Miyambo 14 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 14:1-35

1Mkazi wanzeru amamanga banja lake,

koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

2Amene amayenda molungama amaopa Yehova,

koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.

3Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,

koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.

4Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,

koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.

5Mboni yokhulupirika sinama,

koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.

6Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,

koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.

7Khala kutali ndi munthu wopusa

chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.

8Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.

Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.

9Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,

koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.

10Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,

ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.

11Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,

koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.

12Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,

koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

13Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,

ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.

14Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,

koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.

15Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,

koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.

16Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,

koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.

17Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,

ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.

18Anthu opusa amalandira uchitsiru,

koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.

19Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,

ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.

20Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,

koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.

21Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa

koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.

22Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?

Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.

23Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,

koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.

24Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,

koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.

25Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,

koma mboni yabodza imaphetsa.

26Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira

ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.

27Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,

kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.

28Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,

koma popanda anthu kalonga amawonongeka.

29Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,

koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.

30Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,

koma nsanje imawoletsa mafupa.

31Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,

koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.

32Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,

koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.

33Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,

koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.

34Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,

koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

35Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,

koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 14:1-35

1智慧的女子建立家園,

愚昧的女子親手拆毀。

2行為正直的人敬畏耶和華,

行事邪僻的人輕視耶和華。

3愚人的狂言招來鞭打,

智者的唇舌保護自己。

4沒有耕牛槽頭淨,

五穀豐登需壯牛。

5忠實的證人不會撒謊,

虛假的證人謊話連篇。

6嘲諷者徒然尋智慧,

明哲人輕易得知識。

7你要遠離愚昧人,

他口中毫無知識。

8明哲憑智慧辨道,

愚人被愚昧欺騙。

9愚妄人戲看罪惡,

正直人彼此恩待。

10心頭的愁苦,唯有自己明白;

心中的喜樂,外人無法分享。

11惡人的房屋必遭毀滅,

正直人的帳篷必興盛。

12有的路看似正確,

最終卻通向死亡。

13歡笑難消內心的痛苦,

歡樂過後,悲傷猶在。

14背棄正道,自食惡果;

善人行善,必得善報。

15愚昧人什麼都信,

明哲人步步謹慎。

16智者小心謹慎,遠離惡事;

愚人驕傲自負,行事魯莽。

17急躁易怒的人做事愚昧,

陰險奸詐之人遭人痛恨。

18愚昧人得愚昧作產業,

明哲人得知識為冠冕。

19壞人俯伏在善人面前,

惡人俯伏在義人門口。

20窮人遭鄰舍厭,

富人朋友眾多。

21藐視鄰舍是罪過,

憐憫窮人蒙福樂。

22圖謀惡事的步入歧途,

行善的受愛戴和擁護。

23殷勤工作,帶來益處;

滿嘴空談,導致貧窮。

24智者以財富為冠冕,

愚人以愚昧為裝飾。

25誠實的證人挽救性命,

口吐謊言者欺騙他人。

26敬畏耶和華的信心堅定,

他的子孫也有庇護所。

27敬畏耶和華是生命的泉源,

可以使人避開死亡的陷阱。

28人民眾多,是君王的榮耀;

沒有臣民,君主必然敗亡。

29不輕易發怒者深明事理,

魯莽急躁的人顯出愚昧。

30心平氣和,滋潤生命;

妒火中燒,啃蝕骨頭。

31欺壓窮人等於侮辱造物主,

憐憫貧弱就是尊敬造物主。

32惡人因惡行而滅亡,

義人到死仍有倚靠。

33智慧存在哲士心裡,

愚人心中充滿無知。

34公義能叫邦國興盛,

罪惡是人民的恥辱。

35明智的臣子蒙王喜悅,

可恥的僕人惹王發怒。