Miyambo 13 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 13:1-25

1Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,

koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.

2Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,

koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.

3Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,

koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.

4Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,

koma munthu wakhama adzalemera.

5Munthu wolungama amadana ndi zabodza,

koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.

6Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,

koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.

7Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;

munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.

8Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,

koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.

9Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,

koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.

10Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,

koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.

11Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono

koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.

12Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,

koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.

13Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,

koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.

14Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;

amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.

15Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,

koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.

16Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,

koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.

17Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,

koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.

18Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,

koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.

19Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,

koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.

20Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;

koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.

21Choyipa chitsata mwini,

koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.

22Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,

koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.

23Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,

koma anthu opanda chilungamo amachilanda.

24Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,

koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.

25Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,

koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 13:1-25

1智慧兒聽從父訓,

嘲諷者不聽責備。

2口出良言嚐善果,

奸徒貪行殘暴事13·2 奸徒貪行殘暴事」或譯「奸徒必飽受虐待」。

3說話謹慎,可保性命;

口無遮攔,自取滅亡。

4懶惰人空有幻想,

勤快人心想事成。

5義人憎惡虛謊,

惡人行事可恥。

6公義守衛正直的人,

邪惡傾覆犯罪之徒。

7有人強充富有,

其實身無分文;

有人假裝貧窮,

卻是腰纏萬貫。

8富人用財富贖命,

窮人卻免受驚嚇。

9義人的光燦爛,

惡人的燈熄滅。

10自高自大招惹紛爭,

虛心受教才是睿智。

11不義之財必耗盡,

勤儉積蓄財富增。

12盼望無期,使人憂傷;

夙願得償,帶來生機13·12 帶來生機」希伯來文是「使人像棵生命樹」。

13蔑視訓言,自招滅亡;

敬畏誡命,必得賞賜。

14智者的訓言是生命之泉,

可使人避開死亡的網羅。

15睿智使人蒙恩惠,

奸徒之路通滅亡。

16明哲知而後行,

愚人炫耀愚昧。

17奸惡的使者陷入災禍,

忠誠的使者帶來醫治。

18不受管教的貧窮羞愧,

接受責備的受到尊崇。

19願望實現使心甘甜,

遠離惡事為愚人憎惡。

20與智者同行必得智慧,

與愚人結伴必受虧損。

21禍患追趕罪人,

義人必得善報。

22善人為子孫留下產業,

罪人給義人積聚財富。

23窮人的田地出產豐富,

因不公而被搶掠一空。

24不用杖管教兒女是憎惡他們,

疼愛兒女的隨時管教他們。

25義人豐衣足食,

惡人食不果腹。