Maliro 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 1:1-22

1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,

umene kale unali wodzaza ndi anthu!

Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!

Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.

Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,

tsopano wasanduka kapolo.

2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,

misozi ili pa masaya pake.

Mwa abwenzi ake onse,

palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.

Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;

onse akhala adani ake.

3Yuda watengedwa ku ukapolo,

kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.

Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;

ndipo alibe malo opumulira.

Onse omuthamangitsa iye amupitirira,

ndipo alibe kwina kothawira.

4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,

chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.

Zipata zake zonse zili pululu,

ansembe akubuwula.

Anamwali ake akulira,

ndipo ali mʼmasautso woopsa.

5Adani ake asanduka mabwana ake;

odana naye akupeza bwino.

Yehova wamubweretsera mavuto

chifukwa cha machimo ake ambiri.

Ana ake atengedwa ukapolo

pamaso pa mdani.

6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni

wachokeratu.

Akalonga ake ali ngati mbawala

zosowa msipu;

alibe mphamvu zothawira

owathamangitsa.

7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,

Yerusalemu amakumbukira chuma chonse

chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.

Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,

panalibe aliyense womuthandiza.

Adani ake ankamuyangʼana

ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

8Yerusalemu wachimwa kwambiri

ndipo potero wakhala wodetsedwa.

Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,

chifukwa aona umaliseche wake.

Iye mwini akubuwula

ndipo akubisa nkhope yake.

9Uve wake umaonekera pa zovala zake;

iye sanaganizire za tsogolo lake.

Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;

ndipo analibe womutonthoza.

“Inu Yehova, taonani masautso anga,

pakuti mdani wapambana.”

10Adani amulanda

chuma chake chonse;

iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,

amene Inu Mulungu munawaletsa

kulowa mu msonkhano wanu.

11Anthu ake onse akubuwula

pamene akufunafuna chakudya;

asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya

kuti akhale ndi moyo.

“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,

chifukwa ine ndanyozeka.”

12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?

Yangʼanani ndipo muone.

Kodi pali mavuto ofanana ndi

amene andigwerawa,

amene Ambuye anandibweretsera

pa tsiku la ukali wake?

13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,

unalowa mpaka mʼmafupa anga.

Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga

ndipo anandibweza.

Anandisiya wopanda chilichonse,

wolefuka tsiku lonse.

14“Wazindikira machimo anga onse

ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.

Machimowa afika pakhosi panga,

ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.

Iye wandipereka

kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15“Ambuye wakana

anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:

wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,

kuti litekedze anyamata anga;

mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza

anamwali a Yuda.

16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira

ndipo maso anga adzaza ndi misozi.

Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,

palibe aliyense wondilimbitsa mtima.

Ana anga ali okhaokha

chifukwa mdani watigonjetsa.

17“Ziyoni wakweza manja ake,

koma palibe aliyense womutonthoza.

Yehova walamula kuti abale ake

a Yakobo akhale adani ake;

Yerusalemu wasanduka

chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18“Yehova ndi wolungama,

koma ndine ndinawukira malamulo ake.

Imvani inu anthu a mitundu yonse;

onani masautso anga.

Anyamata ndi anamwali anga

agwidwa ukapolo.

19“Ndinayitana abwenzi anga

koma anandinyenga.

Ansembe ndi akuluakulu anga

anafa mu mzinda

pamene ankafunafuna chakudya

kuti akhale ndi moyo.

20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!

Ndikuzunzika mʼkati mwanga,

ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa

chifukwa ndakhala osamvera.

Mʼmisewu anthu akuphedwa,

ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21“Anthu amva kubuwula kwanga,

koma palibe wonditonthoza.

Adani anga onse amva masautso anga;

iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.

Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija

kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;

muwalange

ngati mmene mwandilangira ine

chifukwa cha machimo anga onse.

Ndikubuwula kwambiri

ndipo mtima wanga walefuka.”

Bibelen på hverdagsdansk

Klagesangene 1:1-22

Jerusalem i sorg

1Ak ja, den travle by er nu folketom.

Den storslåede by sidder tilbage som en fattig enke.

Dronningen blandt byer blev degraderet til tjenestepige.

2Byen jamrer og græder natten lang.

