Yesaya 1 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

New International Version

Isaiah 1:1-31

1The vision concerning Judah and Jerusalem that Isaiah son of Amoz saw during the reigns of Uzziah, Jotham, Ahaz and Hezekiah, kings of Judah.

A Rebellious Nation

2Hear me, you heavens! Listen, earth!

For the Lord has spoken:

“I reared children and brought them up,

but they have rebelled against me.

3The ox knows its master,

the donkey its owner’s manger,

but Israel does not know,

my people do not understand.”

4Woe to the sinful nation,

a people whose guilt is great,

a brood of evildoers,

children given to corruption!

They have forsaken the Lord;

they have spurned the Holy One of Israel

and turned their backs on him.

5Why should you be beaten anymore?

Why do you persist in rebellion?

Your whole head is injured,

your whole heart afflicted.

6From the sole of your foot to the top of your head

there is no soundness—

only wounds and welts

and open sores,

not cleansed or bandaged

or soothed with olive oil.

7Your country is desolate,

your cities burned with fire;

your fields are being stripped by foreigners

right before you,

laid waste as when overthrown by strangers.

8Daughter Zion is left

like a shelter in a vineyard,

like a hut in a cucumber field,

like a city under siege.

9Unless the Lord Almighty

had left us some survivors,

we would have become like Sodom,

we would have been like Gomorrah.

10Hear the word of the Lord,

you rulers of Sodom;

listen to the instruction of our God,

you people of Gomorrah!

11“The multitude of your sacrifices—

what are they to me?” says the Lord.

“I have more than enough of burnt offerings,

of rams and the fat of fattened animals;

I have no pleasure

in the blood of bulls and lambs and goats.

12When you come to appear before me,

who has asked this of you,

this trampling of my courts?

13Stop bringing meaningless offerings!

Your incense is detestable to me.

New Moons, Sabbaths and convocations—

I cannot bear your worthless assemblies.

14Your New Moon feasts and your appointed festivals

I hate with all my being.

They have become a burden to me;

I am weary of bearing them.

15When you spread out your hands in prayer,

I hide my eyes from you;

even when you offer many prayers,

I am not listening.

Your hands are full of blood!

16Wash and make yourselves clean.

Take your evil deeds out of my sight;

stop doing wrong.

17Learn to do right; seek justice.

Defend the oppressed.1:17 Or justice. / Correct the oppressor

Take up the cause of the fatherless;

plead the case of the widow.

18“Come now, let us settle the matter,”

says the Lord.

“Though your sins are like scarlet,

they shall be as white as snow;

though they are red as crimson,

they shall be like wool.

19If you are willing and obedient,

you will eat the good things of the land;

20but if you resist and rebel,

you will be devoured by the sword.”

For the mouth of the Lord has spoken.

21See how the faithful city

has become a prostitute!

She once was full of justice;

righteousness used to dwell in her—

but now murderers!

22Your silver has become dross,

your choice wine is diluted with water.

23Your rulers are rebels,

partners with thieves;

they all love bribes

and chase after gifts.

They do not defend the cause of the fatherless;

the widow’s case does not come before them.

24Therefore the Lord, the Lord Almighty,

the Mighty One of Israel, declares:

“Ah! I will vent my wrath on my foes

and avenge myself on my enemies.

25I will turn my hand against you;1:25 That is, against Jerusalem

I will thoroughly purge away your dross

and remove all your impurities.

26I will restore your leaders as in days of old,

your rulers as at the beginning.

Afterward you will be called

the City of Righteousness,

the Faithful City.”

27Zion will be delivered with justice,

her penitent ones with righteousness.

28But rebels and sinners will both be broken,

and those who forsake the Lord will perish.

29“You will be ashamed because of the sacred oaks

in which you have delighted;

you will be disgraced because of the gardens

that you have chosen.

30You will be like an oak with fading leaves,

like a garden without water.

31The mighty man will become tinder

and his work a spark;

both will burn together,

with no one to quench the fire.”