Miyambo 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

New Russian Translation

Притчи 1:1-33

Вступление

1Притчи Соломона, сына Давидова, царя Израиля:

2да принесут они мудрость и наставление

и да помогут осмыслить разумные высказывания;

3да научат они правилам благоразумной жизни,

праведности, справедливости и честности

4и дадут простакам проницательность,

а юным – знание и рассудительность;

5пусть послушают мудрые и умножат познания,

и пусть разумные получат советы;

6да уразумеют они пословицы и притчи,

слова мудрецов и загадки их.

7Страх перед Господом – начало мудрости,

только глупцы1:7 Еврейское слово, переведенное здесь как «глупцы», в книге Притчей и нередко в других местах Ветхого Завета обозначает человека, несовершенного нравственно. презирают мудрость и наставление.

Наставления в мудрости

Предостережение от соблазна

8Сын мой, послушай наставление своего отца

и не отвергай поучения своей матери.

9Они будут прекрасным венком на твоей голове

и ожерельем на твоей шее.

10Сын мой, если грешники соблазняют тебя,

не поддавайся им.

11Если скажут они: «Идем с нами,

устроим засаду для пролития крови,

без причины подстережем невинного,

12живьем их проглотим, как мир мертвых1:12 Мир мертвых – евр.: «шеол».,

целиком – как тех, кто нисходит в пропасть;

13награбим всевозможных дорогих вещей

и наполним дома свои добычей.

14Бросай с нами жребий,

общая будет у нас мошна»,

15то не ходи с ними, сын мой,

не вставай на путь их.

16Ведь их ноги бегут к злу,

спешат они на пролитие крови.

17Как бессмысленно ставить сеть

на глазах у всех птиц,

18но эти люди устраивают засаду для пролития своей же крови,

подстерегают самих же себя!

19Таковы пути всех, кто жаждет преступной добычи;

она отнимает жизнь у завладевших ею.

Предостережение не отвергать мудрости

20Мудрость восклицает на улицах,

возвышает свой голос на площадях;

21на углах шумных улиц1:21 Смысл этого места в еврейском тексте неясен. кричит она

и при входе в городские ворота держит речь:

22«До каких же пор вы, простаки,

будете любить свою простоту?

Сколько же еще глумливые

будут наслаждаться насмешками,

а глупцы – ненавидеть знание?

23Если бы вы ответили на мой укор,

я излила бы на вас мой дух

и открыла бы вам свои мысли1:23 Букв.: «мои слова»..

24Но раз вы отвергли меня, когда я призывала,

и никто не внимал, когда я протягивала вам руку;

25раз вы пренебрегли всеми моими советами

и не приняли моего укора,

26то и я в свой черед посмеюсь над вашей бедой,

поиздеваюсь, когда поразит вас ужас, –

27когда поразит вас ужас, как буря,

и беда пронесется над вами, как вихрь,

когда горе и скорбь вас подавят.

28Тогда будут звать меня, но я не отвечу;

будут искать меня, но не найдут.

29Раз они знание возненавидели

и страх перед Господом не избрали,

30раз мой совет не приняли

и укор мой с презрением отвергли –

31то они будут есть плоды своего пути

и получат сполна от своих замыслов.

32Ведь своенравие убьет простаков,

и беспечность погубит глупцов,

33но слушающий меня будет жить безопасно и спокойно,

не страшась беды».