Miyambo 1 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

Nueva Versión Internacional

Proverbios 1:1-33

Prólogo: Propósito y tema

1Proverbios de Salomón, hijo de David, rey de Israel:

2para adquirir sabiduría y disciplina;

para discernir palabras de inteligencia;

3para recibir la corrección que dan la prudencia,

la rectitud, la justicia y la equidad;

4para infundir prudencia en los inexpertos,

conocimiento y discreción en los jóvenes.

5Escuche esto el sabio y aumente su saber;

reciba dirección el entendido,

6para discernir el proverbio y la parábola,

los dichos de los sabios y sus enigmas.

7El temor del Señor es el principio del conocimiento;

los necios desprecian la sabiduría y la disciplina.

Exhortaciones a buscar la sabiduría

Advertencia contra el engaño

8Hijo mío, escucha las correcciones de tu padre

y no abandones las enseñanzas de tu madre.

9Adornarán tu cabeza como una hermosa diadema;

adornarán tu cuello como un collar.

10Hijo mío, si los pecadores quieren engañarte,

no vayas con ellos.

11Estos te dirán:

«¡Ven con nosotros!

Acechemos a algún inocente

y démonos el gusto de matar a algún incauto;

12traguémonos a alguien vivo,

como se traga la muerte1:12 la muerte. Lit. el Seol. a la gente;

devorémoslo entero,

como devora la tumba a los muertos.

13Obtendremos toda clase de riquezas;

con el botín llenaremos nuestras casas.

14Echa tu suerte con nosotros

y compartiremos contigo lo que obtengamos».

15¡Pero no te dejes llevar por ellos,1:15 no … por ellos. Lit. no vayas por sus caminos. hijo mío!

¡Apártate de sus senderos!

16Pues corren presurosos a hacer lo malo;

¡tienen prisa por derramar sangre!

17De nada sirve tender la red

a la vista de todos los pájaros,

18pero aquellos acechan su propia vida1:18 vida. Lit. sangre.

y acabarán por destruirse a sí mismos.

19Así terminan los que van tras ganancias mal habidas;

por estas perderán la vida.

Advertencia contra el rechazo a la sabiduría

20Clama la sabiduría en las calles;

en los lugares públicos levanta su voz.

21Clama en las esquinas de calles transitadas;

a la entrada de la ciudad razona:

22«¿Hasta cuándo, muchachos inexpertos,

seguirán aferrados a su inexperiencia?

¿Hasta cuándo, ustedes los insolentes,

se complacerán en su insolencia?

¿Hasta cuándo, ustedes los necios,

aborrecerán el conocimiento?

23¡Respondan a mis reprensiones!

Yo les compartiré mis pensamientos1:23 compartiré mis pensamientos. Lit. derramaré mi espíritu.

y les daré a conocer mis enseñanzas.

24Como ustedes no me escucharon cuando los llamé

ni me hicieron caso cuando les tendí la mano,

25sino que rechazaron todos mis consejos

y no acataron mis reprensiones,

26ahora yo voy a reírme de ustedes

cuando caigan en desgracia.

Yo seré quien se ría de ustedes

cuando les sobrevenga el miedo,

27cuando el miedo les sobrevenga como una tormenta

y la desgracia los arrastre como un torbellino.

28»Entonces me llamarán, pero no les responderé;

me buscarán, pero no me encontrarán.

29Por cuanto aborrecieron el conocimiento

y no quisieron temer al Señor;

30por cuanto no siguieron mis consejos,

sino que rechazaron mis reprensiones,

31cosecharán el fruto de su conducta,

se hartarán con sus propias intrigas;

32su desobediencia e inexperiencia los destruirán,

su complacencia y necedad los aniquilarán.

33Pero el que me obedezca vivirá tranquilo,

sosegado y sin temor del mal».