Masalimo 39 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

New Russian Translation

Псалтирь 39:1-18

Псалом 39

(Пс. 69)

1Дирижеру хора. Псалом Давида.

2Твердо надеялся я на Господа,

и Он склонился ко мне и услышал мой крик.

3Он поднял меня из страшной пропасти,

из зыбкой трясины.

Он поставил ноги мои на камень

и стопы мои утвердил.

4Он вложил мне в уста новую песнь –

хвалу нашему Богу.

Увидят многие и устрашатся,

и будут на Господа уповать.

5Блажен тот человек,

кто надежду свою возлагает на Господа,

кто не обращается к гордым

и к уклоняющимся ко лжи.

6Многочисленны, Господи, мой Боже,

чудеса, которые Ты сотворил,

и замыслы Твои о нас!

Кто с Тобою сравнится!

Я бы стал возвещать о них и рассказывать,

но их больше, чем можно счесть.

7Не захотел Ты ни жертв, ни даров,

но Ты открыл39:7 Или: «проколол». Ср. Исх. 21:5-6. мне уши39:7 В одном из древних переводов: «Ты приготовил мне тело»..

Ты не потребовал ни всесожжения,

ни жертвы за грех.

8Тогда я сказал: «Вот, я иду,

как и написано в свитке обо мне.

9Бог мой, я желаю волю Твою исполнить,

и в сердце моем Твой Закон».

10В большом собрании я возвещал Твою праведность;

я не удерживал своих уст –

Ты это знаешь, Господи.

11Я не скрыл Твоей праведности в своем сердце,

но возвещал верность Твою и спасение.

Я не таил Твою милость и истину

перед большим собранием.

12Не удерживай, Господи,

щедрот Твоих от меня,

пусть милость Твоя и истина

охраняют меня непрестанно.

13Ведь беды окружили меня, и нет им числа;

грехи мои мной овладели, и не могу я видеть.

Их больше, чем волос на моей голове;

храбрость39:13 Букв.: «сердце мое». меня оставила.

14Господи, да будет угодно Тебе избавить меня!

Поспеши мне на помощь, Господи!

15Пусть все, кто ищет жизни моей,

будут пристыжены и посрамлены.

Пусть все, кто хочет моей погибели,

в бесчестии повернут назад.

16Пусть ужаснутся своему позору

говорящие мне: «Ага! Ага!»

17Пусть ликуют и радуются о Тебе

все ищущие Тебя.

Пусть те, кто любит Твое спасение,

говорят непрестанно: «Велик Господь!»

18Я же беден и нищ,

пусть Владыка позаботится обо мне.

Ты – помощь моя и мой избавитель;

Бог мой, не замедли!