Luka 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 1:1-80

Mawu Oyamba

1Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu, 2monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu. 3Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo, 4kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.

Aneneratu za Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

5Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni. 6Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse. 7Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.

8Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu, 9Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani. 10Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.

11Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira. 12Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha. 13Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane. 14Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake, 15chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa. 16Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo. 17Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”

18Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”

19Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu. 20Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”

21Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu. 22Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.

23Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo. 24Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu. 25Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”

Aneneratu za Kubadwa kwa Yesu

26Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya, 27kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya. 28Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”

29Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere. 30Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu. 31Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu. 32Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide, 33ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.”

34Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”

35Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu. 36Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi. 37Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”

38Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”

Mariya Acheza kwa Elizabeti

39Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya, 40kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti. 41Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera. 42Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke! 43Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine? 44Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe. 45Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”

Nyimbo ya Mariya

46Ndipo Mariya anati:

“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.

47Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

48pakuti wakumbukira

kudzichepetsa kwa mtumiki wake.

Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,

49pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,

dzina lake ndi loyera.

50Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye

kufikira mibadomibado.

51Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;

Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.

52Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,

koma wakweza odzichepetsa.

53Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino

koma anachotsa olemera wopanda kanthu.

54Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,

pokumbukira chifundo chake.

55Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse

monga ananena kwa makolo athu.”

56Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.

Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

57Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna. 58Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.

59Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya, 60koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”

61Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”

62Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo. 63Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.” 64Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu. 65Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi. 66Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.

Nyimbo ya Zakariya

67Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,

68“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli

chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.

69Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife

mu nyumba ya mtumiki wake Davide.

70(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),

71chipulumutso kuchoka kwa adani athu

ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,

72kuonetsa chifundo kwa makolo athu

ndi kukumbukira pangano lake loyera,

73lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:

74kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,

ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,

75mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.

76“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;

pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,

77kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso

kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,

78chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,

ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,

79kuwalira iwo okhala mu mdima

ndi mu mthunzi wa imfa,

kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”

80Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

New Russian Translation

Луки 1:1-80

Введение

1Поскольку уже многие принялись составлять описание произошедших среди нас событий 2на основе сведений, переданных нам людьми, которые с самого начала были очевидцами и служителями Слова, 3то и я решил, тщательно исследовав все от начала, описать тебе, достопочтеннейший Феофил, все по порядку, 4чтобы ты мог убедиться в достоверности того, чему был научен.

Ангел предвозвещает Захарии рождение Иоанна

5Во время правления Ирода1:5 Ирод – это Ирод Великий, который был царем Иудеи с 40 по 4 гг. до н. э. Кроме Иудеи, его владения включали в себя также Самарию и Галилею., царя Иудеи, был священник по имени Захария, из смены Авия1:5 Служение в Иерусалимском храме было разделено между 24 сменами священников потомков Аарона (см. 1 Пар. 24:1-19).. Его жена тоже была потомком Аарона, ее звали Елизавета. 6Оба они были праведны перед Богом, живя непорочно и строго соблюдая все заповеди и установления Господа. 7Но у них не было детей, потому что Елизавета была бесплодна. Они оба были уже в преклонном возрасте.

8Однажды, когда была очередь служить смене, к которой принадлежал Захария, он нес службу перед Богом. 9В соответствии с установленным для священников порядком ему выпало по жребию войти в храм Господа и возжигать благовония1:9 См. Исх. 30:6-8.. 10Во время возжигания благовоний множество народа молилось снаружи. 11Захарии же явился ангел Господа. Он стоял справа от жертвенника, где возжигались благовония. 12Когда Захария увидел его, он был чрезвычайно поражен и испуган. 13Ангел сказал ему:

– Не бойся, Захария, твоя молитва услышана. Твоя жена Елизавета родит тебе сына, и ты назовешь его Иоанном. 14Твое сердце наполнится счастьем и ликованием, и многие будут радоваться его рождению, 15потому что он будет великим перед Господом. Он никогда не будет пить вина и других хмельных напитков. От самого рождения он будет исполнен Святым Духом. 16Многих израильтян он обратит к Господу, их Богу. 17Он будет предшествовать Ему в духе и силе Илии, чтобы обратить сердца отцов к детям, а непокорных – к мудрости праведных, приготовляя народ к приходу Господа1:17 См. Мал. 4:5-6..

18Захария спросил ангела:

– Как мне узнать, что это сбудется? Ведь я уже стар, и жена моя в преклонных годах.

19Ангел ответил:

– Я – Гавриил, стоящий перед Богом, и я послан, чтобы сообщить тебе эту радостную весть. 20Но сейчас за то, что ты не поверил моим словам, которые обязательно исполнятся в свое время, ты лишишься дара речи и не будешь говорить до того дня, пока это не сбудется.

21Между тем люди ждали Захарию и удивлялись, почему он так долго не выходит из храма. 22Когда Захария вышел, он не мог говорить и вынужден был общаться с ними жестами. Все поняли, что в храме ему было видение.

23Когда срок его служения закончился, Захария возвратился домой. 24Вскоре его жена Елизавета забеременела и пять месяцев не выходила из дома1:24 Букв.: «скрывала себя».. 25Она говорила:

– Вот что сделал для меня Господь, по милости Своей сняв с меня позор перед людьми!

Предсказание о рождении Иисуса

26Когда Елизавета была на шестом месяце беременности, Бог послал ангела Гавриила в галилейский город Назарет, 27к деве по имени Мария1:27 На греческом языке «Мариам». Так во всех местах в этой книге, за исключением ст. 1:41.. Мария была обручена с Иосифом, потомком Давида. 28Ангел пришел к ней и сказал:

– Приветствую тебя, получившая милость! С тобой Господь!

