Yeremiya 51 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 51:1-64

1Yehova akuti,

“Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga

kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.

2Ndidzatuma alendo ku Babuloni

kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu.

Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse

pa tsiku la masautso ake.

3Okoka uta musawalekerere

kapena wonyadira chovala chawo chankhondo.

Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo;

koma muwononge ankhondo ake kotheratu.

4Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni

lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.

5Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye

ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse,

koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo

pamaso pa Woyerayo wa Israeli.

6“Thawaniko ku Babuloni!

Aliyense apulumutse moyo wake!

Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake.

Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange;

Yehova adzamulipsira.

7Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova;

kuti aledzeretse dziko lonse lapansi.

Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake;

nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.

8Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka.

Mulireni!

Mfunireni mankhwala opha ululu wake;

mwina iye nʼkuchira.”

9Ena anati, “ ‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni,

koma sanachire;

tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo,

pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga,

wafika mpaka kumwamba.’

10“ ‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa;

tiyeni tilengeze mu Ziyoni

zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’

11“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi,

popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni.

Motero adzalipsira Ababuloni

chifukwa chowononga Nyumba yake.

Ndiye Yehova akuti,

‘Nolani mivi, tengani zishango.’

12Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni!

Limbitsani oteteza,

ikani alonda pa malo awo,

konzekerani kulalira.

Pakuti Yehova watsimikiza

ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.

13Inu muli ndi mitsinje yambiri

ndi chuma chambiri.

Koma chimaliziro chanu chafika,

moyo wanu watha.

14Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti:

Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe,

kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.

15“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake;

Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake

ndipo anayala thambo mwaluso lake.

16Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba.

Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.

Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula

ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.

17“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru;

mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake.

Mafano akewo ndi abodza;

alibe moyo mʼkati mwawo.

18Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo.

Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.

19Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo.

Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse,

kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake.

Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

20“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga,

chida changa chankhondo.

Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu,

ndi iwe ndimawononga maufumu,

21ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo,

ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.

22Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi,

ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata,

ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.

23Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto,

ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe,

ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.

24“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.

25“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga,

amene umawononga dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

“Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga,

kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako,

ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.

26Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga

kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba,

chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,”

akutero Yehova.

27“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko!

Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu!

Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo;

itanani maufumu awa:

Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo.

Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye;

tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.

28Konzekeretsani mitundu ya anthu.

Amenewa ndiwo mafumu a Amedi,

abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo,

ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.

29Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira,

chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni;

kusakaza dziko la Babuloni

kuti musapezeke wokhalamo.

30Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo;

iwo angokhala mʼmalinga awo.

Mphamvu zawo zatheratu;

ndipo akhala ngati akazi.

Malo ake wokhala atenthedwa;

mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.

31Othamanga akungopezanapezana,

amithenga akungotsatanatsatana

kudzawuza mfumu ya ku Babuloni

kuti alande mzinda wake wonse.

32Madooko onse alandidwa,

malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto,

ndipo ankhondo onse asokonezeka.”

33Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu

pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti,

Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”

34A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga,

watiphwanya,

ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu.

Watimeza ngati ngʼona,

wakhuta ndi zakudya zathu zokoma,

kenaka nʼkutilavula.”

35Anthu a ku Ziyoni anene kuti,

“Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.”

Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti,

“Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”

36Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Taona, ndidzakumenyera nkhondo

ndi kukulipsirira;

ndidzawumitsa nyanja yake

ndipo akasupe ake adzaphwa.

37Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka,

malo okhala nkhandwe,

malo ochititsa mantha ndi onyozedwa,

malo wopanda aliyense wokhalamo.

38Anthu ake onse adzabangula ngati mkango,

adzadzuma ngati ana amkango.

39Ngati achita dyera

ndiye ndidzawakonzera madyerero

ndi kuwaledzeretsa,

kotero kuti adzasangalala,

kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,”

akutero Yehova.

40“Ine ndidzawatenga

kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa,

ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.

41“Ndithu Babuloni walandidwa,

mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa!

Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha

pakati pa mitundu ya anthu!

42Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni;

mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.

43Mizinda yake yasanduka bwinja,

dziko lowuma ndi lachipululu,

dziko losakhalamo wina aliyense,

dziko losayendamo munthu aliyense.

44Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni,

ndidzamusanzitsa zimene anameza.

Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye.

Malinga a Babuloni agwa.

45“Tulukani mʼBabuloni anthu anga!

Pulumutsani miyoyo yanu!

Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.

46Musataye mtima kapena kuchita mantha

pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu.

Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera

za ziwawa mʼdziko lapansi,

ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.

47Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu

pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni;

dziko lake lonse lidzachita manyazi

ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.

48Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo

zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni.

Anthu owononga ochokera kumpoto

adzamuthira nkhondo,”

akutero Yehova.

49“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi.

Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa

chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.

50Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni,

chokani pano ndipo musazengereze!

Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali,

ganizirani za Yerusalemu.”

51Inu mukuti, “Tikuchita manyazi,

chifukwa tanyozedwa

ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi,

chifukwa anthu achilendo alowa

malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”

52Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake,

ndipo mʼdziko lake lonse

anthu ovulala adzabuwula.

53Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga

ndi kulimbitsa nsanja zake,

ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,”

akutero Yehova.

54“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni.

Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu

kuchokera mʼdziko la Babuloni.

55Pakuti Yehova akuwononga Babuloni,

ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu.

Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri.

Phokoso lawo likunka likwererakwerera.

56Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni,

ankhondo ake agwidwa,

ndipo mauta awo athyoka.

Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango;

adzabwezera kwathunthu.

57Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake,

abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo;

adzagona kwamuyaya osadzukanso,”

akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

58Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa

ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa;

mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe.

Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”

59Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo. 60Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni. 61Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa. 62Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’ 63Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate. 64Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’ ”

Mawu a Yeremiya athera pamenepa.