Masalimo 139 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 139:1-24

Salimo 139

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mwandisanthula

ndipo mukundidziwa.

2Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka;

mumazindikira maganizo anga muli kutali.

3Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga;

mumadziwa njira zanga zonse.

4Mawu asanatuluke pa lilime langa

mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.

5Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe;

mwasanjika dzanja lanu pa ine.

6Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga,

ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.

7Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu?

Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?

8Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko;

ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko.

9Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa,

ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,

10kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,

dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.

11Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu

ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”

12komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu;

usiku udzawala ngati masana,

pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.

13Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga;

munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.

14Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa;

ntchito zanu ndi zodabwitsa,

zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.

15Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu

pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi,

pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.

16Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe.

Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu

asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.

17Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu,

ndi zosawerengeka ndithu!

18Ndikanaziwerenga,

zikanakhala zochuluka kuposa mchenga;

pamene ndadzuka, ndili nanube.

19Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu!

Chokereni inu anthu owononga anzanu!

20Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa;

adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.

21Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova?

Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?

22Ndimadana nawo kwathunthu;

ndi adani anga.

23Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga;

Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.

24Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine,

ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

King James Version

Psalms 139:1-24

To the chief Musician, A Psalm of David.

1O LORD, thou hast searched me, and known me.

2Thou knowest my downsitting and mine uprising, thou understandest my thought afar off.

3Thou compassest my path and my lying down, and art acquainted with all my ways.139.3 compassest: or, winnowest

4For there is not a word in my tongue, but, lo, O LORD, thou knowest it altogether.

5Thou hast beset me behind and before, and laid thine hand upon me.

6Such knowledge is too wonderful for me; it is high, I cannot attain unto it.

7Whither shall I go from thy spirit? or whither shall I flee from thy presence?

8If I ascend up into heaven, thou art there: if I make my bed in hell, behold, thou art there.

9If I take the wings of the morning, and dwell in the uttermost parts of the sea;

10Even there shall thy hand lead me, and thy right hand shall hold me.

11If I say, Surely the darkness shall cover me; even the night shall be light about me.

12Yea, the darkness hideth not from thee; but the night shineth as the day: the darkness and the light are both alike to thee.139.12 hideth…: Heb. darkeneth not139.12 the darkness and…: Heb. as is the darkness, so is the light

13For thou hast possessed my reins: thou hast covered me in my mother’s womb.

14I will praise thee; for I am fearfully and wonderfully made: marvellous are thy works; and that my soul knoweth right well.139.14 right…: Heb. greatly

15My substance was not hid from thee, when I was made in secret, and curiously wrought in the lowest parts of the earth.139.15 substance: or, strength, or, body

16Thine eyes did see my substance, yet being unperfect; and in thy book all my members were written, which in continuance were fashioned, when as yet there was none of them.139.16 all…: Heb. all of them139.16 which…: or, what days they should be fashioned

17How precious also are thy thoughts unto me, O God! how great is the sum of them!

18If I should count them, they are more in number than the sand: when I awake, I am still with thee.

19Surely thou wilt slay the wicked, O God: depart from me therefore, ye bloody men.

20For they speak against thee wickedly, and thine enemies take thy name in vain.

21Do not I hate them, O LORD, that hate thee? and am not I grieved with those that rise up against thee?

22I hate them with perfect hatred: I count them mine enemies.

23Search me, O God, and know my heart: try me, and know my thoughts:

24And see if there be any wicked way in me, and lead me in the way everlasting.139.24 wicked…: Heb. way of pain, or, grief