Nyimbo ya Solomoni 4 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 4:1-16

Mwamuna

1Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga!

Ndithudi, ndiwe wokongola!

Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

2Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene,

zochokera kozisambitsa kumene.

Iliyonse ili ndi ana amapasa;

palibe imene ili yokha.

3Milomo yako ili ngati mbota yofiira;

pakamwa pako ndi pokongola kwambiri.

Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba

kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.

4Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide,

yomangidwa bwino ndi yosalala;

pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000,

zishango zonsezo za anthu ankhondo.

5Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala,

ngati ana amapasa a nswala

amene akudya pakati pa maluwa okongola.

6Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

ndidzapita ku phiri la mure

ndi ku chitunda cha lubani.

7Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga;

palibe chilema pa iwe.

8Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga,

tiye tichoke ku Lebanoni,

utsikepo pa msonga ya Amana,

kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni,

kuchoka ku mapanga a mikango

ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.

9Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima,

iwe wanditenga mtima

ndi kapenyedwe ka maso ako,

ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.

10Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa!

Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo,

ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!

11Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi;

pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi.

Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.

12Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa;

ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.

13Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza;

muli zipatso zokoma kwambiri,

muli hena ndi nadi,

14nadi ndi safiro,

kalamusi ndi sinamoni,

komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino.

Mulinso mure ndi aloe

ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.

15Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda,

chitsime cha madzi oyenda,

mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.

Mkazi

16Dzuka, iwe mphepo yakumpoto,

ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera!

Uzira pa munda wanga,

kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse.

Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake

ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.

New International Version

Song of Songs 4:1-16

He

1How beautiful you are, my darling!

Oh, how beautiful!

Your eyes behind your veil are doves.

Your hair is like a flock of goats

descending from the hills of Gilead.

2Your teeth are like a flock of sheep just shorn,

coming up from the washing.

Each has its twin;

not one of them is alone.

3Your lips are like a scarlet ribbon;

your mouth is lovely.

Your temples behind your veil

are like the halves of a pomegranate.

4Your neck is like the tower of David,

built with courses of stone4:4 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.;

on it hang a thousand shields,

all of them shields of warriors.

5Your breasts are like two fawns,

like twin fawns of a gazelle

that browse among the lilies.

6Until the day breaks

and the shadows flee,

I will go to the mountain of myrrh

and to the hill of incense.

7You are altogether beautiful, my darling;

there is no flaw in you.

8Come with me from Lebanon, my bride,

come with me from Lebanon.

Descend from the crest of Amana,

from the top of Senir, the summit of Hermon,

from the lions’ dens

and the mountain haunts of leopards.

9You have stolen my heart, my sister, my bride;

you have stolen my heart

with one glance of your eyes,

with one jewel of your necklace.

10How delightful is your love, my sister, my bride!

How much more pleasing is your love than wine,

and the fragrance of your perfume

more than any spice!

11Your lips drop sweetness as the honeycomb, my bride;

milk and honey are under your tongue.

The fragrance of your garments

is like the fragrance of Lebanon.

12You are a garden locked up, my sister, my bride;

you are a spring enclosed, a sealed fountain.

13Your plants are an orchard of pomegranates

with choice fruits,

with henna and nard,

14nard and saffron,

calamus and cinnamon,

with every kind of incense tree,

with myrrh and aloes

and all the finest spices.

15You are4:15 Or I am (spoken by She) a garden fountain,

a well of flowing water

streaming down from Lebanon.

She

16Awake, north wind,

and come, south wind!

Blow on my garden,

that its fragrance may spread everywhere.

Let my beloved come into his garden

and taste its choice fruits.