Nyimbo ya Solomoni 3 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 3:1-11

1Usiku wonse ndili pa bedi langa

ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;

ndinamufunafuna koma osamupeza.

2Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,

mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;

ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.

Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.

3Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzinda.

“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”

4Nditawapitirira pangʼono

ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.

Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke

mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

mʼchipinda cha amene anandibereka.

5Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

6Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu

ngati utsi watolotolo,

wonunkhira mure ndi lubani,

zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?

7Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,

choperekezedwa ndi asilikali 60,

anthu amphamvu a ku Israeli,

8onse atanyamula lupanga,

onse odziwa bwino nkhondo,

aliyense ali ndi lupanga pambali pake,

kukonzekera zoopsa za usiku.

9Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;

anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.

10Milongoti yake anayipanga yasiliva,

kumbuyo kwake kwa golide.

Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,

anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi

cha akazi a ku Yerusalemu.

11Tukulani inu akazi a ku Ziyoni

ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,

chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka

pa tsiku la ukwati wake,

tsiku limene mtima wake unasangalala.

New International Version

Song of Songs 3:1-11

1All night long on my bed

I looked for the one my heart loves;

I looked for him but did not find him.

2I will get up now and go about the city,

through its streets and squares;

I will search for the one my heart loves.

So I looked for him but did not find him.

3The watchmen found me

as they made their rounds in the city.

“Have you seen the one my heart loves?”

4Scarcely had I passed them

when I found the one my heart loves.

I held him and would not let him go

till I had brought him to my mother’s house,

to the room of the one who conceived me.

5Daughters of Jerusalem, I charge you

by the gazelles and by the does of the field:

Do not arouse or awaken love

until it so desires.

6Who is this coming up from the wilderness

like a column of smoke,

perfumed with myrrh and incense

made from all the spices of the merchant?

7Look! It is Solomon’s carriage,

escorted by sixty warriors,

the noblest of Israel,

8all of them wearing the sword,

all experienced in battle,

each with his sword at his side,

prepared for the terrors of the night.

9King Solomon made for himself the carriage;

he made it of wood from Lebanon.

10Its posts he made of silver,

its base of gold.

Its seat was upholstered with purple,

its interior inlaid with love.

Daughters of Jerusalem, 11come out,

and look, you daughters of Zion.

Look3:10,11 Or interior lovingly inlaid / by the daughters of Jerusalem. / 11 Come out, you daughters of Zion, / and look on King Solomon wearing a crown,

the crown with which his mother crowned him

on the day of his wedding,

the day his heart rejoiced.