Luka 24 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 24:1-53

Yesu Auka kwa Akufa

1Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda. 2Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika 3ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu. 4Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo. 5Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa? 6Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya: 7‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’ ” 8Ndipo anakumbukira mawu ake.

9Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse. 10Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi. 11Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru. 12Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.

Zochitika pa Njira ya ku Emau

13Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu. 14Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo. 15Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi; 16koma iwo sanamuzindikire.

17Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?”

Iwo anayima ndi nkhope zakugwa. 18Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”

19Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?”

Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse. 20Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye; 21koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi. 22Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa 23koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo. 24Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”

25Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena! 26Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?” 27Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.

28Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira. 29Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.

30Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira. 31Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo. 32Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”

33Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi 34ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.” 35Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira

36Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”

37Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa. 38Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu? 39Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”

40Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake. 41Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?” 42Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika. 43Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.

44Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”

45Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba. 46Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu. 47Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu. 48Inu ndinu mboni za zimenezi. 49Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”

Kupita Kumwamba

50Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa. 51Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba. 52Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu. 53Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.

New Russian Translation

Луки 24:1-53

Воскресение Иисуса из мертвых

(Мат. 28:1-8; Мк. 16:1-8; Ин. 20:1-8)

1Рано утром в первый день недели24:1 У иудеев неделя начиналась с воскресенья., женщины, взяв приготовленные душистые мази, пришли к гробнице. 2Здесь они обнаружили, что камень от входа в гробницу отвален. 3Войдя внутрь, они не нашли тела Господа Иисуса. 4Стоя в недоумении, они увидели, что рядом с ними вдруг появились два человека24:4 Два человека – т. е. ангелы (см. 24:23). в сияющих одеждах. 5В испуге женщины опустили свои лица к земле, но те сказали им:

– Что вы ищете живого среди мертвых? 6Его здесь нет, Он воскрес! Вспомните, что Он говорил вам еще в Галилее: 7«Сын Человеческий должен быть предан в руки грешников, распят, и на третий день воскреснуть».

8Тогда они вспомнили слова Иисуса 9и, вернувшись от гробницы, рассказали обо всем одиннадцати и всем остальным. 10Среди тех, кто рассказал это апостолам, были Мария Магдалина, Иоанна, Мария – мать Иакова и другие женщины. 11Но они не поверили рассказу женщин, им казалось, что это лишь пустые слова. 12Петр, однако же, побежал к гробнице. Он наклонился, заглянул внутрь и увидел только льняные полотна. Он вернулся к себе, удивляясь всему случившемуся.

Иисус является ученикам на дороге в Эммаус

13В тот же день двое из учеников шли в селение Эммаус, что расположено в шестидесяти стадиях24:13 То есть 11 км. от Иерусалима, 14и говорили обо всем, что произошло. 15И когда они разговаривали и спорили, вдруг Сам Иисус подошел и присоединился к ним, 16но они были словно в ослеплении и не узнали Его. 17Иисус спросил их:

– О чем это вы говорите между собой по дороге?

Они остановились с печальными лицами. 18Один из них, которого звали Клеопа, ответил:

– Ты, видно, единственный из пришедших в Иерусалим, кто не знает о том, что произошло в эти дни.

19– О чем? – спросил Он.

– О том, что произошло с Иисусом из Назарета, – ответили они. – Он был пророком, сильным перед Богом и перед людьми в словах и делах. 20Первосвященники и наши вожди осудили Его на смерть и распяли. 21А мы надеялись, что Он Тот, Кто должен освободить Израиль. Но вот уже третий день, как все это произошло. 22Однако некоторые из наших женщин удивили нас. Они пошли сегодня рано утром к гробнице 23и, не найдя там Его тела, вернулись и рассказали нам, что им явились ангелы и сказали, что Он жив. 24Потом некоторые из наших друзей пошли к гробнице и нашли там все, как рассказали женщины, но Его они не видели.

25Иисус сказал им:

– Как же вы глупы, как медленно вы соображаете, чтобы верить всему, что предсказали пророки! 26Разве не должен был Христос пройти через все эти страдания и затем войти в Свою славу?

27И начав от Моисея и всех пророков, Он объяснил им, что было сказано о Нем во всех Писаниях. 28Когда они подходили к селению, Иисус сделал вид, что хочет идти дальше, 29но они стали уговаривать Его:

– Останься с нами, ведь уже вечер, день почти окончился.

И Он вошел в дом и остался с ними. 30За столом Иисус взял хлеб, благословил его, разломил и дал им. 31Тогда их глаза открылись, и они узнали Его. Но Он стал невидим для них. 32Они стали говорить друг другу:

– Разве не горело в нас сердце, когда Он говорил с нами по дороге и объяснял нам Писания?!

33Они встали и сразу же пошли обратно в Иерусалим. Там они нашли одиннадцать и тех, кто был вместе с ними. 34Те сказали им, что Господь действительно воскрес и явился Симону. 35Затем эти двое рассказали все, что произошло с ними по дороге, и то, как они узнали Иисуса, когда Он разламывал хлеб.

Явление Иисуса ученикам

(Ин. 20:19-23)

36Они еще говорили, когда Иисус Сам появился среди них и сказал:

– Мир вам!

37Они замерли в испуге, думая, что видят призрак. 38Он же сказал им:

– Что вы так испуганы? Почему вы сомневаетесь? 39Посмотрите на Мои руки и на Мои ноги. Это же Я! Потрогайте Меня и рассмотрите. У духов ведь не бывает ни тела, ни костей, а у Меня, как видите, есть.

40Сказав это, Он показал им Свои руки и ноги. 41Но они, радуясь и изумляясь, еще не могли поверить. Тогда Иисус спросил их:

– У вас есть что-нибудь поесть?

42Они дали Ему печеной рыбы. 43Он взял и ел перед ними.

44– Об этом Я и говорил вам, когда был еще с вами, – сказал Он. – Все записанное обо Мне в Законе Моисея, у Пророков и в Псалмах должно исполниться.

45Затем Он раскрыл их умы к пониманию Писаний.

46– Написано, что Христос должен пострадать и на третий день воскреснуть из мертвых, – сказал Он им. 47– Во имя Его всем народам, начиная от Иерусалима, будет проповедано покаяние и прощение грехов. 48Вы свидетели этому. 49Я же пошлю вам обещанное Моим Отцом, но пока вы не получите силу свыше, оставайтесь в городе.

Вознесение Иисуса

(Мк. 16:19-20; Деян. 1:9-11)

50Потом Он вывел их из города до Вифании и, подняв руки, благословил их. 51И в то время как Он благословлял их, Он стал отдаляться от них и поднялся на небеса. 52Ученики поклонились Ему и, безмерно радуясь, возвратились в Иерусалим, 53где постоянно находились в храме, славя Бога.