Masalimo 82 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 82:1-8

Salimo 82

Salimo la Asafu.

1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;

Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,

ndi kukondera anthu oyipa?

3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;

mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;

apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.

Amayendayenda mu mdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,

nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7Koma mudzafa ngati anthu wamba;

mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Nueva Versión Internacional

Salmo 82:1-8

Salmo 82

Salmo de Asaf.

1Dios preside el consejo celestial;

entre los dioses dicta sentencia:

2«¿Hasta cuándo juzgarán injustamente

y favorecerán a los malvados? Selah

3Defiendan la causa del débil y del huérfano;

háganles justicia al pobre y al oprimido.

4Salven al débil y al necesitado;

líbrenlos de la mano de los malvados.

5»Ellos no saben nada, no entienden nada.

Deambulan en la oscuridad;

se estremecen todos los cimientos de la tierra.

6»Yo les he dicho: “Ustedes son dioses;

todos ustedes son hijos del Altísimo”.

7Pero morirán como cualquier mortal;

caerán como cualquier otro gobernante».

8Levántate, oh Dios, y juzga a la tierra,

pues tuyas son todas las naciones.