Yesaya 64 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 64:1-12

1Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,

kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!

2Monga momwe moto umatenthera tchire

ndiponso kuwiritsa madzi,

tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,

ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.

3Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,

ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo

kapena kuona

Mulungu wina wonga Inu,

amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.

5Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,

amene amakumbukira njira zanu.

Koma Inu munakwiya,

ife tinapitiriza kuchimwa.

Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?

6Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,

ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;

tonse tafota ngati tsamba,

ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.

7Palibe amene amapemphera kwa Inu

kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;

pakuti mwatifulatira

ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

8Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.

Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;

ife tonse ndi ntchito ya manja anu.

9Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso

musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.

Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,

pakuti tonsefe ndi anthu anu.

10Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;

ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.

11Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,

yatenthedwa ndi moto

ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.

12Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?

Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

Korean Living Bible

이사야 64:1-12

1여호와여, 하늘을 가르고 내려오소서. 작은 나뭇가지가 불에 타고

2물이 불에 끓듯이 산들이 주를 보면 두려워 떨 것입니다. 여호와여, 오셔서 주의 원수들에게 주의 능력을 나타내셔서 온 세상이 주 앞에서 떨게 하소서.

3주께서 오셔서 우리가 생각할 수 없는 놀라운 일을 행하셨을 때에 산들이 주 앞에서 두려워 떨었습니다.

4자기에게 희망을 건 사람들을 위하여 주와 같이 이런 놀라운 일을 행하시는 신이 있었다는 말을 옛날부터 들은 자가 없고 깨달은 자도 없으며 그런 신을 본 사람도 없습니다.

5주는 기쁘게 옳은 일을 행하는 자와 주의 법도를 기억하는 자를 환영하십니다. 그러나 우리가 주께 계속 범죄했을 때 주는 분노하셨으니 우리가 어떻게 구원을 얻겠습니까?

6우리는 다 64:6 또는 ‘부정한 자 같아서’죄로 더러워졌으며 우리의 의로운 행위는 때묻은 누더기와 같아서 우리가 다 잎사귀처럼 말라 죄악의 바람에 휩쓸려가고 있습니다.

7주의 이름을 부르는 자가 없으며 애써 주를 붙들려고 하는 자도 없습니다. 그러므로 주께서는 우리의 죄 때문에 우리를 외면하시고 버리셨습니다.

8그러나 여호와여, 주는 우리의 아버지이십니다. 우리는 진흙이며 주는 토기장이와 같아서 주의 손으로 우리를 만드셨습니다.

9여호와여, 너무 분노하지 마시고 우리의 죄를 영원히 기억하지 마소서. 우리는 다 주의 백성들입니다. 우리를 굽어살피소서.

10주의 거룩한 성들이 파괴되고 시온이 광야가 되었으며 예루살렘이 폐허가 되었습니다.

11우리 조상들이 주를 찬양하던 거룩하고 아름다운 우리의 성전이 불에 탔으며 우리가 소중히 여기던 곳이 다 황무지가 되고 말았습니다.

12여호와여, 이런 일이 있었는데도 주는 우리를 돕지 않으시겠습니까? 우리가 말할 수 없는 고통을 당하고 있는데도 주는 침묵만 지키고 계시겠습니까?