Yeremiya 46 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 46:1-28

1Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.

Uthenga Wonena za Igupto

2Kunena za Igupto:

Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,

3anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo,

ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!

4Mangani akavalo,

ndipo kwerani inu okwerapo!

Khalani pa mzere

mutavala zipewa!

Nolani mikondo yanu,

valani malaya anu ankhondo!

5Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani?

Achita mantha

akubwerera,

ankhondo awo agonjetsedwa.

Akuthawa mofulumirapo

osayangʼananso mʼmbuyo,

ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,”

akutero Yehova.

6Waliwiro sangathe kuthawa

ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka.

Akunka napunthwa ndi kugwa

kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.

7“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo,

ngati mtsinje wa madzi amkokomo?

8Igupto akusefukira ngati Nailo,

ngati mitsinje ya madzi amkokomo.

Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi;

ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’

9Tiyeni, inu akavalo!

Thamangani inu magaleta!

Tulukani, inu ankhondo,

ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango,

ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.

10Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse;

tsiku lolipsira, lolipsira adani ake.

Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi,

lidzaledzera ndi magazi.

Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe

mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.

11“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala

iwe namwali Igupto.

Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira;

palibe mankhwala okuchiritsa.

12Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako;

kulira kwako kwadzaza dziko lapansi.

Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana,

onse awiri agwa pansi limodzi.”

13Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:

14“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli.

Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi.

Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza,

chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’

15Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa?

Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.

16Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa.

Aliyense akuwuza mnzake kuti,

‘Tiyeni tibwerere kwathu,

ku dziko kumene tinabadwira,

tithawe lupanga la adani athu.’

17Kumeneku iwo adzafuwula kuti,

‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti,

Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’

18“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu,

imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse,

“wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena,

ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.

19Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo

inu anthu a ku Igupto,

pakuti Mefisi adzasanduka chipululu

ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.

20“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola,

koma chimphanga chikubwera

kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.

21Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye

ali ngati ana angʼombe onenepa.

Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi.

Palibe amene wachirimika.

Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira;

ndiyo nthawi yowalanga.

22Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa

pamene adani abwera ndi zida zawo,

abwera ndi nkhwangwa

ngati anthu odula mitengo.

23Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,”

akutero Yehova,

“ngakhale kuti ndi yowirira.

Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe,

moti sangatheke kuwerengeka.

24Anthu a ku Igupto achita manyazi

atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”

25Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira. 26Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.

27“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha;

usataye mtima, iwe Israeli.

Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali,

ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere,

ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.

28Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha,

pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova.

“Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu

a ku mayiko kumene ndakupirikitsira,

Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu.

Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera;

sindidzakulekerera osakulanga.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 46:1-28

關於埃及的預言

1耶和華把有關列國的事告訴了耶利米先知。 2猶大約西亞的兒子約雅敬執政第四年,埃及王法老尼哥的軍隊在幼發拉底河邊的迦基米施巴比倫尼布甲尼撒擊敗。論到埃及,耶和華說:

3「要預備大小盾牌,

衝向戰場。

4要套好戰車,

騎上戰馬,

擦亮矛槍,

頂盔貫甲。

5可是,我看見的是什麼呢?

他們驚慌後退,

勇士敗逃,不敢回頭,

驚恐不安。

這是耶和華說的。

6善跑者跑不掉,

強壯者逃不了,

他們仆倒在北面的幼發拉底河邊。

7「那如尼羅河漲溢,

如江水奔騰的是誰呢?

8埃及尼羅河漲溢,

如江水奔騰。

她說,『我要漲溢,淹沒大地,

毀滅城邑和其中的居民。』

9戰馬奔馳吧!

戰車疾駛吧!

勇士啊,就是那些手拿盾牌的古實人和人以及箭法嫺熟的呂底亞人啊,出戰吧!

10因為這是主——萬軍之耶和華向敵人報仇的日子。

刀劍必吞噬他們,

痛飲他們的血,

因為要在北方的幼發拉底河邊向主——萬軍之耶和華獻祭。

11埃及人啊,

基列取乳香吧!

然而,再多的良藥也無法醫治你們。

12你們的恥辱傳遍列國,

你們的哀哭響徹大地,

你們的勇士彼此碰撞,

倒在一起。」

13論到巴比倫尼布甲尼撒要來攻打埃及的事,耶和華對耶利米先知說:

14「你要在埃及宣佈,在密奪挪弗答比匿宣告,

『你們要準備戰鬥,

因為刀劍要吞噬你們周圍的人。』

15你們的勇士為何仆倒?

他們無法堅立,

因為耶和華擊倒了他們,

16使他們跌跌絆絆,紛紛倒下。

他們說,『起來,我們回到同胞那裡,回到故鄉吧,

好躲避敵人的刀劍。』

17他們在那裡喊叫,

埃及王法老只會虛張聲勢,

他已錯失良機。』」

18名叫萬軍之耶和華的王說:

「我憑我的永恆起誓,

將有一位要來,

他的氣勢如群山中的他泊山,

又像海邊的迦密山。

19住在埃及的子民啊,

收拾行裝準備流亡吧!

因為挪弗必被燒毀,

淪為廢墟,杳無人跡。

20埃及像頭肥美的母牛犢,

但從北方卻來了牛虻。

21埃及的傭兵好像肥牛犢,

都轉身逃之夭夭,無力抵擋,

因為他們遭難、受罰的日子到了。

22「敵軍進攻的時候,

埃及必像蛇一樣嘶嘶地溜走。

敵軍必拿著斧頭蜂擁而來,

像樵夫砍樹一樣攻擊他們。

23埃及的人口雖然稠密如林,

敵軍必像無數的蝗蟲一樣掃平他們。

這是耶和華說的。

24埃及人必蒙羞,

落在北方人的手中。」

25以色列的上帝——萬軍之耶和華說:「看啊,我要懲罰提比斯的神明亞捫埃及的其他神明、法老、首領以及依靠法老的人。 26我要把他們交在想殺他們的巴比倫尼布甲尼撒及其官長手中。然而,日後埃及必再有人居住,如往日一樣。這是耶和華說的。

27「我的僕人雅各啊,不要害怕!

以色列人啊,不要驚慌!

因為我要從遠方把你們救回來,

使你們從流亡之地歸回。

你們必重返家園,安享太平,

無人攪擾。

28我的僕人雅各啊,不要害怕,

因為我與你同在。

我曾使你流亡到列國,

我必徹底毀滅列國,

但不會徹底毀滅你,

也不會饒過你,

我必公正地懲治你。

這是耶和華說的。」