Yohane 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 1:1-51

Mawu Asandulika Thupi

1Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu. 2Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.

3Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa. 4Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu. 5Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.

6Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane. 7Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire. 8Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika. 9Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.

10Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye. 11Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye. 12Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu; 13ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.

14Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.

15Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’ ” 16Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso. 17Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu. 18Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.

Yohane Mʼbatizi Akana kuti Iye ndi Khristu

19Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani. 20Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”

21Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?”

Iye anati, “Sindine.”

“Kodi ndiwe Mneneri?”

Iye anayankha kuti, “Ayi.”

22Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”

23Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’ ”

24Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa 25anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”

26Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa. 27Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”

28Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.

Yesu Mwana Wankhosa wa Mulungu

29Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi! 30Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’ 31Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”

32Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye. 33Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’ 34Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”

Ophunzira Oyamba a Yesu

35Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake. 36Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”

37Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu. 38Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?”

Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”

39Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.”

Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.

40Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu. 41Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).

42Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).

Yesu Ayitana Filipo ndi Natanieli

43Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”

44Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida. 45Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”

46Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?”

Filipo anati, “Bwera udzaone.”

47Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”

48Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?”

Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”

49Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”

50Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.” 51Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

New Russian Translation

Иоанна 1:1-51

Слово становится Человеком

1В начале было Слово1:1 Слово – одно из имен Иисуса Христа (см. 1:14; Отк. 19:13).,

и Слово было с Богом,

и Слово было Богом.

2Оно было в начале с Богом.

3Все, что существует,

было сотворено через Него,

и без Него ничто из того, что есть,

не начало существовать.

4В Нем заключена жизнь,

и эта жизнь – Свет человечеству.

5Свет светит во тьме,

и тьма не поглотила1:5 Или: «не поняла». Его.

6Богом был послан человек по имени Иоанн. 7Он пришел как свидетель, свидетельствовать о Свете, чтобы благодаря ему все поверили в Этот Свет. 8Сам он не был Светом, но пришел, чтобы свидетельствовать о Свете.

9Был истинный Свет,

Который просвещает каждого человека,

приходящего в мир1:9 Или: «Был истинный Свет, приходящий в мир, Который просвещает каждого человека»..

10Он был в мире, который через Него был создан,

но мир не узнал Его.

11Он пришел к Своим,

но Свои не приняли Его.

12Но всем тем, кто Его принял

и кто поверил в Его имя,

Он дал власть стать детьми Божьими –

13детьми, рожденными не от крови,

не от желаний или намерений человека,

а рожденными от Бога.

14Слово стало Человеком1:14 Букв.: «плотью».

и жило среди нас.

Мы видели Его славу,

славу, которой наделен единственный Сын Отца,

полный благодати и истины.

15Иоанн свидетельствовал о Нем, провозглашая:

– Это Тот, о Ком я говорил: «Идущий за мной – выше меня, потому что Он существовал еще до меня».

16По Его безграничной благодати

мы все получили одно благословение за другим.

17Ведь через Моисея был дан Закон,

а благодать и истина пришли через Иисуса Христа.

18Бога никто никогда не видел,

Его явил нам единственный Сын Его,

пребывающий у самого сердца Отца,

и Который Сам – Бог.

Иоанн Креститель объявляет о цели своего служения

(Мат. 3:1-12; Мк. 1:2-8; Лк. 3:1)

19И вот свидетельство Иоанна. Когда предводители иудеев1:19 В Евангелии от Иоанна термин «иудеи» относится, в первую очередь, к предводителям иудеев, которые противились Иисусу. Читателю нужно иметь эту косвенную информацию в виду, когда термин «иудеи» встречается в этой книге. послали к Иоанну священников и левитов, чтобы спросить его, кто он такой, 20он сказал им прямо, не скрывая:

– Я не Христос.

21Они спросили его:

– Тогда кто же ты? Илия?

Он ответил:

– Нет.

– Так ты Пророк?1:21 Имеется в виду Пророк, о Котором говорил Моисей (см. Втор. 18:15, 18). Ср. Деян. 3:18-24.

– Нет, – отвечал Иоанн.

22– Кто же ты? – спросили они тогда. – Скажи, чтобы мы смогли передать твой ответ тем, кто нас послал. Что ты сам скажешь о себе?

23Иоанн ответил им словами пророка Исаии:

– «Я голос, который раздается в пустыне: выпрямите путь для Господа»1:23 Ис. 40:3..

24А посланные были фарисеями. 25Они допытывались:

– Если ты не Христос, не Илия и не Пророк, то почему ты крестишь?

