt, som dommere og administrative ledere, nogle med ansvar for 1000, andre med ansvar for 100, for 50 eller for 10. 16Jeg indprentede dem, at alle skulle være lige for loven, også de fremmede, og at de skulle lade begge parter komme til orde og derefter dømme retfærdigt. 17‚Når I afsiger dom,’ forklarede jeg dem, ‚skal alle behandles ens, hvad enten de er rige eller fattige. Sørg for at yde alle samme retfærdighed. I må ikke frygte for nogen, for I dømmer på Guds vegne, og hvis en sag er for vanskelig til, at I kan træffe en afgørelse, skal I komme til mig med den, så jeg kan overtage den.’ 18Ved den lejlighed gav jeg også folket instrukser vedrørende mange andre ting.

19På Herrens befaling forlod vi så Horeb og rejste gennem den store og forfærdelige ørken, som I selv har oplevet eller hørt om, indtil vi nåede til Kadesh-Barnea på grænsen til amoritternes land. 20Da sagde jeg til folket: ‚Nu er vi kommet til det land, som Herren, vores Gud, vil give os, 21og han vil hjælpe os med at erobre det. Vær derfor ikke bange, men vær ved godt mod og gør, som han har befalet jer at gøre.’

22De svarede: ‚Lad os først sende nogle spioner ind i landet, så vi kan se, hvilken rute der er den bedste, og hvilke byer vi først skal indtage.’

23Jeg gik ind på forslaget og udvalgte 12 spioner, en fra hver stamme. 24De drog ind i bjerglandet og nåede til Eshkoldalen, som de undersøgte grundigt. 25Derfra vendte de tilbage med noget af landets frugt. De var enige om, at det var et godt og frugtbart land, som Herren, vores Gud, ville give os. 26Men folket turde alligevel ikke gå ind i landet og satte sig dermed op imod Herrens befaling.

27I stedet begyndte de at beklage sig i deres telte. ‚Herren hader os,’ klagede de. ‚Han har ført os den lange vej fra Egypten, men kun for at udlevere os til amoritterne, så de kan slå os ihjel. 28Hvad er det dog, vi har indladt os på?’ Spionerne tog modet fra folket ved at berette om landets indfødte, der var langt højere og stærkere end os, og om deres befæstede byer, hvis mure nåede til himlen! De fortalte tilmed, at de havde set anakitiske1,28 Anakitterne var en slægt af kæmper, der nedstammede fra Anak, jf. 4.Mos. 13,22. kæmper i landet.

29Men jeg opfordrede dem til ikke at være bange. 30‚Det er Herren, jeres Gud, som er jeres leder,’ sagde jeg. ‚Han vil gå foran jer og gøre store undere for øjnene af jer, nøjagtig som han gjorde i Egypten. 31Har I allerede glemt, hvordan han bar jer på sine arme hele vejen gennem ørkenen som en far, der bærer sin søn?’

32Men folket ville stadig ikke adlyde. De nægtede at tro på Herren, deres Gud, 33som førte dem fra sted til sted ved hjælp af en sky om dagen og en ildsky om natten og viste dem de bedste steder at slå lejr i ørkenen.

34Da blev Herren vred over deres beklagelser. Han svor, 35at ikke en eneste af hele den ulydige og vantro generation skulle få lov at opleve det gode land, han havde lovet deres forfædre, 36undtagen Kaleb, der som belønning for sin tro og lydighed fik lovning på den jord, han som en af de 12 spioner havde betrådt.

37Selv mig blev Herren vred på, og det var folkets skyld. Herren sagde til mig: ‚Heller ikke du får lov at komme ind i landet, 38men din medhjælper Josva skal i dit sted føre folket ind. Derfor skal du styrke og opmuntre ham til at overtage din plads. 39Jeg vil senere give landet til de børn, som man påstod ville blive taget til fange og gjort til slaver, 40men I skal nu vende om og gå tilbage gennem ørkenen mod Det Røde Hav.’

41Så kom de straks på andre tanker: ‚Vi har syndet imod Herren!’ sagde de. ‚Men nu vil vi gerne gå ind i landet og kæmpe, sådan som Herren, vores Gud, har sagt.’ Derpå greb de til våben i den tro, at de med lethed kunne erobre hele området.

42Men Herren sagde til mig: ‚Sig til dem, at de skal lade være, for jeg har ikke i sinde at hjælpe dem, og de vil blive hugget ned af deres fjender.’

43Jeg fortalte dem, hvad Herren havde sagt, men de ville stadig ikke høre efter. De trodsede Herrens ord og rykkede ind i bjerglandet. 44Amoritterne gik til modangreb og jagtede dem som bier, så der lå faldne hele vejen fra Seir til Horma. 45De, der vendte hjem, græd for Herrens ansigt, men nu var det Herren, der ikke ville lytte til dem. 46Derfor var de tvunget til at blive i Kadesh i længere tid.