Masalimo 140 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 140:1-13

Salimo 140

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;

tetezeni kwa anthu ankhanza,

2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa

ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.

3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;

pa milomo yawo pali ululu wa mamba.

Sela

4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;

tchinjirizeni kwa anthu ankhanza

amene amakonza zokola mapazi anga.

5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;

iwo atchera zingwe za maukonde awo

ndipo anditchera misampha pa njira yanga.

Sela

6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

Imvani kupempha kwanga Yehova.

7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,

mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.

8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;

musalole kuti zokonza zawo zitheke,

mwina iwo adzayamba kunyada.

Sela

9Mitu ya amene andizungulira

iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.

10Makala amoto agwere pa iwo;

aponyedwe pa moto,

mʼmaenje amatope, asatulukemonso.

11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;

choyipa chilondole anthu ankhanza.

12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,

ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.

13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,

ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

King James Version

Psalms 140:1-13

To the chief Musician, A Psalm of David.

1Deliver me, O LORD, from the evil man: preserve me from the violent man;140.1 violent…: Heb. man of violences

2Which imagine mischiefs in their heart; continually are they gathered together for war.

3They have sharpened their tongues like a serpent; adders’ poison is under their lips. Selah.

4Keep me, O LORD, from the hands of the wicked; preserve me from the violent man; who have purposed to overthrow my goings.

5The proud have hid a snare for me, and cords; they have spread a net by the wayside; they have set gins for me. Selah.

6I said unto the LORD, Thou art my God: hear the voice of my supplications, O LORD.

7O GOD the Lord, the strength of my salvation, thou hast covered my head in the day of battle.

8Grant not, O LORD, the desires of the wicked: further not his wicked device; lest they exalt themselves. Selah.140.8 lest…: or, let them not be exalted

9As for the head of those that compass me about, let the mischief of their own lips cover them.

10Let burning coals fall upon them: let them be cast into the fire; into deep pits, that they rise not up again.

11Let not an evil speaker be established in the earth: evil shall hunt the violent man to overthrow him.140.11 an…: or, an evil speaker (Heb. a man of tongue), a wicked man of violence, be established in the earth: let him be hunted to his overthrow

12I know that the LORD will maintain the cause of the afflicted, and the right of the poor.

13Surely the righteous shall give thanks unto thy name: the upright shall dwell in thy presence.