Yeremiya 47 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 47:1-7

Uthenga Wonena za Afilisti

1Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

2Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;

adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.

Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,

mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.

Anthu adzafuwula;

anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira

3akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,

phokoso la magaleta ake

ndi kulira kwa mikombero yake.

Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;

manja awo adzangoti khoba.

4Pakuti tsiku lafika

lowononga Afilisti onse

ndi kupha onse otsala,

onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.

Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,

otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.

5Anthu a ku Gaza ameta mipala;

anthu a ku Asikeloni akhala chete.

Inu otsala a ku chigwa,

mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

6“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,

kodi udzapumula liti?

Bwerera mʼmalo ako;

ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’

7Koma lupangalo lidzapumula bwanji

pamene Yehova walilamulira

kuti lithire nkhondo

Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 47:1-7

關於非利士的預言

1在法老攻打迦薩之前,耶和華告訴了耶利米先知有關非利士人的事。

2耶和華說:

「看啊,大水將從北方漲溢,

形成一道洪流,

淹沒大地和地上的一切,

吞噬城邑和其中的居民。

人們必呼喊,

地上的居民必哀哭。

3一聽見馬蹄噠噠、

戰車隆隆、車輪滾滾的聲音,

做父親的就嚇得手腳發軟,

無力照顧兒女。

4因為毀滅所有非利士人的日子到了,

剷除泰爾西頓剩餘幫手的日子到了。

耶和華要滅絕迦斐托島剩餘的非利士人。

5迦薩一片荒涼,

亞實基倫淪為廢墟。

谷中的餘民啊!

你們要割傷身體到何時呢?

6你們大喊,『耶和華的刀啊,

你何時才停下來呢?

求你入鞘吧!停下來吧!』

7但耶和華已命令它攻擊亞實基倫和沿海一帶,

它怎能停下來呢?」