Yeremiya 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 1:1-19

1Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. 2Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. 3Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

4Yehova anayankhula nane kuti,

5“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,

iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;

ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

6Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

7Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. 8Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

9Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu

polowera pa zipata za Yerusalemu;

iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake

ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.

16Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo

chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.

Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,

ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Jeremiasʼ Bog 1:1-19

Gud kalder Jeremias til profet

1Denne bog indeholder de budskaber, som Herren åbenbarede for mig. Jeg hedder Jeremias, er præst og søn af Hilkija, og jeg kommer fra Anatot i Benjamins land. 2Herren begyndte at tale til mig i kong Josias1,2 Teksten har Josias, søn af Amon. af Judas 13. regeringsår, 3og budskaberne fortsatte med at komme, mens Josias’ søn, Jojakim, var konge, helt frem til den femte måned i Zidkijas 11. regeringsår, da Jerusalem blev indtaget og indbyggerne ført i eksil.1,3 Både Jojakim og Zidkija var sønner af Josias. Se 2.Kong. 22–25. Jerusalem faldt i året 586 f.Kr.

4Herren sagde til mig: 5„Længe før jeg dannede dig i din mors liv, havde jeg planer for dig. Før du blev født, udvalgte jeg dig til at være profet for folkeslagene.”

6„Åh, almægtige Gud!” svarede jeg. „Jeg er alt for ung. Jeg har slet ikke autoritet til at kunne tale som profet.”

7„Du skal ikke undskylde dig med, at du er for ung,” svarede Herren. „Du skal bare gå, hvor jeg sender dig, og sige alt, hvad jeg befaler dig. 8Du skal ikke være bange for, hvordan folk vil reagere, for jeg går med dig og beskytter dig.”

9Så rakte Herren hånden ud og rørte ved min mund. „Jeg vil lægge mine ord i din mund,” sagde han. 10„Jeg giver dig hermed autoritet over folkeslag og kongeriger. Noget skal rykkes op med rode, mens andet skal plantes på ny. Noget skal rives ned til grunden, mens andet skal genopbygges.”

To syner, som bekræfter kaldet

11Derefter sagde Herren til mig: „Jeremias! Hvad ser du?”

„Jeg ser en gren fra et mandeltræ,” svarede jeg.

12„Det er rigtigt,” svarede Herren. „For jeg våger1,12 Et ordspil: Mandelgren hedder shaked på hebraisk, at våge hedder shoked. over mit ord for at opfylde det.”

13Lidt efter spurgte Herren: „Hvad ser du nu?”

„Jeg ser en gryde med kogende vand mod nord, og den er ved at vælte hen imod os,” svarede jeg.

14„Rigtigt,” svarede Gud. „For ulykken vil komme nordfra og strømme ud over alle landets indbyggere. 15Jeg tilkalder alle nordens konger med deres hære, så de kommer og belejrer Jerusalem og alle Judas byer. 16På den måde vil jeg dømme og straffe mit folk, fordi de har forladt mig og vendt sig til andre folks guder. Nu tilbeder de afgudsbilleder, som de selv har lavet. 17Gør dig parat til at stå frem og fortælle dem alt, hvad jeg befaler dig. Vær ikke bange for at konfrontere dem, ellers skal jeg give dig noget at være bange for. 18-19Jeg vil gøre dig hård over for deres kritik. Jeg gør dig stærk som en befæstet by, der er umulig at indtage, urokkelig som en jernsøjle, massiv som en mur af bronze. Hele folket med kongerne, embedsmændene og præsterne i spidsen vil være imod dig, men de vil ikke kunne vinde over dig, for jeg går med dig og beskytter dig.”