Marko 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 1:1-45

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

1Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu, 2monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya:

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu,

amene adzakonza njira yanu,”

3“Mawu a wofuwula mʼchipululu,

‘Konzani njira ya Ambuye,

wongolani njira zake.’ ”

4Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo. 5Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani. 6Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo. 7Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake. 8Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”

Kubatizidwa ndi Kuyesedwa kwa Yesu

9Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani. 10Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda. 11Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”

12Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu, 13ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.

Yesu Alengeza za Uthenga Wabwino

14Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati, 15“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

16Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi. 17Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 18Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

19Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo. 20Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

21Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa. 22Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo. 23Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti, 24“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

25Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!” 26Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.

27Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.” 28Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

29Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya. 30Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye. 31Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.

32Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda. 33Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo, 34Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.

Yesu Apemphera Kumalo a Yekha

35Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera. 36Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye, 37ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”

38Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.” 39Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.

Yesu Achiritsa Wakhate

40Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

41Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” 42Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.

43Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti, 44“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.” 45Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

New Russian Translation

Марка 1:1-45

Иоанн Креститель готовит путь Иисусу

(Мат. 3:1-12; Лк. 3:2-16; Ин. 1:19-28)

1Вот начало Радостной Вести1:1 Букв.: «Евангелия». об Иисусе Христе, Сыне Бога. 2Как написано у пророка Исаии:

«Вот, Я посылаю перед Тобой Моего вестника,

который приготовит Тебе путь»1:2 См. Мал. 3:1..

3«Голос раздается в пустыне:

„Приготовьте путь Господу1:3 Слово, стоящее в греческом тексте, является переводом еврейского «ЙГВГ» (Ис. 40:3). Это имя, под которым Бог открылся Моисею и народу Израиля (см. Исх. 3:13-15). Оно переводится как «Он Есть», показывая неизменность Его природы и характера (см. Пс. 101:26-28).,

сделайте прямыми дороги Его!“»1:3 Ис. 40:3.

4В пустыне появился Иоанн Креститель и проповедовал крещение в знак покаяния для прощения грехов. 5К нему приходили люди со всей Иудеи и все жители Иерусалима. Они исповедовали свои грехи, и Иоанн крестил их в реке Иордане. 6Иоанн носил одежду из верблюжьей шерсти и подпоясывался кожаным поясом. Ел он саранчу и дикий мед. 7В своей проповеди он говорил:

– После меня придет Тот, Кто могущественнее меня, и я даже не достоин, нагнувшись, развязать ремни Его сандалий. 8Я крестил вас водой, а Он будет крестить вас Святым Духом.

Иоанн крестит Иисуса

(Мат. 3:13-17; Лк. 3:21-22; Ин. 1:32-34)

9В то время из галилейского города Назарета пришел Иисус и тоже был крещен Иоанном в Иордане. 10И когда Иисус выходил из воды, Он тотчас увидел раскрывшиеся небеса и Духа, спускающегося на Него в образе голубя. 11И с небес прозвучал голос:

– Ты Мой любимый Сын! В Тебе Моя радость!

Сатана искушает Иисуса в пустыне

(Мат. 4:1-11; Лк. 4:1-13)

12Тотчас Дух побудил Иисуса пойти в пустыню. 13Он находился в пустыне сорок дней, искушаемый сатаной. Иисус был там один, в окружении диких зверей, и ангелы служили Ему.

Иисус начинает Свое служение

(Мат. 4:12-17; Лк. 4:14-15)

14После того как Иоанн был арестован, Иисус пришел в Галилею, возвещая Радостную Весть от Бога.

15– Пришло время, – говорил Он, – Царство Божье уже близко! Покайтесь и верьте в Радостную Весть!

Четыре рыбака следуют за Иисусом

(Мат. 4:18-22; Лк. 5:2-11; Ин. 1:35-42)

16Однажды, проходя вдоль Галилейского озера, Иисус увидел Симона и его брата Андрея. Они забрасывали в озеро сети, так как были рыбаками.

17– Идите за Мной, – сказал им Иисус, – и Я сделаю вас ловцами людей.

18Братья сразу же оставили сети и пошли за Ним. 19Пройдя немного дальше, Он увидел Иакова и Иоанна, сыновей Зеведея, которые сидели в лодке и чинили сети. 20И Он сразу же позвал их, и они, оставив своего отца Зеведея с наемными работниками в лодке, пошли за Ним.

Иисус изгоняет нечистого духа

(Лк. 4:31-37)

21Когда они пришли в Капернаум, Иисус в первую же субботу пошел в синагогу и учил там. 22Люди изумлялись Его учению, потому что Он учил их как имеющий власть, а не как учители Закона. 23Как раз в это время в синагоге находился человек, одержимый нечистым духом, который вдруг закричал:

24– Что Ты хочешь от нас, Иисус из Назарета? Ты пришел, чтобы погубить нас? Я знаю, Кто Ты! Ты – Святой Божий!

25– Замолчи! – строго приказал Иисус. – Выйди из него!

26Нечистый дух сотряс человека и с громким криком вышел из него. 27Люди в изумлении говорили друг другу:

– Что это? Новое учение, да еще и с такой властью! Он даже нечистым духам приказывает, и те подчиняются Ему!

28Слух об Иисусе мгновенно разошелся по всей Галилее.

Иисус исцеляет больных

(Мат. 8:14-16; Лк. 4:38-41)

29Из синагоги они с Иаковом и Иоанном сразу же пошли домой к Симону и Андрею. 30Теща Симона лежала в горячке, и Иисусу сразу сказали о ней. 31Он подошел к ней, взял ее за руку и помог подняться. Жар ее прошел, и она начала накрывать им на стол.

32С наступлением вечера, после захода солнца, к Иисусу стали приносить всех больных и одержимых демонами. 33Весь город собрался у дверей. 34В тот день Иисус исцелил многих от самых различных болезней и изгнал много демонов. Демонам Он запрещал говорить, потому что они знали, Кто Он.

Иисус проповедует в Галилее

(Лк. 4:42-44)

35На следующее утро, когда было еще темно, Иисус вышел из дома, пошел в безлюдное место и там молился. 36Симон и другие ученики бросились искать Его 37и, когда нашли, сказали Ему:

– Все Тебя ищут!

38А Он им ответил:

– Пойдем в другие места, в соседние селения, чтобы Мне и там проповедовать Радостную Весть, Я ведь для этого и пришел.

39И Он ходил по всей Галилее, проповедуя в синагогах и изгоняя демонов.

Иисус исцеляет прокаженного

(Мат. 8:2-4; Лк. 5:12-16)

40Однажды к Нему подошел человек, больной проказой. Упав перед Иисусом на колени, он стал умолять Его:

– Если Ты захочешь, Ты можешь меня очистить.

41Иисусу стало жаль его. Он протянул руку, прикоснулся к нему и сказал:

– Хочу, очистись!

42Как только Он это сказал, проказа сошла с человека, и тот стал чистым. 43Иисус тут же отослал его, строго предупредив:

44– Смотри, никому не говори об этом, но пойди, покажись священнику и принеси в жертву за очищение то, что повелел Моисей1:44 См. Лев. 14:1-32.. Так твое исцеление будет удостоверено перед людьми.

45Но тот пошел и начал повсюду рассказывать о случившемся. Из-за этого Иисусу стало невозможно открыто появляться в городе, и Он оставался в безлюдных местах. Народ, однако, стекался к Нему отовсюду.