29Марию эти слова очень удивили, и она размышляла, что бы значило такое приветствие. 30Ангел продолжал:

– Не бойся, Мария, потому что Бог проявил к тебе милость! 31Ты забеременеешь и родишь Сына, и назовешь Его Иисусом1:31 Иисус – на языке иудеев звучит как «Йешуа» и означает «ЙГВГ (Господь) спасает».. 32Он станет великим, и Его будут называть Сыном Всевышнего. Господь Бог даст Ему престол Его предка Давида, 33и Он будет царствовать над домом Иакова вовеки, и Его Царству не будет конца.

34– Как это может быть? – спросила Мария. – Ведь я еще не была с мужчиной.

35Ангел ответил:

– Святой Дух сойдет на тебя, и тебя осенит сила Всевышнего. Поэтому Ребенок, Который родится у тебя, будет свят – Он будет зваться Сыном Бога. 36Вот и твоя родственница Елизавета тоже родит сына в ее преклонные годы. О ней говорили, что она бесплодна, но она уже на шестом месяце беременности. 37Для Бога нет ничего невозможного.

38– Я готова служить Господу, – ответила Мария, – пусть все произойдет со мной так, как ты сказал.

И ангел оставил ее.

Мария навещает Елизавету

39Вскоре после этого Мария собралась и поспешила в город, расположенный в нагорьях Иудеи. 40Она вошла в дом Захарии и поприветствовала Елизавету. 41Когда Елизавета услышала приветствие Марии, ребенок внутри у нее встрепенулся; Елизавету наполнил Святой Дух, 42и она громким голосом воскликнула:

– Благословенна ты среди женщин, и благословен Ребенок, Которого ты носишь! 43Чем я заслужила такую милость, что ко мне пришла мать моего Господа? 44Как только я услышала твое приветствие, ребенок во мне так и встрепенулся от радости. 45Блаженна поверившая в исполнение того, что сказал Господь!

46Мария ответила:

– Душа моя славит Господа,

47и дух мой радуется о Боге, Спасителе моем,

48потому что Он увидел смирение Своей служанки1:48 См. 1 Цар. 1:11; 2:1..

Отныне все поколения будут называть меня благословенной,

49потому что Всемогущий совершил такое великое дело для меня!

Его имя свято!1:49 См. Пс. 110:9.

50Из поколения в поколение

Он проявляет милость к боящимся Его!1:50 См. Пс. 102:17.

51Его рукой совершены великие дела:

Он рассеял гордых в надмении сердца их,

52сверг правителей с их престолов

и возвысил смиренных!

53Он насытил благами голодных,

а богатых отослал ни с чем.

54Он помог Своему слуге Израилю,

помня Свое обещание нашим предкам –

55быть милосердным к Аврааму

и его семени вовеки.

56Мария погостила у Елизаветы около трех месяцев и затем возвратилась домой.

Рождение, наречение имени и обрезание Иоанна Крестителя

57Когда подошло время, Елизавета родила сына. 58Ее соседи и родственники услышали о том, что Бог явил ей великую милость, и радовались вместе с ней. 59На восьмой день1:59 Восьмой день – по Закону Божьему обрезание производилось на восьмой день (см. Быт. 17:12). они пришли, чтобы совершить над ребенком обряд обрезания, и хотели назвать его в честь отца Захарией. 60Но мать ребенка возразила:

– Нет! Его будут звать Иоанном.

61Ей стали говорить:

– Но ведь среди ваших родственников нет никого с таким именем!

62Они стали жестами спрашивать отца, как бы он хотел назвать сына. 63Захария попросил табличку для письма и, к удивлению всех, написал:

«Его имя Иоанн».

64В тот же миг к нему вернулась речь, и он начал говорить, прославляя Бога. 65Всех соседей объял страх, и весть о случившемся разнеслась по всем нагорьям Иудеи. 66Все, кто слышал об этом, с удивлением спрашивали:

– Кем же станет этот ребенок? – потому что рука Господа была с ним.

Пророческое слово Захарии

67Святой Дух наполнил Захарию, отца Иоанна, и он начал пророчествовать:

68– Благословен Господь, Бог Израиля1:68 См. Пс. 40:14; 71:18; 105:48.,

Который посетил Свой народ и искупил его!

69Он воздвиг нам рог спасения1:69 То есть «могучего Спасителя»; (см. Пс. 17:3). Рог был символом могущества, власти и силы (см., напр., 1 Цар. 2:10; Иер. 48:25; Мих. 4:13).

из дома Своего слуги Давида,

70как Он издавна обещал через Своих святых пророков,

71что Он спасет нас от врагов

и от рук тех, кто ненавидит нас.

72Так Он проявил милость к нашим предкам,

помня Свой святой завет,

73клятву, которой Он поклялся нашему предку Аврааму:

74избавить нас от рук наших врагов,

чтобы мы могли без страха служить Ему,

75живя перед Ним в святости и праведности

во все дни нашей жизни!

76И ты, дитя, будешь назван пророком Всевышнего,

потому что будешь идти перед Господом,

чтобы приготовить Ему пути1:76 См. Ис. 40:3; Мал. 3:1.,

77возвестить Его народу спасение

через прощение грехов,

78по глубочайшему милосердию нашего Бога,

Который пошлет нам Утреннюю Зарю с небес,

79чтобы дать свет живущим во тьме и тени смертной1:79 См. Ис. 9:2.

и направить наши стопы на путь мира!

80Ребенок рос и укреплялся в духе. Он жил в пустыне до того времени, когда открыто явился Израилю.