Yesaya 65 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

Korean Living Bible

이사야 65:1-25

거역하는 자들에 대한 하나님의 심판

1여호와께서 말씀하셨다. “나에게 묻지 않은 사람들에게 내가 나를 나 타내고 나를 찾지 않던 사람들에게 내가 발견되었으며 내 이름을 부르지 않은 나라에 ‘내가 여기 있다. 내가 여기 있다’ 하였다.

2내가 하루 종일 팔을 벌리고 내 백성을 맞을 준비를 하였으나 그들은 거역하며 자기들 멋대로 악한 짓을 하고 있다.

3그들은 정원에서 제사를 지내고 벽돌 제단에서 분향하여 항상 내 분노를 일으키는 백성이다.

4밤이 되면 그들은 죽은 자들의 영들을 만나려고 무덤이나 동굴을 찾아가며 먹지 못하도록 되어 있는 돼지고기를 먹고 우상에게 제사한 고기를 삶아 그 국물을 마시면서도

5다른 사람에게는 ‘너무 가까이 오지 말아라. 나는 네가 만져서는 안 될 거룩한 몸이다’ 하고 말하니 이런 자들이 65:5 원문에는 ‘내 코의 연기요 종일 타는 불이로다’밤낮 내 분노를 일으키고 있다.

6“내가 이미 그들을 벌하기로 작정하였고 그들의 심판이 내 앞에 기록되었으니 그들이 행한 일을 내가 모르는 척하지 않고 반드시 그 대가를 받도록 할 것이다.

7그들의 죄는 물론 그 조상들의 죄에 대해서도 내가 그들에게 벌을 내리겠다. 그들이 산 위의 이방 신전에서 분향하며 나를 모욕하였으므로 내가 그들의 지난 일을 철저하게 계산하여 그들이 행한 그대로 갚아 줄 것이다.

8“나쁜 포도송이에도 즙을 짤 만한 좋은 포도가 있으므로 사람들이 그것을 송이째 던져 버리지 않는 것처럼 나도 내 백성을 송두리째 멸망시키지 않고

9이스라엘 땅을 소유할 내 백성을 살아 남게 하겠다. 나를 섬기는 택한 내 백성들이 거기서 살 것이다.

10그들이 나를 섬기며 사론 평야와 아골 골짜기에서 그들의 소떼와 양떼를 먹일 것이다.

11“그러나 나 여호와를 버리고 나의 거룩한 산을 잊고 행운과 운명의 신인 갓과 므니 신을 섬기는 자들은

12칼날에 죽음을 당하도록 하겠다. 이것은 내가 불러도 그들이 대답하지 않았으며 내가 말을 해도 그들이 듣지 않고 내 앞에서 악을 행하며 내가 기뻐하지 않는 일을 택하였기 때문이다.

13그래서 내가 말하지만 나를 섬기는 종들은 먹고 마실 것이 풍성할 것이나 그들은 굶주리고 목마를 것이다. 내 종들은 즐거워할 것이지만 그들은 수치를 당할 것이며

14내 종들은 기뻐서 노래할 것이나 그들은 슬픔과 절망 가운데서 통곡할 것이다.

15내가 택한 백성들이 그들의 이름을 저줏거리로 사용할 것이니 나 여호와가 그들은 죽이고 내 종들에게는 새로운 이름을 줄 것이다.

16복을 구하는 자들이 진리의 하나님께 복을 구하며 맹세하는 자들이 신실한 하나님의 이름으로 맹세할 때가 올 것이다. 이것은 내가 지나간 일들을 다 잊어버릴 것이기 때문이다.”

새 하늘과 새 땅

17여호와께서 말씀하신다. “보라! 내가 새 하늘과 새 땅을 창조한다. 이전 것은 기억되거나 생각나지 않을 것이다.

18너희는 내가 창조하는 것을 보고 영원히 기뻐하며 즐거워하라. 내가 만들 새 예루살렘은 기쁨이 충만할 것이며 그 백성들은 행복할 것이다.

19내가 예루살렘과 그 백성 때문에 기뻐할 것이니 다시는 거기서 우는 소리와 부르짖는 소리가 들리지 않을 것이다.

20거기에는 며칠 살지 못하고 죽는 유아가 없을 것이며 제 명대로 다 살지 못하는 사람이 없을 것이다. 백 세에 죽는 사람도 젊어서 죽는 사람으로 여기고 백 세가 되지 못해서 죽는 사람은 저주를 받은 것으로 여길 것이다.

21내 백성이 집을 짓고 거기에 살며 포도원을 가꾸어 그 포도를 먹을 것이다.

22그들이 지은 집에 다른 사람이 살지 않을 것이며 그들이 재배한 것을 타인이 먹지 않을 것이다. 이것은 그들이 나무처럼 오래 살며 자기들이 수고하여 얻은 것을 길이 누릴 것이기 때문이다.

23그들의 수고가 헛되지 않을 것이며 그들의 자녀들이 재난을 만나지 않을 것이다. 내가 그들과 그 후손들을 축복하겠다.

24그들이 나를 부르기도 전에 내가 대답할 것이며 그들이 말을 끝맺기도 전에 내가 그들의 기도에 응답할 것이다.

25이리와 어린 양이 함께 먹고 사자가 소처럼 짚을 먹을 것이며 뱀이 흙을 먹고 살 것이다. 이와 같이 나의 거룩한 산에서는 상하거나 해치는 일이 없을 것이다.”