Yesaya 63 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 63:1-19

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

1Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,

atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?

Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,

akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo

ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

2Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,

ngati za munthu wofinya mphesa?

3“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,

palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.

Ndinawapondereza ndili wokwiya

ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;

magazi awo anadothera pa zovala zanga,

ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.

4Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;

ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.

5Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.

Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;

choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,

ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.

6Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;

ndipo ndinawasakaza

ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

7Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,

ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.

Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.

Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake

Yehova wachitira nyumba ya Israeli

zinthu zabwino zambiri.

8Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,

ana anga amene sadzandinyenga Ine.”

Choncho anawapulumutsa.

9Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,

ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.

Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,

anawanyamula ndikuwatenga

kuyambira kale lomwe.

10Komabe iwo anawukira

ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.

Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo

ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,

masiku a Mose mtumiki wake;

ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,

pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?

Ali kuti Iye amene anayika

Mzimu Woyera pakati pawo?

12Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa

ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?

Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,

kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,

13amene anawayendetsa pa nyanja yozama?

Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,

iwo sanapunthwe;

14Mzimu Woyera unawapumulitsa

ngati mmene ngʼombe zimapumulira.

Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu

kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,

wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.

Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?

Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.

16Koma Inu ndinu Atate athu,

ngakhale Abrahamu satidziwa

kapena Israeli kutivomereza ife;

Inu Yehova, ndinu Atate athu,

kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.

17Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?

Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?

Bwererani chifukwa cha atumiki anu;

mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.

18Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,

adani athu anasakaza malo anu opatulika.

19Ife tili ngati anthu amene

simunawalamulirepo

ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 63:1-19

Guds dom over Israels undertrykkere

1Hvem er den mægtige fyrste i blodrøde klæder, som kommer fra Botzra i Edoms land?

„Det er mig, Herren, som har magt til at frelse, og som afsiger retfærdige domme.”

2Hvorfor er dit tøj så rødt, som om du havde trampet druerne i vinpersen?

3„Jeg trådte vinpersen alene. Der var ingen, som hjalp mig. I min vrede nedtrådte jeg dem, som var de druer. Jeg trampede på dem, så jeg blev oversprøjtet med blod. 4Hævnens time var kommet, tiden til at befri mit folk fra deres undertrykkere. 5Jeg ventede på, om nogen ville hjælpe mig, jeg undrede mig over, at ingen støttede mig. Så fuldførte jeg dommen alene i min stærke vrede. 6Jeg nedtrådte folkene i vrede, fyldte dem med min harmes vin og lod deres blod løbe ud på jorden.”

Profeten mindes befrielsen fra slaveriet i Egypten og folkets utroskab

7Jeg vil mindes Herrens trofasthed. Jeg vil takke ham for alt, hvad han gjorde for os, glæde mig over hans godhed imod Israels folk, over hans barmhjertighed og urokkelige troskab. 8Han sagde: „Det er jo mit folk, og de vil ikke svigte mig.” Da befriede han dem fra slaveriet. 9Han sendte ikke en engel eller et sendebud for at redde dem, men han greb selv ind. På grund af sin kærlighed ynkedes han over dem og befriede dem. Han har jo båret dem og beskyttet dem helt fra begyndelsen.

10Men de gjorde alligevel oprør imod ham og bedrøvede hans hellige Ånd. Derfor blev han deres fjende og kæmpede imod dem.

Folket mindes Guds indgreb i fortiden og beder om hjælp

11Men så kom de i tanke om de gamle dage, hvor Moses førte folket ud af Egypten, og de råbte: „Hvor er den Gud, som førte Israels folk med dets ledere sikkert gennem havet? Hvor er den Gud, som gav sin hellige Ånd til sin tjener Moses? 12-13Hvor er den Gud, som viste sin vældige magt og gav Moses autoritet til at kløve havet foran hele folket? Hvor er den Gud, som udførte de store mirakler, som vi aldrig glemmer? De vandrede gennem havet så let som heste gennem ørkenen. 14Som kvæget, der føres ned til græsset i dalen, førte Herrens Ånd folket til et hvilested. Sådan førte Herren sit folk for at vise sin herlighed.

15Herre, se nu til os fra din hellige bolig i din herligheds Himmel. Hvad er der blevet af din nidkærhed for dit folk? Hvor er din vældige magt? Hvor er din barmhjertighed og kærlighed? Hvorfor oplever vi det ikke? 16Du er jo vores Far. Abraham og Jakob kan ikke hjælpe os. Det er dig, Herre, som har hjulpet og reddet os fra ældgammel tid. 17Herre, hvorfor tillader du os at fare vild fra dine veje? Hvorfor gør du os sløve, så vi glemmer at have ærefrygt for dig? Kom tilbage og grib ind, for vi ønsker at tjene dig, og vi tilhører dig. 18Dit hellige folk boede i landet en kort tid, men nu er det vores fjender, der nedtramper dit hellige sted. 19Vi har altid været dit folk. De andre folkeslag tilbeder dig ikke, og det er ikke dem, der har dig som deres Herre. Gid du ville flænge himlen og stige ned til os. Så ville bjergene bæve.