Yeremiya 48 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 48:1-47

Uthenga Wonena za Mowabu

1Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.

Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;

linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.

2Palibenso amene akutamanda Mowabu;

ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:

‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’

Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;

ankhondo adzakupirikitsani.

3Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.

Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’

4Mowabu wawonongeka;

ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.

5Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,

akulira kwambiri pamene akupita.

Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka

pa njira yotsikira ku Horonaimu.

6Thawani! Dzipulumutseni;

khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.

7Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,

nanunso mudzatengedwa ukapolo,

ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.

8Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,

ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.

Chigwa chidzasanduka bwinja

ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa

monga Yehova wayankhulira.

9Mtsineni khutu Mowabu

chifukwa adzasakazika;

mizinda yake idzasanduka mabwinja,

wopanda munthu wokhalamo.

10“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!

Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,

ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,

osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;

iye sanatengedwepo ukapolo.

Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja

ndipo fungo lake silinasinthe.

12Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko

ndipo adzamukhutula;

adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake

pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.

13Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,

monga momwe Aisraeli anachitira manyazi

ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.

Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’

15Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;

anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”

ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;

masautso ake akubwera posachedwa.

17Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,

inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;

nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,

taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18“Tsikani pa ulemerero wanu

ndipo khalani pansi powuma,

inu anthu okhala ku Diboni,

pakuti wowononga Mowabu

wabwera kudzamenyana nanu,

wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.

19Inu amene mumakhala ku Aroeri,

imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.

Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,

afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”

20Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.

Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!

Lengezani ku mtsinje wa Arinoni

kuti Mowabu wawonongedwa.

21Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,

ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,

22Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,

23Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,

24Keriyoti ndi Bozira

ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.

25Mphamvu za Mowabu zawonongeka;

mkono wake wathyoka,”

akutero Yehova.

26“Muledzeretseni Mowabu,

chifukwa anadzikuza powukira Yehova.

Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;

mulekeni akhale chinthu chomachiseka.

27Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?

Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba

kuti nthawi zonse poyankhula za iye,

iwe uzimupukusira mutu momunyoza?

28Inu amene mumakhala ku Mowabu,

siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.

Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake

pa khomo la phanga.

29“Tamva za kunyada kwa Mowabu,

kunyada kwake nʼkwakukulu.

Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.

Ali ndi mtima wodzikweza.

30Ine ndikuzidziwa ntchito zake,

akutero Yehova.

Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.

31Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,

ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,

ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.

32Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.

Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa

imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;

zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.

Wowononga wasakaza

zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.

33Chimwemwe ndi chisangalalo zatha

ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.

Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;

palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.

Ngakhale kufuwula kulipo,

koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira

ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,

kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.

Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.

35Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu

kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera

ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”

akutero Yehova.

36“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.

Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro

chifukwa chuma chimene anachipata chatha.

37Aliyense wameta mutu wake

ndi ndevu zake;

manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,

ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.

38Pa madenga onse a ku Mowabu

ndiponso mʼmisewu yake

anthu akungolira,

pakuti ndaphwanya Mowabu

ngati mtsuko wopanda ntchito,”

akutero Yehova.

39“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!

Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.

Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,

chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga

chimene chatambalitsa mapiko ake.

41Mizinda idzagwidwa

ndipo malinga adzalandidwa.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu

idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

42Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu

chifukwa unadzikuza powukira Yehova.

43Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira

inu anthu a ku Mowabu,”

akutero Yehova.

44“Aliyense wothawa zoopsa

adzagwera mʼdzenje,

aliyense wotuluka mʼdzenje

adzakodwa mu msampha.

Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu

pa nthawi ya chilango chake,”

akutero Yehova.

45“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni

chifukwa chotopa.

Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,

malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.

Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,

dziko la anthu onyada.

46Tsoka kwa iwe Mowabu!

Anthu opembedza Kemosi awonongeka.

Ana ako aamuna ndi aakazi

atengedwa ukapolo.

47“Komabe masiku akutsogolo

ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”

akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 48:1-47

關於摩押的預言

1論到摩押以色列的上帝——萬軍之耶和華說:

尼波大禍臨頭了!

它必被毀滅;

基列亭必蒙羞淪陷,

堡壘必蒙羞被毀。

2摩押不再受稱讚,

敵人在希實本圖謀害她,說,

『來吧!我們剷除這個國家。』

瑪得緬啊,你也將被敵人追殺,

變得死寂無聲。

3「從何羅念傳來呼喊聲,

『荒涼了!毀滅了!』

4摩押滅亡了,

她的孩童放聲哀哭。

5摩押人痛哭著走上魯希坡,

他們在何羅念的山坡下聽見悲慘的哀號。

6逃命吧!藏到曠野去吧!

