Lonjezo la Mzimu Woyera
1Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa, 2mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha. 3Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi. 4Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani. 5Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
Yesu Akwera Kumwamba
6Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo. 8Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo. 11Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
Matiyasi Alowa Mʼmalo mwa Yudasi Isikarioti
12Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo. 13Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo. 14Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120). 16Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu. 17Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka. 19Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti,
“Nyumba yake isanduke bwinja,
ndipo pasakhale wogonamo.
Ndiponso,
“Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe, 22kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi. 24Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa 25kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.” 26Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.
Вознесение Иисуса на небеса
1В моем первом повествовании, Феофил, я написал обо всем, что Иисус делал и чему Он учил от начала 2до того дня, когда, дав через Святого Духа повеления избранным Им апостолам, Он вознесся на небеса. 3После Своего страдания Он представал перед этими людьми живым со многими доказательствами. Иисус являлся им в течение сорока дней и говорил о Божьем Царстве. 4Однажды, обедая вместе с ними1:4 Или: «Однажды, собрав их»., Он велел им не покидать Иерусалима, но ждать обещанного Отцом.
– Это то, о чем вы и слышали от Меня. 5Потому что Иоанн крестил водой, а вы через несколько дней будете крещены Святым Духом.
6Когда ученики собрались вместе, они спросили Его:
– Господи, не настало ли время Тебе восстановить царство Израиля?1:6 В те времена Израиль находился под властью римской империи, и народ надеялся, что Христос избавит их от гнета завоевателей. Но Царство, о котором возвещал Иисус, не принадлежит этому миру и устанавливается духовным путем.
7Он сказал им:
– Не ваше дело знать времена и сроки, которые Отец установил Своей властью. 8Когда на вас сойдет Святой Дух, вы получите силу и будете Моими свидетелями в Иерусалиме, по всей Иудее, в Самарии и до края земли.
9Сказав это, Он на их глазах был поднят ввысь, и облако скрыло Его от их взглядов.
10Они пристально смотрели в небо, пока Он поднимался, как вдруг рядом с ними оказались два человека в белых одеждах.
11– Галилеяне, – сказали они, – что вы стоите и смотрите в небо? Этот Иисус, Который был взят от вас в небеса, придет точно таким же образом, каким вы видели Его возносящимся.
Избрание нового апостола вместо Иуды
(Мат. 10:2-4; Мк. 3:15-19; Лк. 6:14-16)
12После этого они возвратились в Иерусалим с горы, называемой Оливковой, которая находится на расстоянии субботнего пути1:12 То есть примерно в 1 100 метрах. от Иерусалима. 13Придя, они поднялись в верхнюю комнату и там оставались – Петр и Иоанн, Иаков и Андрей, Филипп и Фома, Варфоломей и Матфей, Иаков, сын Алфея, Симон Зилот и Иуда, сын Иакова. 14Все они единодушно пребывали в молитве. С ними были и несколько женщин, а также мать Иисуса Мария1:14 Греч.: «Мариам». и Его братья.
15В те дни Петр встал посреди верующих (в собрании было около ста двадцати человек) 16и сказал:
– Братья, должно было исполниться Писание, где Святой Дух предсказал через Давида об Иуде, который вел тех, кто шел арестовать Иисуса. 17Иуда был одним из нас и принимал участие в нашем служении. 18(На деньги, полученные за совершенное им зло, он купил поле1:18 Он купил поле – имеется в виду, что поле было куплено священниками на деньги Иуды, т. е. как бы от его имени (см. Мат. 27:5-7)., но, упав вниз головой1:18 Не совсем понятно, как это описание сопоставимо с тем, что записано в Мат. 27:3-10. Возможно, что после того, как Иуда повесился, оборвалась веревка (или сломалась ветка) и он рухнул на землю., он разбился, и его внутренности вывалились наружу. 19Об этом узнали все жители Иерусалима и прозвали поле, на своем языке1:19 То есть на арамейском языке. Акелдама1:19 На арамейском языке «Хакал Дема»., то есть «Кровавое поле».) 20Ведь в книге Псалмов написано:
«Пусть его жилище будет в запустении,
пусть никто там больше не живет»1:20 См. Пс. 68:26.
и
«Пусть другой займет его положение»1:20 См. Пс. 108:8..
21Поэтому нам необходимо выбрать одного из тех людей, кто сопровождал нас все то время, когда Господь Иисус был среди нас, 22начиная от крещения Иоанна и до того дня, когда Иисус был взят от нас. Он, как и мы, должен быть свидетелем Его воскресения.
23Предложили двоих: Иосифа, которого еще называют Варсавой или Иустом, и Матфия. 24И помолились:
– Господи, Ты знаешь сердце каждого; укажи на одного из этих двоих, кого Ты избрал 25на это служение: быть Твоим апостолом вместо Иуды, который ушел, куда ему суждено.
26Потом они бросили жребий, и жребий выпал на Матфия, который и был причислен к одиннадцати апостолам.