Yehova Asankha Yoswa Kukhala Mtsogoleri
1Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose: 2“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse. 3Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose. 4Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo. 5Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa. 7Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana. 8Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana. 9Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti, 11“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’ ”
12Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti, 13“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’ 14Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza. 15Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita. 17Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose. 18Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Herrens løfte til Josva
1Efter at Moses var død, sagde Herren til hans medhjælper Josva, Nuns søn:
2„Min tjener Moses er død. Nu er det dig, som skal føre israelitterne over Jordanfloden og ind i det land, jeg vil give dem. 3Hvad jeg sagde til Moses, siger jeg til dig: De områder, I erobrer i landet, skal tilhøre jer, 4fra Negevs ørken i syd til Libanons bjerge mod nord, ja, helt op til den store flod, Eufratfloden, og ud til Middelhavet mod vest, hele det land, hittitterne nu bor i. 5Ingen vil kunne holde stand imod dig, så længe du lever, for jeg vil være med dig, som jeg var med Moses. Jeg vil ikke svigte dig eller forlade dig.
6Stå fast og vær modig, for du skal lede mit folk i erobringen af hele det land, jeg har lovet jeres forfædre. 7Ret dig omhyggeligt efter de forordninger, Moses gav dig. Hold fast ved dem, så vil tingene lykkes for dig. 8Mind hele tiden folket om disse love—og selv skal du tænke på dem døgnet rundt, så du handler efter dem, for så vil det gå dig godt, og du vil lykkes. 9Jeg siger det igen: Stå fast og vær modig! Vær ikke bange eller frygtsom! Husk, at jeg er Herren, din Gud, og jeg vil hjælpe dig med alt, hvad du skal gøre.”
Josva befaler folket at gøre sig klar
10Så sagde Josva til folkets ledere: 11„Gå rundt i lejren og sig til folket: Gør jer klar, for om tre dage går vi over Jordanfloden for at tage det land i besiddelse, som Gud har lovet os.”
12Til lederne for Rubens, Gads og Manasses halve stamme sagde han: 13„Husk, hvad Guds tjener Moses sagde til jer: Herren, jeres Gud, har givet jer landet øst for Jordanfloden. 14Jeres koner, børn og kvæg har lov at blive her på østsiden, men alle våbenføre mænd skal gå over Jordanfloden i spidsen for de andre stammer og hjælpe dem med at indtage deres områder på den anden side. 15I skal kæmpe sammen med dem, indtil de har erobret det land, Herren har givet dem. Derefter må I vende tilbage og bosætte jer øst for Jordanfloden, hvor Moses tildelte jer land.”
16„Alt, hvad du siger, vil vi gøre,” svarede de. „Og hvor som helst, du sender os, vil vi gå. 17Vi vil adlyde dig, som vi adlød Moses. Må Herren din Gud være med dig, som han var med Moses. 18Enhver, der ikke vil adlyde dig, skal dø. Stå fast og vær modig.”