Miyambo 21 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 21:1-31

1Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova;

Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.

2Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo,

koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.

3Za chilungamo ndi zolondola

ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.

4Maso odzikuza ndi mtima wonyada,

zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.

5Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake;

koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.

6Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa

ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

7Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga,

pakuti iwo amakana kuchita zolungama.

8Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota,

koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.

9Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba,

kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.

10Munthu woyipa amalakalaka zoyipa;

sachitira chifundo mnansi wake wovutika.

11Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru;

koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.

12Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova,

ndipo Iye adzawononga woyipayo.

13Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira,

nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.

14Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo,

ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.

15Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala,

koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.

16Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru

adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.

17Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi,

ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama

ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.

19Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu

kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.

20Munthu wanzeru samwaza chuma chake,

koma wopusa amachiwononga.

21Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika,

amapeza moyo ndi ulemerero.

22Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu

ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.

23Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake

sapeza mavuto.

24Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,”

iye amachita zinthu modzitama kwambiri.

25Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha

chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.

26Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri,

koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.

27Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova,

nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!

28Mboni yonama idzawonongeka,

koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.

29Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima,

koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.

30Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu,

zimene zingapambane Yehova.

31Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo,

koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

New Russian Translation

Притчи 21:1-31

1Как поток воды, сердце царя в руке Господней:

куда Он захочет, туда его и направит.

2Все пути человека пред глазами его прямы,

но Господь испытывает сердца.

3Кто поступает праведно и справедливо –

угодней Господу, нежели приносящий жертвы.

4Надменный взгляд и гордое сердце –

как светильник для нечестивого, но это грех.

5Замыслы усердного принесут изобилие,

а всякий торопливый лишь обнищает.

6Состояние, нажитое лживым языком, –

это тающий пар ищущих смерти21:6 В некоторых рукописях еврейского текста и в некоторых древних переводах: «смертоносная западня»..

7Жестокость злодеев их же и погубит,

ведь они отказываются поступать справедливо.

8Путь преступных извилист,

а поступки невинных чисты.

9Лучше жить на углу крыши,

чем делить дом со сварливой женой.

10Нечестивый желает зла,

милости ближний у него не найдет.

11Когда наказан глумливый, простаки становятся мудрее;

когда наставлен мудрец, он обретает знание.

12Праведник примечает дом нечестивца

и насылает на нечестивца гибель.

13Если кто затыкает уши от крика бедных,

то он однажды сам будет кричать, и его не услышат.

14Тайный подарок предотвращает гнев,

и взятка, скрытая под плащом, – лютую ярость.

15Радость праведным, когда вершат правосудие,

но ужас злодеям.

16Тот, кто сошел с пути разума,

упокоится в обществе мертвецов21:16 Евр.: «рефаим»..

17Любящий развлечения обеднеет,

любящий вино и дорогие мази21:17 Дорогие мази – или «дорогую еду». не разбогатеет.

18Нечестивым праведника выкупают,

а вероломным – верного.

19Лучше жить в пустыне,

чем со сварливой и злобной женой.

20Дорогое добро и масло остается в доме у мудрого,

а глупец его проедает.

21Стремящийся к праведности и любви

найдет и жизнь, и праведность, и славу.

22Один мудрец может покорить город, полный воинов,

и низвергнуть крепость, на которую они полагались.

23Сторожащий уста свои и язык

хранит себя от беды.

24Гордец надменный, «глумливый» – имя ему;

он действует в чрезмерной гордыне.

25Желания ленивца его умертвят,

так как руки его отказываются трудиться.

26День напролет он жаждет и желает,

а праведный дает не жалея.

27Жертва злодеев – мерзость,

тем паче, когда приносится со злым умыслом.

28Лживый свидетель погибнет,

свидетельство того, кто все слышал, устоит21:28 Букв.: «человек, который слышит, будет говорить вовек»..

29Нечестивый делает уверенное лицо,

а праведный обдумывает свой путь21:29 Или: «твердо идет по своему пути»..

30Нет ни мудрости, ни разума, ни замысла,

что имели бы успех против Господа.

31Коня готовят на день сражения,

а победу дает Господь.