Masalimo 40 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 40:1-17

Salimo 40

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mofatsa ndinadikira Yehova

Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.

2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,

mʼthope ndi mʼchithaphwi;

Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe

ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.

3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,

nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.

Ambiri adzaona,

nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

4Ndi wodala munthu

amakhulupirira Yehova;

amene sayembekezera kwa odzikuza,

kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.

5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,

ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.

Zinthu zimene munazikonzera ife

palibe amene angathe kukuwerengerani.

Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,

zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,

koma makutu anga mwawatsekula;

zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo

Inu simunazipemphe.

7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.

Mʼbuku mwalembedwa za ine.

8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;

lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;

sinditseka milomo yanga

monga mukudziwa Inu Yehova.

10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;

ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.

Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu

pa msonkhano waukulu.

11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;

chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.

12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;

machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.

Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,

ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13Pulumutseni Yehova;

Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.

14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga

achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;

onse amene amakhumba chiwonongeko changa

abwezedwe mwamanyazi.

15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”

abwerere akuchita manyazi.

16Koma iwo amene amafunafuna Inu

akondwere ndi kusangalala mwa Inu;

iwo amene amakonda chipulumutso chanu

nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;

Ambuye andiganizire.

Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;

Inu Mulungu wanga, musachedwe.

New Russian Translation

Псалтирь 40:1-14

Псалом 40

1Дирижеру хора. Псалом Давида.

2Блажен тот, кто о слабом40:2 Или: «о бедном». заботится:

во время беды избавит его Господь.

3Господь сохранит его и сбережет ему жизнь,

счастьем одарит его на земле

и не отдаст его на произвол врагов.

4Господь укрепит его на одре болезни

и с ложа недуга его поднимет.

5Я сказал: «Помилуй меня, Господь;

исцели меня – я пред Тобой согрешил».

6Враги мои зло говорят обо мне:

«Когда же умрет он и имя его погибнет?»

7Если приходит кто навестить меня,

то ложь говорит, а в сердце своем слагает злые слухи;

потом он выходит и всем их рассказывает.

8Все враги мои шепчутся против меня,

думают худшее обо мне40:8 Или: «зло замышляют против меня».:

9«Смертельный недуг его одолел;

он слег и больше ему не встать».

10Даже близкий друг, на которого я полагался,

тот, кто ел мой хлеб,

поднял свою пяту против меня40:10 См. Ин. 13:18, 21-27..

11Но Ты, Господи, помилуй меня;

подними меня, и я воздам им!

12Из того я узнаю, что угоден Тебе,

если враг мой не превозможет меня,

13а меня Ты поддержишь за непорочность мою

и поставишь пред Собою навеки.

14Благословен Господь, Бог Израиля,

от века и до века!

Аминь и аминь!