Ingen kommer for at trøste hende i sorgen.

Alle de gamle venner har svigtet hende.

3Det judæiske folk blev mishandlet og ført bort som slaver.

De vansmægter nu i det fremmede uden at finde hvile.

De kunne ikke undslippe, da fjenden oversvømmede byen.

4Efter at templet blev ødelagt, er det forbi med højtid og fest.

Vejene op til Jerusalem er øde, og byens gader tomme.

Præsterne sørger, pigerne græder, hele byen er fortvivlet.

5Fjenderne gik af med sejren og plyndrede byen.

Det var Herrens straf for al folkets ulydighed.

Alle byens indbyggere blev ført bort som slaver.

6Glansen er fuldstændig gået af den før så herlige by.

Byens ledere var udhungrede som hjorte, der forgæves leder efter føde.

De var for udmattede til at undslippe deres forfølgere.

7Hjemløs og fattig sidder Jerusalem og mindes de skatte, hun1,7 Byer er i bibelsk poesi altid hunkøn. har mistet.

Ingen af hendes venner kom hende til hjælp mod fjendens angreb.

Hun blev hånet og spottet af den overlegne fjende.

8Ingen vil længere se op til Jerusalem, som de gjorde engang.

Hun blev ydmyget og plyndret på grund af sine mange synder.

Nu sidder hun og jamrer, afklædt og skamfuld.

9Jerusalem var utro mod Herren uden at tænke på følgerne.

Hun fik en frygtelig straf, og der er ingen, der trøster hende.

„Se min elendighed!” råber hun til Herren. „Min fjende foragter mig!”

10Katastrofen er ikke til at bære, for alt er tabt.

Ikke alene blev alle byens værdier plyndret,

men fremmede folkeslag brød ind i templet og vanhelligede det.

11Lidelsen ramte alle, som boede i byen.

Hungersnøden tvang dem til at sælge deres sidste ejendele for lidt mad.

Byen råber i sin nød: „Ak, Herre, se dog, hvor foragtet jeg er!

12Mon der findes en større smerte end min?

Hvad mener I, der står og ser på min ulykke?

Det er jo Herren selv, der har sendt sin straf.

13Nettet blev kastet ud over mig, og han fangede mig i fælden.

Dommen kom ned fra himlen som en fortærende ild.

Ensom og forladt sidder jeg her i min stadige pine.

14Om halsen på mig ligger en byrde, som tynger mig til jorden.

Alle mine synder har han lagt som et åg på mine skuldre.

Jeg kunne intet gøre mod de mægtige fjender, han sendte.

15På slagmarken ligger mine døde, tapre krigere.

Han sendte en mægtig hær mod mine unge soldater.

Han trampede på os, som man tramper druer i vinpersen.

16Resultatet er en stadig strøm af tårer.

Der er ingen til at trøste og hjælpe mig.

Alt er håbløst, for fjenden har besejret os totalt.”

17Selv om byen beder om nåde, er der ingen trøst at hente.

Det var Herren, der befalede nabofolkene at gå imod Israel.

De ser nu på Jerusalem som det værste skidt.

18„Trods mine lidelser,” siger Jerusalem, „ved jeg, at Herrens dom var retfærdig,

for vi gjorde oprør imod alle hans befalinger.

Forstå min smerte, alle I folkeslag: Mine indbyggere er ført bort som slaver.

19Uanset mit råb om hjælp blev jeg svigtet af mine nærmeste venner.

Mine præster og ledere bukkede under for hungersnøden,

forgæves søgte de efter mad nok til at overleve.

20Vær mig nådig, Herre, for jeg erkender min synd.

De, der vovede sig ud på gaden, blev dræbt af sværdet,

men de, der blev inde i husene, bukkede under for sulten.

21Ynkelige suk er alt, hvad jeg kan ytre, og der kommer ingen for at trøste mig.

Mine fjender fryder sig over den dom, du har afsagt over mig.

Gid du snart vil fælde dom over dem, ligesom du dømte mig.

22Åh, Herre, glem ikke al deres ondskab!

Straf dem, som du har straffet mig!

Mit hjerte er fuldt af sorg, og jeg sukker konstant.”