Yesaya 66 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 66:1-24

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?”

Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

3Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

amaphanso munthu,

ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,

amaphanso galu.

Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya

amaperekanso magazi a nkhumba.

Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso

amapembedzanso fano.

Popeza iwo asankha njira zawozawo,

ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.

4Inenso ndawasankhira chilango chowawa

ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.

Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,

pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.

Anachita zoyipa pamaso panga

ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

5Imvani mawu a Yehova,

inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:

“Abale anu amene amakudani,

ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,

‘Yehova alemekezeke

kuti ife tione chimwemwe chanu!’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6Imvani mfuwu mu mzinda,

imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!

Limenelo ndi liwu la Yehova,

kulanga adani ake onse.

7“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

wachira kale;

asanayambe kumva ululu,

wabala kale mwana wamwamuna.

8Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

Ndani anazionapo zinthu zoterezi?

Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,

kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?

Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa

nthawi yomweyo anabereka ana ake.

9Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.

“Kodi ndingatseke mimba

pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,

kondwera nayeni kwambiri,

nonse amene mumamulira.

11Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri

wa mʼmawere

a chitonthozo chake.”

12Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,

ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,

kapena kumufungata pa miyendo yake.

13Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

moteronso Ine ndidzakusangalatsani;

ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

14Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira

ndi kuti ndimakwiyira adani anga.

15Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;

Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake

ndi malawi amoto.

16Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

ndi moto ndi lupanga,

Yehova adzapha anthu ambiri.

17Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 66:1-24

1„Himlen er min trone, og jorden er min fodskammel. Hvordan vil I bygge et hus til mig? Hvordan vil I skaffe mig et sted at bo? 2Jeg har jo selv skabt det hele, og det tilhører mig,” siger Herren.

„Jeg hjælper dem, som har et ydmygt og sønderknust hjerte, og som handler på mine ord. 3Men mange håner mig med deres ondskab. De ofrer en okse til mig, men slår samtidig mennesker ihjel. De ofrer et lam til mig, men ofrer samtidig en hund til afguderne. De bringer et afgrødeoffer til mig, men et offer af svineblod til afguderne. De brænder røgelse for mig, men hylder også en afgud.66,3 Teksten er uklar. Oversættelsen støtter sig delvis til LXX. De har valgt at følge deres egne lyster og tager med glæde del i afskyelige handlinger. 4Men nu vil jeg også straffe dem og bringe al den ulykke over dem, som de håbede at undgå. For da jeg kaldte på dem, nægtede de at svare. Da jeg talte til dem, ville de ikke høre efter. I stedet syndede de lige op i mit åbne ansigt og handlede stik imod min vilje.

5Men hør, hvad jeg, Herren, har at sige til jer, som adlyder mig: De fra jeres eget folk, som hader jer og støder jer bort på grund af jeres loyalitet imod mig, håner jer og siger: ‚Få Herren til at vise sin herlighed, så vi kan se, hvad det er, I er så glade for.’ Men de vil blive ydmyget eftertrykkeligt.

6Hør et råb i byen, en høj lyd fra templet. Det er mig, Herren, der taler. Jeg vil gøre op med mine fjender.

7Jerusalem er som en kvinde, der pludselig føder et barn, så snart veerne begynder. 8Hvem har nogen sinde oplevet, hvad I nu ser med egne øjne? Fødes en nation på en enkelt dag? Fødes et folk på et øjeblik? Men sådan føder Jerusalem. Pludselig får hun veer og føder straks sine børn. 9Skulle jeg tillade svangerskab og så hindre fødslen? Skulle jeg afbryde en fødsel, jeg selv har sat i gang?” siger Herren.

10Glæd jer med Jerusalem. Vær glade på hendes vegne, alle I, som elsker hende, og som før har sørget over hende. 11Så skal I mættes ved hendes overflod og finde hvile som spædbarnet, der mættes og hviler trygt ved sin mors bryst. 12„Ja,” siger Herren, „jeg sender en flod af fred over hende tillige med en strøm af rigdom fra fremmede nationer. Hendes børn bæres på hoften, sidder på skødet og får kærtegn. 13Som en mor trøster sit barn, sådan trøster jeg jer. I vil finde trøst i Jerusalem.”

14Når I ser Jerusalems genrejsning, vil I juble af glæde, og I vil vokse jer sunde og raske. Da vil Guds tjenere erfare Herrens magt, og hans fjender vil smage hans vrede. 15For se, Herren kommer med lyn og tordenskrald, hans vrede er en fortærende ild, hans dom er et brølende flammehav. 16Herren vil straffe sine modstandere med ild og sværd i et vældigt blodbad.

17Herren siger: „De, som dyrker afguder i offerlundene, og som spiser svinekød og mus og andre urene dyr, vil blive udryddet. 18Jeg kender menneskets tanker og gerninger, og alle folkeslagene vil opleve min kraft og magt til at straffe dem. 19Jeg vil gøre et under iblandt dem, og dem, der undslipper, sender jeg ud til Tarshish, Pul, Lud (de berømte bueskytter), Tubal, Javan, og til de fjerne lande, der ikke har hørt om mig eller oplevet min kraft. De skal fortælle folkene om min herlighed, 20og de skal føre alle jeres brødre iblandt folkeslagene tilbage som et offer til mig. På heste, i vogne, i bærestole, på muldyr og kamelryg skal de komme til Jerusalem og mit hellige bjerg,” siger Herren. „De skal komme, som når israelitterne bringer offergaver i rene kar til mit tempel. 21Da vil jeg udpege nogle af dem, som er vendt hjem, til at være mine præster og levitter,” siger Herren.

22„Ligesom den nye himmel og den nye jord altid vil bestå, skal jeres slægt og efterkommere aldrig dø ud. 23Hver uge på sabbatten og hver den første i måneden skal alle mennesker komme for at tilbede mig,” siger Herren. 24„Og de skal gå ud og se på ligene af dem, som gjorde oprør imod mig. De ligger på lossepladsen, hvor ormene aldrig dør, og ilden aldrig slukkes. Synet af dem vil tjene til skræk og advarsel for alle.”