Salimo 82
Salimo la Asafu.
1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Salmo 82
Salmo de Asaf.
1Dios preside el consejo celestial;
entre los dioses dicta sentencia:
2«¿Hasta cuándo juzgarán injustamente
y favorecerán a los malvados? Selah
3Defiendan la causa del débil y del huérfano;
háganles justicia al pobre y al oprimido.
4Salven al débil y al necesitado;
líbrenlos de la mano de los malvados.
5»Ellos no saben nada, no entienden nada.
Deambulan en la oscuridad;
se estremecen todos los cimientos de la tierra.
6»Yo les he dicho: “Ustedes son dioses;
todos ustedes son hijos del Altísimo”.
7Pero morirán como cualquier mortal;
caerán como cualquier otro gobernante».
8Levántate, oh Dios, y juzga a la tierra,
pues tuyas son todas las naciones.