Masalimo 138 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 138:1-8

Salimo 138

Salimo la Davide.

1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”

2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera

ndipo ndidzayamika dzina lanu

chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,

pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu

kupambana zinthu zonse.

3Pamene ndinayitana, munandiyankha;

munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,

pamene amva mawu a pakamwa panu.

5Iwo ayimbe za njira za Yehova,

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,

koma anthu onyada amawadziwira chapatali.

7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,

mumasunga moyo wanga;

mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,

mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.

8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;

chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha

musasiye ntchito ya manja anu.

King James Version

Psalms 138:1-8

A Psalm of David.

1I will praise thee with my whole heart: before the gods will I sing praise unto thee.

2I will worship toward thy holy temple, and praise thy name for thy lovingkindness and for thy truth: for thou hast magnified thy word above all thy name.

3In the day when I cried thou answeredst me, and strengthenedst me with strength in my soul.

4All the kings of the earth shall praise thee, O LORD, when they hear the words of thy mouth.

5Yea, they shall sing in the ways of the LORD: for great is the glory of the LORD.

6Though the LORD be high, yet hath he respect unto the lowly: but the proud he knoweth afar off.

7Though I walk in the midst of trouble, thou wilt revive me: thou shalt stretch forth thine hand against the wrath of mine enemies, and thy right hand shall save me.

8The LORD will perfect that which concerneth me: thy mercy, O LORD, endureth for ever: forsake not the works of thine own hands.