Miyambo 1 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 1:1-33

Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu

1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:

2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;

kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;

3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,

akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.

4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,

achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.

5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,

ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,

6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,

mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.

7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.

Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.

Malangizo kuti Asunge Nzeru

Malangizo kwa Achinyamata

8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako

ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.

9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako

ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.

10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa

usamawamvere.

11Akadzati, “Tiye kuno;

tikabisale kuti tiphe anthu,

tikabisalire anthu osalakwa;

12tiwameze amoyo ngati manda,

ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.

13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali

ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;

14Bwera, chita nafe maere,

ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”

15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,

usatsagane nawo mʼnjira zawozo.

16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,

amathamangira kukhetsa magazi.

17Nʼkopanda phindu kutchera msampha

mbalame zikuona!

18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;

amangodzitchera okha msampha!

19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;

chumacho chimapha mwiniwake.

Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru

20Nzeru ikufuwula mu msewu,

ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;

21ikufuwula pa mphambano ya misewu,

ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,

22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?

Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?

Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?

23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.

Ine ndikukuwuzani maganizo anga

ndi kukudziwitsani mawu anga.

24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.

Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.

25Uphungu wanga munawunyoza.

Kudzudzula kwanga simunakusamale.

26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;

ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.

27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,

tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,

mavuto ndi masautso akadzakugwerani.

28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;

mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.

29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso

ndipo sanasankhe kuopa Yehova,

30popeza iwo sanasamale malangizo anga

ndipo ananyoza chidzudzulo changa.

31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo

ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.

32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,

ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.

33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;

adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

King James Version

Proverbs 1:1-33

1The proverbs of Solomon the son of David, king of Israel; 2To know wisdom and instruction; to perceive the words of understanding; 3To receive the instruction of wisdom, justice, and judgment, and equity;1.3 equity: Heb. equities 4To give subtilty to the simple, to the young man knowledge and discretion.1.4 discretion: or, advisement 5A wise man will hear, and will increase learning; and a man of understanding shall attain unto wise counsels: 6To understand a proverb, and the interpretation; the words of the wise, and their dark sayings.1.6 the interpretation: or, an eloquent speech

7¶ The fear of the LORD is the beginning of knowledge: but fools despise wisdom and instruction.1.7 the beginning: or, the principal part 8My son, hear the instruction of thy father, and forsake not the law of thy mother: 9For they shall be an ornament of grace unto thy head, and chains about thy neck.1.9 an…: Heb. an adding

10¶ My son, if sinners entice thee, consent thou not. 11If they say, Come with us, let us lay wait for blood, let us lurk privily for the innocent without cause: 12Let us swallow them up alive as the grave; and whole, as those that go down into the pit: 13We shall find all precious substance, we shall fill our houses with spoil: 14Cast in thy lot among us; let us all have one purse: 15My son, walk not thou in the way with them; refrain thy foot from their path: 16For their feet run to evil, and make haste to shed blood. 17Surely in vain the net is spread in the sight of any bird.1.17 in the…: Heb. in the eyes of every thing that hath a wing 18And they lay wait for their own blood; they lurk privily for their own lives. 19So are the ways of every one that is greedy of gain; which taketh away the life of the owners thereof.

20¶ Wisdom crieth without; she uttereth her voice in the streets:1.20 Wisdom: Heb. Wisdoms, that is, Excellent wisdom 21She crieth in the chief place of concourse, in the openings of the gates: in the city she uttereth her words, saying, 22How long, ye simple ones, will ye love simplicity? and the scorners delight in their scorning, and fools hate knowledge? 23Turn you at my reproof: behold, I will pour out my spirit unto you, I will make known my words unto you.

24¶ Because I have called, and ye refused; I have stretched out my hand, and no man regarded; 25But ye have set at nought all my counsel, and would none of my reproof: 26I also will laugh at your calamity; I will mock when your fear cometh; 27When your fear cometh as desolation, and your destruction cometh as a whirlwind; when distress and anguish cometh upon you. 28Then shall they call upon me, but I will not answer; they shall seek me early, but they shall not find me: 29For that they hated knowledge, and did not choose the fear of the LORD: 30They would none of my counsel: they despised all my reproof. 31Therefore shall they eat of the fruit of their own way, and be filled with their own devices. 32For the turning away of the simple shall slay them, and the prosperity of fools shall destroy them.1.32 turning…: or, ease of the simple 33But whoso hearkeneth unto me shall dwell safely, and shall be quiet from fear of evil.