Salimo 137
1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
pamene tinakumbukira Ziyoni.
2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
tinapachika apangwe athu,
3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
mʼdziko lachilendo?
5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
chimwemwe changa chachikulu.
7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
mpaka pa maziko ake!”
8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
pa zimene watichitira.
9Amene adzagwira makanda ako
ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
1By the rivers of Babylon, there we sat down, yea, we wept, when we remembered Zion.
2We hanged our harps upon the willows in the midst thereof.
3For there they that carried us away captive required of us a song; and they that wasted us required of us mirth, saying, Sing us one of the songs of Zion.137.3 a song: Heb. the words of a song137.3 wasted…: Heb. laid us on heaps
4How shall we sing the LORD’s song in a strange land?137.4 strange…: Heb. land of a stranger?
5If I forget thee, O Jerusalem, let my right hand forget her cunning.
6If I do not remember thee, let my tongue cleave to the roof of my mouth; if I prefer not Jerusalem above my chief joy.137.6 my chief…: Heb. the head of my joy
7Remember, O LORD, the children of Edom in the day of Jerusalem; who said, Rase it, rase it, even to the foundation thereof.137.7 Rase it: Heb. Make bare
8O daughter of Babylon, who art to be destroyed; happy shall he be, that rewardeth thee as thou hast served us.137.8 destroyed: Heb. wasted137.8 rewardeth…: Heb. recompenseth unto thee thy deed which thou didst to us
9Happy shall he be, that taketh and dasheth thy little ones against the stones.137.9 the stones: Heb. the rock