Yesaya 62 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 62:1-12

Dzina Latsopano la Ziyoni

1Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete,

chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete,

mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala,

ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.

2Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo

ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako.

Adzakuyitanira dzina latsopano

limene adzakupatse ndi Yehova.

3Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova,

ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.

4Sadzakutchanso “Wosiyidwa,”

ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.”

Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.”

Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.”

Chifukwa Yehova akukondwera nawe,

ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.

5Monga mnyamata amakwatira namwali,

momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira;

monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi,

chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.

6Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda;

sadzakhala chete usana kapena usiku.

Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake

musapumule.

7Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu

kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.

8Yehova analumbira atakweza dzanja lake.

Anati,

“Sindidzaperekanso tirigu wako

kuti akhale chakudya cha adani ako,

ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano

pakuti unamuvutikira.

9Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi

ndi kutamanda Yehova,

ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo

mʼmabwalo a Nyumba yanga.”

10Tulukani, dutsani pa zipata!

Konzerani anthu njira.

Lambulani, lambulani msewu waukulu!

Chotsani miyala.

Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.

11Yehova walengeza

ku dziko lonse lapansi kuti,

Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti,

“Taonani, chipulumutso chanu chikubwera;

Yehova akubwera ndi mphotho yake

akubwera nazo zokuyenerani.”

12Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika,

owomboledwa a Yehova;

ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova”

“Mzinda umene Yehova sanawusiye.”

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 62:1-12

1For Zions skyld vil jeg ikke tie. For Jerusalems skyld får jeg ikke ro, før retfærdigheden bryder igennem som morgenrøden, og frelsen som en flammende fakkel. 2Folkeslagene skal få øjnene op for, at du er god, og konger skal se din herlighed. Herren giver dig et nyt navn, som han selv vælger. 3Da bliver du som en prægtig kongekrone i Herren, din Guds, hånd. 4Du skal ikke længere kaldes „Den forkastede”, og dit land skal ikke længere hedde „Det gudsforladte land”. Nej, du skal kaldes „Min elskede” og „Min brud”, for Herren glæder sig over dig og hjemfører dig som sin brud. 5Som en ung mand hjemfører en jomfru, vil din Skaber hjemføre dig. Som en brudgom, der fryder sig over sin brud, vil Gud fryde sig over dig.

Bøn og forventning om Jerusalems genrejsning

6På dine mure, Jerusalem, har jeg sat vægtere ud, som dag og nat skal råbe til Gud, indtil hans løfter bliver opfyldt. Lad ikke hænderne synke, I, som beder. 7Lad ikke Herren få fred, før han genrejser Jerusalem og lader byen komme til ære og værdighed på jorden. 8Herren har aflagt et højtideligt løfte til sit folk, som han vil bakke op med al sin magt: „Jeres fjender skal ikke længere leve af jeres korn. De fremmede skal ikke drikke den vin, I har arbejdet så hårdt på at fremstille. 9Nej, I skal få lov at spise af det korn, I har høstet, og I skal prise Herren for det. Og I skal få lov til i templets forgård at drikke vinen fra de druer, I har plukket.”

10Gå ud af byen, Jerusalems indbyggere, og ban vej for det hjemvendende folk. Fjern de store sten og hejs et banner som tegn for hele verden. 11Herren siger til alle folkeslag på jorden: „Sig til Jerusalems indbyggere: Se, din Frelser er på vej, og han går foran sit frigivne folk.”

12De skal kaldes „Guds hellige folk” og „Herrens løskøbte folk”, og Jerusalem skal kaldes „Den foretrukne by” og „Byen, som ikke bliver forladt”.