Yesaya 63 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 63:1-19

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

1Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,

atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?

Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,

akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo

ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

2Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,

ngati za munthu wofinya mphesa?

3“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,

palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.

Ndinawapondereza ndili wokwiya

ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;

magazi awo anadothera pa zovala zanga,

ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.

4Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;

ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.

5Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.

Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;

choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,

ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.

6Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;

ndipo ndinawasakaza

ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

7Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,

ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.

Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.

Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake

Yehova wachitira nyumba ya Israeli

zinthu zabwino zambiri.

8Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,

ana anga amene sadzandinyenga Ine.”

Choncho anawapulumutsa.

9Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,

ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.

Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,

anawanyamula ndikuwatenga

kuyambira kale lomwe.

10Komabe iwo anawukira

ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.

Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo

ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,

masiku a Mose mtumiki wake;

ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,

pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?

Ali kuti Iye amene anayika

Mzimu Woyera pakati pawo?

12Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa

ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?

Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,

kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,

13amene anawayendetsa pa nyanja yozama?

Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,

iwo sanapunthwe;

14Mzimu Woyera unawapumulitsa

ngati mmene ngʼombe zimapumulira.

Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu

kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,

wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.

Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?

Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.

16Koma Inu ndinu Atate athu,

ngakhale Abrahamu satidziwa

kapena Israeli kutivomereza ife;

Inu Yehova, ndinu Atate athu,

kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.

17Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?

Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?

Bwererani chifukwa cha atumiki anu;

mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.

18Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,

adani athu anasakaza malo anu opatulika.

19Ife tili ngati anthu amene

simunawalamulirepo

ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

Korean Living Bible

이사야 63:1-19

심판하시고 구원하시는 하나님

1에돔의 보스라성에서 오는 자가 누구냐? 화려하게 붉은 옷을 입고 63:1 또는 ‘큰 능력으로’위 풍 당당하게 걸어오는 자가 누구냐? “그는 의를 말하며 구원할 능력을 가진 나 여호와이다.”

2어째서 네 옷이 포도즙틀을 밟는 사람처럼 붉은가?

3“내가 분노하여 포도즙틀을 밟듯이 내 원수들을 혼자서 짓밟았는데 그들의 피가 튀어 내 옷을 더럽혔다.

4내가 내 백성의 원수를 갚아 그들을 구할 때가 되었으나

5내가 보니 나를 도와주는 자가 아무도 없어 놀라지 않을 수 없었다. 그래서 내가 분노하여 혼자 심판을 단행하였으니

6내가 분노로 이방 나라들을 마구 짓밟아 부수고 그들의 피를 땅에 쏟아 버렸다.”

찬양과 기도

7내가 여호와의 한결같은 사랑을 말하고 우리를 위해 행하신 모든 일에 대하여 그를 찬양할 것이니 여호와께서는 그의 자비와 한결같은 사랑으로 이스라엘 백성에게 풍성한 은혜를 베푸셨다.

8여호와께서 “그들은 내 백성이며 거짓말을 하지 않는 자녀” 라 하시고 그들의 구원자가 되셨으며

9그들의 모든 환난에 동참하셔서 그들을 직접 구원하셨다. 그가 사랑과 자비로 그들을 구출해 내시고 그들을 항상 돌보셨으나

10그들이 여호와를 거역하고 그의 성령을 근심하게 하였다. 그래서 그가 그들의 대적이 되어 그들과 싸우셨다.

11그때 백성들이 옛날 모세 때의 일을 기억하며 이렇게 말하였다. “바다에서 자기 백성의 지도자들을 구원하신 분이 어디 계시는가? 그들 가운데 성령을 보내신 분이 지금 어디 계시는가?

12-13모세를 통하여 그의 크신 능력으로 위 대한 일을 행하시며 바닷물을 갈라 자기 백성을 깊은 물 가운데로 인도해 내셔서 영구한 명성을 얻으신 분이 어디 계시는가?” 그들은 여호와의 인도를 받아 광야를 누비는 말처럼 넘어지지 않고 안전하게 깊은 물을 건넜다.

14여호와의 성령께서 비옥한 골짜기로 내려가는 가축처럼 그들을 편히 쉬게 하셨다. 이와 같이 여호와께서는 자기 백성을 인도하여 자기 이름을 영화롭게 하셨다.

15여호와여, 하늘에서 굽어살피시며 거룩하고 영광스러운 주의 처소에서 우리를 보소서. 전에 우리에게 보여 주신 주의 크신 관심은 어디 있습니까? 이제 주의 능력은 어디 있으며 주의 사랑과 자비는 어디 있습니까? 제발 우리를 외면하지 마소서.

16주는 우리의 아버지이십니다. 우리의 조상 아브라함과 야곱은 우리를 인정하지 않을지라도 주는 항상 우리를 구원하시는 우리의 아버지가 아니십니까?

17여호와여, 어째서 우리가 주의 길에서 떠나 우리 마음을 굳게 하여 주를 두려운 마음으로 섬길 수 없게 하십니까? 항상 주를 섬기는 주의 종들을 위해 돌아오소서.

18주의 백성들이 주의 성소를 차지한 지 얼마 되지 않아 우리 원수들이 그 곳을 짓밟아 버렸습니다.

19주는 마치 우리를 다스리시는 분이 아닌 것처럼, 또 우리가 주의 백성이 아닌 것처럼 우리를 취급하십니다.