Miyambo 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 22:1-29

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;

kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.

2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;

onsewa anawalenga ndi Yehova.

3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.

4Mphotho ya munthu wodzichepetsa

ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.

5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,

koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.

6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,

ndipo akadzakalamba sadzachokamo.

7Wolemera amalamulira wosauka,

ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.

8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,

ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.

9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,

pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.

10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;

mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.

11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,

adzakhala bwenzi la mfumu.

12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,

koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.

13Munthu waulesi amati,

“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”

14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;

amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.

15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,

koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.

16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,

ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;

uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.

18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako

ndi wokonzeka kuziyankhula.

19Ndakuphunzitsa zimenezi lero

koma makamaka uziopa Yehova.

20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu

okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,

21malangizo okudziwitsa zolungama

ndi zoona

ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?

22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,

ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,

23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo

ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.

24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima

ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya

25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake

ndi kukodwa mu msampha.

26Usakhale munthu wopereka chikole

kapena kukhala mboni pa ngongole;

27ngati ulephera kupeza njira yolipirira

adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.

28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale

amene anayikidwa ndi makolo ako.

29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?

Iye adzatumikira mafumu;

sadzatumikira anthu wamba.

New Russian Translation

Притчи 22:1-29

1Доброе имя великих богатств желаннее;

добрая слава лучше серебра и золота.

2Богач и нищий вот чем сродни:

их обоих создал Господь.

3Разумный увидит опасность – и скроется,

а простаки пойдут дальше – и пострадают.

4Награда за смирение и страх перед Господом –

богатство, и слава, и жизнь.

5На пути коварных – колючки да западни:

дорожащий жизнью к ним и не подойдет.

6Наставь ребенка на верный путь22:6 Или: «Наставь ребенка в начале его пути».,

он и в старости не собьется с него.

7Богатые властвуют над бедными,

и должник заимодавцу раб.

8Сеющий беззаконие пожнет беду,

и не станет жезла его гнева.

9Человек щедрый22:9 Букв.: «Имеющий приятный глаз» – фразеологический оборот, обозначающий человека щедрого, в отличие от человека скупого, имеющего «дурной глаз» (см. сноску на 23:6). будет благословен,

так как пищей делится с бедным.

10Прогони глумливого – уйдет и вражда,

и утихнут раздоры и ругань.

11Кто любит чистоту сердца, чья речь любезна,

тому царь будет другом.

12Очи Господа охраняют знание,

а слова вероломного Он опровергает.

13Лентяй говорит: «На улице лев!

Смерть мне, ежели выйду!»

14Уста чужой жены22:14 Букв.: «чужих женщин». – глубокая яма,

прогневавший Господа туда упадет.

15Глупость привязана к сердцу ребенка,

но прогонит ее исправляющая розга.

16Притесняющий бедных, чтобы обогатиться,

и дающий богатым подарки обнищают.

Тридцать изречений мудрецов

17Приклони ухо свое и слова мудрецов послушай,

сердце к учению моему обрати;

18если ты сохранишь их в себе,

если все они будут у тебя на устах,

то это будет приятно.

19Чтобы ты мог надеяться на Господа,

я сегодня учу им тебя, да, тебя.

20Разве я не написал для тебя тридцать изречений22:20 Смысл этого места в еврейском тексте неясен.

увещевания и знания,

21чтобы ты научился верным словам истины

и смог принести верный ответ посылавшим тебя?

22Не обирай бедных лишь потому, что они бедны;

не притесняй нуждающихся на суде22:22 На суде – букв.: «у ворот». Ворота были местом, где собирались старейшины города. Там проводились судебные разбирательства, официальные церемонии, заключались договоры и торговые сделки.,

23дело их защитит Господь,

жизнь отберет у тех, кто их обирает.

24Не дружи с гневливым,

с раздражительным не общайся,

25чтобы не научиться его путям

и не попасть в западню.

26Не будь одним из тех, кто дает залог

и поручается за долги;

27когда не найдешь ты, чем заплатить,

даже постель из-под тебя заберут.

28Не передвигай древней межи,

которую поставили твои предки22:28 См. Втор. 19:14; 27:17..

29Видишь искусного в деле своем?

Он будет служить царям,

простым он служить не будет.