Nyimbo ya Solomoni 5 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 5:1-16

Mwamuna

1Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;

ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.

Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;

ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.

Abwenzi

Idyani abwenzi anga, imwani;

Inu okondana, imwani kwambiri.

Mkazi

2Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.

Tamverani, bwenzi langa akugogoda:

“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,

nkhunda yanga, wangwiro wanga.

Mutu wanga wanyowa ndi mame,

tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”

3Ndavula kale zovala zanga,

kodi ndizivalenso?

Ndasamba kale mapazi anga

kodi ndiwadetsenso?

4Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;

mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.

5Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,

ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,

zala zanga zinali mure chuchuchu,

pa zogwirira za chotsekera.

6Ndinamutsekulira wachikondi wanga,

koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.

Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.

Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.

Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.

7Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzindawo.

Anandimenya ndipo anandipweteka;

iwo anandilanda mwinjiro wanga,

alonda a pa khoma aja!

8Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,

mukapeza wokondedwa wangayo,

kodi mudzamuwuza chiyani?

Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.

Abwenzi

9Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?

Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani

kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi

pakati pa anthu 1,000.

11Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;

tsitsi lake ndi lopotanapotana,

ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.

12Maso ake ali ngati nkhunda

mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,

zitayima ngati miyala yamtengowapatali.

13Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya

zopatsa fungo lokoma.

Milomo yake ili ngati maluwa okongola

amene akuchucha mure.

14Manja ake ali ngati ndodo zagolide

zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.

Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu

woyikamo miyala ya safiro.

15Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,

yokhazikika pa maziko a golide.

Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,

abwino kwambiri ngati mkungudza.

16Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;

munthuyo ndi wokongola kwambiri!

Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,

inu akazi a ku Yerusalemu.

New International Version

Song of Songs 5:1-16

He

1I have come into my garden, my sister, my bride;

I have gathered my myrrh with my spice.

I have eaten my honeycomb and my honey;

I have drunk my wine and my milk.

Friends

Eat, friends, and drink;

drink your fill of love.

She

2I slept but my heart was awake.

Listen! My beloved is knocking:

“Open to me, my sister, my darling,

my dove, my flawless one.

My head is drenched with dew,

my hair with the dampness of the night.”

3I have taken off my robe—

must I put it on again?

I have washed my feet—

must I soil them again?

4My beloved thrust his hand through the latch-opening;

my heart began to pound for him.

5I arose to open for my beloved,

and my hands dripped with myrrh,

my fingers with flowing myrrh,

on the handles of the bolt.

6I opened for my beloved,

but my beloved had left; he was gone.

My heart sank at his departure.5:6 Or heart had gone out to him when he spoke

I looked for him but did not find him.

I called him but he did not answer.

7The watchmen found me

as they made their rounds in the city.

They beat me, they bruised me;

they took away my cloak,

those watchmen of the walls!

8Daughters of Jerusalem, I charge you—

if you find my beloved,

what will you tell him?

Tell him I am faint with love.

Friends

9How is your beloved better than others,

most beautiful of women?

How is your beloved better than others,

that you so charge us?

She

10My beloved is radiant and ruddy,

outstanding among ten thousand.

11His head is purest gold;

his hair is wavy

and black as a raven.

12His eyes are like doves

by the water streams,

washed in milk,

mounted like jewels.

13His cheeks are like beds of spice

yielding perfume.

His lips are like lilies

dripping with myrrh.

14His arms are rods of gold

set with topaz.

His body is like polished ivory

decorated with lapis lazuli.

15His legs are pillars of marble

set on bases of pure gold.

His appearance is like Lebanon,

choice as its cedars.

16His mouth is sweetness itself;

he is altogether lovely.

This is my beloved, this is my friend,

daughters of Jerusalem.