26Иоанн ответил:

– Я крещу водой. Но среди вас стоит Тот, Кого вы не знаете. 27Он Тот, Кто придет после меня, и я даже не достоин развязать ремни Его сандалий.

28Это происходило в Вифании1:28 Вифания – точное расположение не установлено (не следует путать с Вифанией близ Иерусалима, см., напр., 11:1)., на восточном берегу реки Иордана, там, где крестил Иоанн.

Иоанн Креститель объявляет Иисуса Христом

29На следующий день Иоанн увидел идущего к нему Иисуса и сказал:

– Вот Божий Ягненок, Который заберет грех мира! 30Это о Нем я говорил: «Тот, Кто идет за мной, – выше меня, потому что Он существовал еще до меня». 31Я сам не знал, кто Он, но я крещу водой для того, чтобы Он был явлен Израилю.

32И Иоанн подтвердил свои слова:

– Я видел, как Дух спускался на Него с небес в образе голубя и как Он остался на Нем. 33Я бы не узнал Его, если бы Пославший меня крестить водой не сказал мне: «На Кого опустится и на Ком останется Дух, Тот и будет крестить людей Святым Духом». 34Я видел это и свидетельствую, что Он – Сын Бога!

Первые ученики Иисуса

(Мат. 4:18-22; Мк. 1:16-20; Лк. 5:2-11)

35На следующий день Иоанн опять стоял с двумя своими учениками. 36Увидев идущего Иисуса, он сказал:

– Вот Ягненок Божий!

37Оба ученика, услышав эти слова, последовали за Иисусом. 38Иисус обернулся и увидел, что они идут за Ним.

– Что вы хотите? – спросил Он.

– Рабби (что значит «учитель»), скажи, где Ты живешь? – спросили они.

39– Идите за Мной, и вы сами увидите, – сказал Иисус.

Было около десятого часа1:39 То есть около четырех часов пополудни.. Они пошли, увидели, где Он живет, и пробыли у Него до вечера того дня1:39 Или: «Они пошли, увидели, где Он живет, и пробыли у Него до десятого часа (четырех часов дня)»..

40Одним из двух, слышавших слова Иоанна об Иисусе и пошедших за Ним, был брат Симона Петра, Андрей. 41Он разыскал своего брата Симона и сказал:

– Мы нашли Мессию! (Это значит «Помазанник»1:41 «Помазанник» («Машиах» (евр.), «Христос» (греч.)) – праведный Царь и Освободитель, Спаситель, обещанный Богом еще в Законе, Псалмах и в Книге Пророков..)

42И привел его к Иисусу. Иисус посмотрел на Симона и сказал:

– Симон, сын Иоанна1:42 В более поздних рукописях Евангелия от Иоанна: «сын Ионы» (также в ст. 21:15, 16, 17)., тебя будут звать Кифа (что значит «камень», а по-гречески «Петр»).

Иисус призывает Филиппа и Нафанаила

43На следующий день Иисус решил идти в Галилею. Он нашел Филиппа и сказал ему:

– Следуй за Мной!

44Филипп был из Вифсаиды, из того же города, что и Андрей с Петром. 45Он нашел Нафанаила и сказал ему:

– Мы встретили Того, о Ком написано в Законе Моисея и о Ком писали пророки. Это Иисус, сын Иосифа1:45 Сын Иосифа – по закону Иосиф, как муж Марии, считался отцом Иисуса, хотя не был им биологически (см. Лк. 1:35; 3:23). из Назарета.

46Нафанаил ответил:

– Разве из Назарета может быть что-нибудь доброе?

– Пойди и посмотри, – сказал Филипп.

47Когда Иисус увидел идущего к Нему Нафанаила, Он сказал:

– Вот истинный израильтянин, в котором нет ни тени притворства.

48– Откуда Ты меня знаешь? – удивился Нафанаил.

Иисус ответил:

– Еще до того, как Филипп позвал тебя, Я видел тебя под инжиром.

49Тогда Нафанаил сказал:

– Рабби, Ты действительно Сын Бога, Ты Царь Израиля!

50Иисус сказал:

– Ты говоришь это потому, что Я сказал, что видел тебя под инжиром. Ты увидишь еще больше этого.

51И добавил:

– Говорю вам истину, вы увидите открытые небеса и ангелов Божьих, спускающихся и поднимающихся к Сыну Человеческому.