Yesaya 64 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 64:1-12

1Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,

kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!

2Monga momwe moto umatenthera tchire

ndiponso kuwiritsa madzi,

tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,

ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.

3Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,

ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo

kapena kuona

Mulungu wina wonga Inu,

amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.

5Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,

amene amakumbukira njira zanu.

Koma Inu munakwiya,

ife tinapitiriza kuchimwa.

Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?

6Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,

ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;

tonse tafota ngati tsamba,

ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.

7Palibe amene amapemphera kwa Inu

kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;

pakuti mwatifulatira

ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

8Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.

Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;

ife tonse ndi ntchito ya manja anu.

9Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso

musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.

Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,

pakuti tonsefe ndi anthu anu.

10Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;

ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.

11Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,

yatenthedwa ndi moto

ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.

12Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?

Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 64:1-11

1Det ville få folkeslagene til at skælve af angst og fjenderne til at frygte dit herlige navn, som når ild sætter kvas i brand og bringer vand i kog. 2For du gjorde engang undere, vi ikke ventede, og bjergene skælvede, da du viste dig. 3Intet øre har hørt, og intet øje har set en gud som dig, for du griber ind og hjælper dem, som sætter deres lid til dig. 4Du hjælper dem, som med glæde gør din vilje og følger dine veje.

Men vi syndede imod dig, og du blev vred. Evig og altid har vi været onde og ulydige.64,4 Teksten er uklar. 5Vi blev alle urene af synd. Selv det bedste, vi gjorde, var kun beskidte handlinger. Vi blev som visne blade, der blev fejet bort af vores synd som af vinden. 6Ingen bad dig om hjælp eller holdt sig nær til dig. Derfor vendte du dig bort og overlod os til den straf, vi fortjente.

7Men Herre, du er stadig vores Far! Vi er leret, og dine hænder har formet os. Vi er dit værk. 8Vær ikke alt for vred på os, Herre. Husk ikke for evigt på vores synd. Vi er jo dit udvalgte folk.

9Se, dine hellige byer er blevet jævnet med jorden, Zion ligner en øde ørken, Jerusalem ligger i ruiner. 10Vores hellige og prægtige tempel, hvor vores forfædre lovpriste dig, er brændt ned til grunden. Det sted, vi elskede over alt andet, er nu kun en ruinhob. 11Vil du stadig ikke gribe ind, Herre? Vil du stiltiende se på, at vi bliver straffet så hårdt?”