Yeremiya 51 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 51:1-64

1Yehova akuti,

“Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga

kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.

2Ndidzatuma alendo ku Babuloni

kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu.

Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse

pa tsiku la masautso ake.

3Okoka uta musawalekerere

kapena wonyadira chovala chawo chankhondo.

Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo;

koma muwononge ankhondo ake kotheratu.

4Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni

lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.

5Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye

ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse,

koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo

pamaso pa Woyerayo wa Israeli.

6“Thawaniko ku Babuloni!

Aliyense apulumutse moyo wake!

Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake.

Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange;

Yehova adzamulipsira.

7Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova;

kuti aledzeretse dziko lonse lapansi.

Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake;

nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.

8Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka.

Mulireni!

Mfunireni mankhwala opha ululu wake;

mwina iye nʼkuchira.”

9Ena anati, “ ‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni,

koma sanachire;

tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo,

pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga,

wafika mpaka kumwamba.’

10“ ‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa;

tiyeni tilengeze mu Ziyoni

zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’

11“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi,

popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni.

Motero adzalipsira Ababuloni

chifukwa chowononga Nyumba yake.

Ndiye Yehova akuti,

‘Nolani mivi, tengani zishango.’

12Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni!

Limbitsani oteteza,

ikani alonda pa malo awo,

konzekerani kulalira.

Pakuti Yehova watsimikiza

ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.

13Inu muli ndi mitsinje yambiri

ndi chuma chambiri.

Koma chimaliziro chanu chafika,

moyo wanu watha.

14Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti:

Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe,

kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.

15“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake;

Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake

ndipo anayala thambo mwaluso lake.

16Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba.

Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.

Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula

ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.

17“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru;

mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake.

Mafano akewo ndi abodza;

alibe moyo mʼkati mwawo.

18Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo.

Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.

19Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo.

Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse,

kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake.

Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

20“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga,

chida changa chankhondo.

Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu,

ndi iwe ndimawononga maufumu,

21ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo,

ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.

22Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi,

ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata,

ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.

23Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto,

ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe,

ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.

24“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.

25“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga,

amene umawononga dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

“Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga,

kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako,

ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.

26Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga

kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba,

chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,”

akutero Yehova.

27“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko!

Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu!

Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo;

itanani maufumu awa:

Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo.

Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye;

tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.

28Konzekeretsani mitundu ya anthu.

Amenewa ndiwo mafumu a Amedi,

abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo,

ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.

29Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira,

chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni;

kusakaza dziko la Babuloni

kuti musapezeke wokhalamo.

30Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo;

iwo angokhala mʼmalinga awo.

Mphamvu zawo zatheratu;

ndipo akhala ngati akazi.

Malo ake wokhala atenthedwa;

mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.

31Othamanga akungopezanapezana,

amithenga akungotsatanatsatana

kudzawuza mfumu ya ku Babuloni

kuti alande mzinda wake wonse.

32Madooko onse alandidwa,

malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto,

ndipo ankhondo onse asokonezeka.”

33Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu

pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti,

Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”

34A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga,

watiphwanya,

ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu.

Watimeza ngati ngʼona,

wakhuta ndi zakudya zathu zokoma,

kenaka nʼkutilavula.”

35Anthu a ku Ziyoni anene kuti,

“Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.”

Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti,

“Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”

36Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Taona, ndidzakumenyera nkhondo

ndi kukulipsirira;

ndidzawumitsa nyanja yake

ndipo akasupe ake adzaphwa.

37Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka,

malo okhala nkhandwe,

malo ochititsa mantha ndi onyozedwa,

malo wopanda aliyense wokhalamo.

38Anthu ake onse adzabangula ngati mkango,

adzadzuma ngati ana amkango.

39Ngati achita dyera

ndiye ndidzawakonzera madyerero

ndi kuwaledzeretsa,

kotero kuti adzasangalala,

kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,”

akutero Yehova.

40“Ine ndidzawatenga

kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa,

ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.

41“Ndithu Babuloni walandidwa,

mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa!

Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha

pakati pa mitundu ya anthu!

42Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni;

mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.

43Mizinda yake yasanduka bwinja,

dziko lowuma ndi lachipululu,

dziko losakhalamo wina aliyense,

dziko losayendamo munthu aliyense.

44Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni,

ndidzamusanzitsa zimene anameza.

Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye.

Malinga a Babuloni agwa.

45“Tulukani mʼBabuloni anthu anga!

Pulumutsani miyoyo yanu!

Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.

46Musataye mtima kapena kuchita mantha

pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu.

Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera

za ziwawa mʼdziko lapansi,

ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.

47Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu

pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni;

dziko lake lonse lidzachita manyazi

ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.

48Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo

zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni.

Anthu owononga ochokera kumpoto

adzamuthira nkhondo,”

akutero Yehova.

49“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi.

Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa

chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.

50Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni,

chokani pano ndipo musazengereze!

Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali,

ganizirani za Yerusalemu.”

51Inu mukuti, “Tikuchita manyazi,

chifukwa tanyozedwa

ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi,

chifukwa anthu achilendo alowa

malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”

52Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake,

ndipo mʼdziko lake lonse

anthu ovulala adzabuwula.

53Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga

ndi kulimbitsa nsanja zake,

ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,”

akutero Yehova.

54“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni.

Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu

kuchokera mʼdziko la Babuloni.

55Pakuti Yehova akuwononga Babuloni,

ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu.

Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri.

Phokoso lawo likunka likwererakwerera.

56Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni,

ankhondo ake agwidwa,

ndipo mauta awo athyoka.

Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango;

adzabwezera kwathunthu.

57Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake,

abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo;

adzagona kwamuyaya osadzukanso,”

akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

58Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa

ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa;

mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe.

Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”

59Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo. 60Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni. 61Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa. 62Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’ 63Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate. 64Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’ ”

Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

New International Version

Jeremiah 51:1-64

1This is what the Lord says:

“See, I will stir up the spirit of a destroyer

against Babylon and the people of Leb Kamai.51:1 Leb Kamai is a cryptogram for Chaldea, that is, Babylonia.

2I will send foreigners to Babylon

to winnow her and to devastate her land;

they will oppose her on every side

in the day of her disaster.

3Let not the archer string his bow,

nor let him put on his armor.

Do not spare her young men;

completely destroy51:3 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them. her army.

4They will fall down slain in Babylon,51:4 Or Chaldea

fatally wounded in her streets.

5For Israel and Judah have not been forsaken

by their God, the Lord Almighty,

though their land51:5 Or Almighty, / and the land of the Babylonians is full of guilt

before the Holy One of Israel.

6“Flee from Babylon!

Run for your lives!

Do not be destroyed because of her sins.

It is time for the Lord’s vengeance;

he will repay her what she deserves.

7Babylon was a gold cup in the Lord’s hand;

she made the whole earth drunk.

The nations drank her wine;

therefore they have now gone mad.

8Babylon will suddenly fall and be broken.

Wail over her!

Get balm for her pain;

perhaps she can be healed.

9“ ‘We would have healed Babylon,

but she cannot be healed;

let us leave her and each go to our own land,

for her judgment reaches to the skies,

it rises as high as the heavens.’

10“ ‘The Lord has vindicated us;

come, let us tell in Zion

what the Lord our God has done.’

11“Sharpen the arrows,

take up the shields!

The Lord has stirred up the kings of the Medes,

because his purpose is to destroy Babylon.

The Lord will take vengeance,

vengeance for his temple.

12Lift up a banner against the walls of Babylon!

Reinforce the guard,

station the watchmen,

prepare an ambush!

The Lord will carry out his purpose,

his decree against the people of Babylon.

13You who live by many waters

and are rich in treasures,

your end has come,

the time for you to be destroyed.

14The Lord Almighty has sworn by himself:

I will surely fill you with troops, as with a swarm of locusts,

and they will shout in triumph over you.

15“He made the earth by his power;

he founded the world by his wisdom

and stretched out the heavens by his understanding.

16When he thunders, the waters in the heavens roar;

he makes clouds rise from the ends of the earth.

He sends lightning with the rain

and brings out the wind from his storehouses.

17“Everyone is senseless and without knowledge;

every goldsmith is shamed by his idols.

The images he makes are a fraud;

they have no breath in them.

18They are worthless, the objects of mockery;

when their judgment comes, they will perish.

19He who is the Portion of Jacob is not like these,

for he is the Maker of all things,

including the people of his inheritance—

the Lord Almighty is his name.

20“You are my war club,

my weapon for battle—

with you I shatter nations,

with you I destroy kingdoms,

21with you I shatter horse and rider,

with you I shatter chariot and driver,

22with you I shatter man and woman,

with you I shatter old man and youth,

with you I shatter young man and young woman,

23with you I shatter shepherd and flock,

with you I shatter farmer and oxen,

with you I shatter governors and officials.

24“Before your eyes I will repay Babylon and all who live in Babylonia51:24 Or Chaldea; also in verse 35 for all the wrong they have done in Zion,” declares the Lord.

25“I am against you, you destroying mountain,

you who destroy the whole earth,”

declares the Lord.

“I will stretch out my hand against you,

roll you off the cliffs,

and make you a burned-out mountain.

26No rock will be taken from you for a cornerstone,

nor any stone for a foundation,

for you will be desolate forever,”

declares the Lord.

27“Lift up a banner in the land!

Blow the trumpet among the nations!

Prepare the nations for battle against her;

summon against her these kingdoms:

Ararat, Minni and Ashkenaz.

