Masalimo 83 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Nueva Versión Internacional

Salmo 83:1-18

Salmo 83Sal 83 En el texto hebreo 83:1-18 se numera 83:2-19.

Cántico. Salmo de Asaf.

1Oh Dios, no guardes silencio;

no te quedes callado e impasible, oh Dios.

2Mira cómo se alborotan tus enemigos,

cómo te desafían los que te odian.

3Con astucia conspiran contra tu pueblo;

conspiran contra aquellos a quienes tú proteges.

4Y dicen: «¡Vengan, destruyamos su nación!

¡Que el nombre de Israel no vuelva a recordarse!».

5Como un solo hombre se confabulan;

han hecho un pacto contra ti:

6los campamentos de Edom y de Ismael,

los de Moab y de Agar,

7Guebal,83:7 Guebal. Es decir, Biblos. Amón y Amalec,

los de Filistea y los habitantes de Tiro.

8Hasta Asiria se les ha unido;

ha apoyado a los descendientes de Lot. Selah

9Haz con ellos como hiciste con Madián,

como hiciste con Sísara y Jabín en el río Quisón,

10los cuales perecieron en Endor

y quedaron en la tierra, como estiércol.

11Haz con sus nobles como hiciste con Oreb y con Zeb;

haz con todos sus príncipes como hiciste con Zeba y con Zalmuna,

12que decían: «Vamos a adueñarnos

de los pastizales de Dios».

13Hazlos rodar como zarzas, Dios mío;

como paja que se lleva el viento.

14Y así como el fuego consume los bosques

y las llamas incendian las montañas,

15así persíguelos con tus tempestades

y aterrorízalos con tu tormenta.

16Señor, cúbreles el rostro de deshonra

para que busquen tu nombre.

17Queden avergonzados y angustiados para siempre;

que perezcan humillados.

18Que sepan que tú eres el Señor,

que ese es tu nombre;

que sepan que solo tú eres el Altísimo

sobre toda la tierra.