7摩押啊,你要被攻佔,

因為你倚仗自己的成就和財富。

你的神明基抹及供奉它的祭司和官長都要被擄去。

8所有的城邑必被毀滅,

無一倖免;

山谷遭踐踏,

平原被蹂躪。

這是耶和華說的。

9「給摩押翅膀讓她飛走吧48·9 給摩押翅膀讓她飛走吧,」或譯作「給摩押豎起墓碑吧,因為她將被毀滅」或「在摩押撒鹽吧,因為她將被毀滅」。

因為她的城邑將淪為廢墟,

杳無人跡。

10不殷勤地為耶和華做工,

不揮刀斬殺摩押人的必受咒詛。

11摩押自幼常享安逸,

從未被擄到別處,

好像沉澱的酒沒有被從這缸倒到那缸,

味道依舊,香氣未變。

12「不過,看啊,時候將到,我要派倒酒的人去把她倒出來,倒空酒缸,把缸打碎。這是耶和華說的。 13摩押人必因他們的神明基抹而羞愧,就像以色列人因信靠伯特利的神像而羞愧一樣。

14摩押人啊,

你們怎能自稱為驍勇善戰的英雄呢?

15摩押要滅亡了,

她的城邑要被摧毀,

她最勇敢的青年將被殺戮。

這是名叫萬軍之耶和華的君王說的。

16摩押快要被毀滅了,

災難就要來臨。

17她的近鄰和知道她名望的人啊,

你們都要為她哀悼,

『那強大、輝煌的權勢竟然崩潰了!』

18底本的居民啊,

你們要從榮耀的位子上下來,

坐在乾旱的地上,

因為毀滅摩押的要來攻擊你們,

摧毀你們的堡壘。

19亞羅珥的居民啊!

你們要站在路旁觀望,

詢問逃難的男女究竟發生了什麼事。

20你們會得知摩押淪陷了,

她羞愧難當。

你們哀傷痛哭吧!

你們要在亞嫩河邊宣告,

摩押滅亡了!』

21「審判降臨在平原上的何倫雅雜米法押22底本尼波伯·低比拉太音23基列亭伯·迦末伯·米恩24加略波斯拉摩押各地的城邑。 25摩押的權勢被粉碎了,她的力量被摧毀了。這是耶和華說的。

26「你們要灌醉她,因為她藐視耶和華。她必在自己的嘔吐物中打滾,被人恥笑。 27摩押啊,你不是曾經嘲笑以色列嗎?以色列難道是強盜嗎?你每次談到她總是不屑地搖頭。

28摩押人啊,

你們要離開城邑,住到岩洞裡,

像鴿子在岩縫裡築巢一樣。

29我們聽說摩押人傲氣沖天,

他們狂妄自大、心中高傲。

30我知道狂傲的摩押不過是外強中乾,

她的誇耀不過是虛張聲勢。

這是耶和華說的。

31因此,我要為她哀號,

摩押人痛哭,

吉珥·哈列設人悲傷。

32西比瑪的葡萄樹啊,

我為你們比為雅謝人哭得更悲痛!

你們的枝條雖然延伸到大海,

一直到雅謝

但毀滅者已在蹂躪你們夏日的果子了!

33摩押的沃土上再沒有歡喜快樂的聲音。

我使榨酒池不出酒,

再沒有踩踏葡萄的歡呼聲,

歡呼被呐喊取代。

34「哀哭聲從希實本傳到以利亞利雅雜,又從瑣珥傳到何羅念伊基拉·施利施亞,因為連寧林的水也乾涸了。」 35耶和華說:「我要滅絕摩押那些在邱壇獻祭和向假神燒香的人。 36我的心為摩押悲鳴,好像淒涼的簫聲;我的心為吉珥·哈列設人悲鳴,他們的一切財富都消失了。 37他們都悲哀地剃去髮鬚,割傷雙手,腰束麻布。 38摩押境內的屋頂和街頭巷尾,哀聲處處可聞,因為我已把摩押打得粉碎,好像打碎沒人要的器皿。這是耶和華說的。 39摩押破碎不堪!她嚎啕痛哭,羞愧難當,令四圍的人嗤笑、驚懼。」

40耶和華說:

「看啊,敵人必像展翅疾飛的大鷹一樣來攻擊摩押

41他們要攻取城池,佔領堡壘。

那時,摩押的勇士像臨盆的婦人一樣心驚膽戰。

42摩押必被摧毀,徹底滅亡,

因為她藐視耶和華。

43摩押人啊!

你們要充滿恐懼,

陷入深坑和網羅。

這是耶和華說的。

44逃過驚恐的必落入深坑,

爬出深坑的必陷入網羅,

因為我懲罰摩押的時候到了。

這是耶和華說的。

45「逃難的人來到希實本

無助地站著,

因為希實本烈焰熊熊,

西宏的城火光沖天,

燒毀了摩押和其中的叛逆之人。

46基抹神明的摩押人啊,

你們有禍了!

你們滅亡了!

你們的兒女都被擄去了。

47但將來,我要使你們重整家園。

這是耶和華說的。」

摩押的審判到此為止。