Appoint a commander against her;

send up horses like a swarm of locusts.

28Prepare the nations for battle against her—

the kings of the Medes,

their governors and all their officials,

and all the countries they rule.

29The land trembles and writhes,

for the Lord’s purposes against Babylon stand—

to lay waste the land of Babylon

so that no one will live there.

30Babylon’s warriors have stopped fighting;

they remain in their strongholds.

Their strength is exhausted;

they have become weaklings.

Her dwellings are set on fire;

the bars of her gates are broken.

31One courier follows another

and messenger follows messenger

to announce to the king of Babylon

that his entire city is captured,

32the river crossings seized,

the marshes set on fire,

and the soldiers terrified.”

33This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says:

“Daughter Babylon is like a threshing floor

at the time it is trampled;

the time to harvest her will soon come.”

34“Nebuchadnezzar king of Babylon has devoured us,

he has thrown us into confusion,

he has made us an empty jar.

Like a serpent he has swallowed us

and filled his stomach with our delicacies,

and then has spewed us out.

35May the violence done to our flesh51:35 Or done to us and to our children be on Babylon,”

say the inhabitants of Zion.

“May our blood be on those who live in Babylonia,”

says Jerusalem.

36Therefore this is what the Lord says:

“See, I will defend your cause

and avenge you;

I will dry up her sea

and make her springs dry.

37Babylon will be a heap of ruins,

a haunt of jackals,

an object of horror and scorn,

a place where no one lives.

38Her people all roar like young lions,

they growl like lion cubs.

39But while they are aroused,

I will set out a feast for them

and make them drunk,

so that they shout with laughter—

then sleep forever and not awake,”

declares the Lord.

40“I will bring them down

like lambs to the slaughter,

like rams and goats.

41“How Sheshak51:41 Sheshak is a cryptogram for Babylon. will be captured,

the boast of the whole earth seized!

How desolate Babylon will be

among the nations!

42The sea will rise over Babylon;

its roaring waves will cover her.

43Her towns will be desolate,

a dry and desert land,

a land where no one lives,

through which no one travels.

44I will punish Bel in Babylon

and make him spew out what he has swallowed.

The nations will no longer stream to him.

And the wall of Babylon will fall.

45“Come out of her, my people!

Run for your lives!

Run from the fierce anger of the Lord.

46Do not lose heart or be afraid

when rumors are heard in the land;

one rumor comes this year, another the next,

rumors of violence in the land

and of ruler against ruler.

47For the time will surely come

when I will punish the idols of Babylon;

her whole land will be disgraced

and her slain will all lie fallen within her.

48Then heaven and earth and all that is in them

will shout for joy over Babylon,

for out of the north

destroyers will attack her,”

declares the Lord.

49“Babylon must fall because of Israel’s slain,

just as the slain in all the earth

have fallen because of Babylon.

50You who have escaped the sword,

leave and do not linger!

Remember the Lord in a distant land,

and call to mind Jerusalem.”

51“We are disgraced,

for we have been insulted

and shame covers our faces,

because foreigners have entered

the holy places of the Lord’s house.”

52“But days are coming,” declares the Lord,

“when I will punish her idols,

and throughout her land

the wounded will groan.

53Even if Babylon ascends to the heavens

and fortifies her lofty stronghold,

I will send destroyers against her,”

declares the Lord.

54“The sound of a cry comes from Babylon,

the sound of great destruction

from the land of the Babylonians.51:54 Or Chaldeans

55The Lord will destroy Babylon;

he will silence her noisy din.

Waves of enemies will rage like great waters;

the roar of their voices will resound.

56A destroyer will come against Babylon;

her warriors will be captured,

and their bows will be broken.

For the Lord is a God of retribution;

he will repay in full.

57I will make her officials and wise men drunk,

her governors, officers and warriors as well;

they will sleep forever and not awake,”

declares the King, whose name is the Lord Almighty.

58This is what the Lord Almighty says:

“Babylon’s thick wall will be leveled

and her high gates set on fire;

the peoples exhaust themselves for nothing,

the nations’ labor is only fuel for the flames.”

59This is the message Jeremiah the prophet gave to the staff officer Seraiah son of Neriah, the son of Mahseiah, when he went to Babylon with Zedekiah king of Judah in the fourth year of his reign. 60Jeremiah had written on a scroll about all the disasters that would come upon Babylon—all that had been recorded concerning Babylon. 61He said to Seraiah, “When you get to Babylon, see that you read all these words aloud. 62Then say, ‘Lord, you have said you will destroy this place, so that neither people nor animals will live in it; it will be desolate forever.’ 63When you finish reading this scroll, tie a stone to it and throw it into the Euphrates. 64Then say, ‘So will Babylon sink to rise no more because of the disaster I will bring on her. And her people will fall.’ ”

The words of Jeremiah end here.