Luka 14 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 14:1-35

Yesu Mʼnyumba ya Mfarisi

1Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa. 2Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo. 3Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?” 4Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.

5Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?” 6Ndipo iwo analibe choyankha.

Kudzichepetsa ndi Kulandira Ulemu

7Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili: 8“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu. 9Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika. 10Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse. 11Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”

12Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako. 13Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona. 14Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”

Fanizo la Phwando Lalikulu

15Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”

16Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri. 17Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’

18“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’

19“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’

20“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’

21“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’

22“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’

23“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze. 24Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’ ”

Dipo la Kutsatira Yesu

25Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati, 26“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga. 27Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.

28“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire? 29Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka, 30nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’

31“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000? 32Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere. 33Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.

34“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani? 35Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja.

“Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 14:1‏-35

عيسی باز در روز شنبه شفا می‌بخشد

1‏-2يک روز شنبه، عيسی در خانهٔ يكی از بزرگان فريسی دعوت داشت. در آنجا بيماری نيز حضور داشت كه بدنش آب آورده و دستها و پايهايش متورم شده بود. فريسيان مراقب عيسی بودند تا ببينند آيا آن بيمار را شفا می‌دهد يا نه.

3عيسی از فريسيان و علمای دين كه حاضر بودند، پرسيد: «آيا طبق دستورات تورات، می‌توان بيماری را در روز شنبه شفا داد يا نه؟»

4ايشان پاسخی ندادند! پس عيسی دست مريض را گرفت و شفايش داد و به خانه فرستاد. 5سپس رو به ايشان كرد و پرسيد: «كدام يک از شما، در روز شنبه كار نمی‌كند؟ آيا اگر الاغ يا گاوتان در چاه بيفتد، فوراً نمی‌رويد تا بيرونش بياوريد؟»

6اما ايشان جوابی نداشتند كه بدهند.

درس فروتنی

7عيسی چون ديد كه همهٔ مهمانان سعی می‌كنند بالای مجلس بنشينند، ايشان را چنين نصيحت كرد: 8«هرگاه به جشن عروسی دعوت می‌شويد، بالای مجلس ننشينيد، زيرا ممكن است مهمانی مهمتر از شما بيايد و 9میزبان از شما بخواهد كه جايتان را به او بدهيد. آنگاه بايد با شرمساری برخيزيد و در پايين مجلس بنشينيد! 10پس اول، پايين مجلس بنشينيد تا وقتی میزبان شما را آنجا ببيند، بيايد و شما را بالا ببرد. آنگاه، در حضور مهمانان سربلند خواهيد شد. 11زيرا هر كه بكوشد خود را بزرگ جلوه دهد، خوار خواهد شد، اما كسی كه خود را فروتن سازد، سربلند خواهد گرديد.»

12سپس رو به صاحب خانه كرد و گفت: «هرگاه ضيافتی ترتيب می‌دهی، دوستان و برادران و بستگان و همسايگان ثروتمند خود را دعوت نكن، چون ايشان هم در عوض، تو را دعوت خواهند كرد. 13بلكه وقتی مهمانی می‌دهی، فقرا، لنگان و شلان و نابينايان را دعوت كن. 14آنگاه خدا در روز قيامت درستكاران، تو را اجر خواهد داد، زيرا كسانی را خدمت كردی كه نتوانستند محبتت را جبران كنند.»

ضيافت ملكوت خدا

15يكی از آنانی كه بر سر سفره نشسته بود، چون اين سخنان را شنيد، گفت: «خوشا به حال كسی كه در ضيافت ملكوت خدا شركت كند!»

16عيسی در جواب او اين داستان را بيان كرد: «شخصی ضيافت مفصلی ترتيب داد و بسياری را دعوت كرد. 17وقتی همه چيز آماده شد، خدمتكار خود را فرستاد تا به مهمانان اطلاع دهد كه وقت آمدنشان فرا رسيده است. 18اما هر يک از دعوت‌شدگان به نوعی عذر و بهانه آوردند. يكی گفت كه قطعه زمينی خريده است و بايد برود آن را ببيند. 19ديگری گفت كه پنج جفت گاو خريده است و بايد برود آنها را امتحان كند. 20يكی ديگر نيز گفت كه تازه ازدواج كرده و به همين دليل نمی‌تواند بيايد.

21«خدمتكار بازگشت و پاسخ دعوت‌شدگان را به اطلاع ارباب خود رسانيد. ارباب عصبانی شد و به او گفت: فوری به ميدانها و كوچه‌های شهر برو و فقرا و مفلوجان و شلان و كوران را دعوت كن! 22وقتی اين دستور اجرا شد، باز هنوز جای اضافی باقی بود. 23پس ارباب به خدمتكارش گفت: حال به شاهراهها و كوره‌راهها برو و هر كه را می‌بينی به اصرار بياور تا خانه من پر شود. 24چون از آن كسانی كه دعوت كرده بودم، هيچيک طعم خوراكهايی را كه تدارک ديده‌ام، نخواهد چشيد!»

بهای پيروی از مسيح

25يكبار عيسی روگرداند و به جمعيت بزرگی كه به دنبال او حركت می‌كردند، گفت: 26«هر كه می‌خواهد پيرو من باشد، بايد مرا از پدر و مادر، زن و فرزند، برادر و خواهر و حتی از جان خود نيز بيشتر دوست بدارد. 27هر كه صليب خود را برندارد و به دنبال من نيايد، نمی‌تواند شاگرد من باشد.

28«اما پيش از آنكه در مورد پيروی از من، تصميمی بگيريد، همه جوانب را خوب بسنجيد! اگر كسی در نظر دارد ساختمانی بسازد، ابتدا مخارج آن را برآورد می‌كند تا ببيند آيا از عهده آن برمی‌آيد يا نه. 29مبادا وقتی بنياد ساختمان را گذاشت، سرمايه‌اش تمام شود و نتواند كار را تمام كند! آنگاه همه تمسخركنان خواهند گفت: 30اين شخص ساختمان را شروع كرد، اما نتوانست آن را به پايان برساند!

31«يا فرض كنيد پادشاهی می‌خواهد با پادشاه ديگری بجنگد. او ابتدا با مشاورانش مشورت می‌كند تا ببيند كه آيا با يک نيروی ده هزار نفری، می‌تواند يک لشكر بيست هزار نفری را شكست بدهد يا نه. 32اگر ديد كه قادر به اين كار نيست، هنگامی كه سپاه دشمن هنوز دور است، نمايندگانی را می‌فرستد تا درباره شرايط صلح مذاكره كنند. 33به همين طريق، كسی كه می‌خواهد شاگرد من شود، نخست بايد بنشيند و حساب كند كه آيا می‌تواند به خاطر من از مال و دارايی خود چشم بپوشد يا نه.

34«اگر نمک طعم و خاصيت خود را از دست بدهد، ديگر چه فايده‌ای دارد؟ 35نمک بی‌طعم و خاصيت حتی به درد كود زمين هم نمی‌خورد. فقط بايد آن را دور ريخت. اگر می‌خواهيد منظورم را درک كنيد، با دقت به سخنانم گوش فرا دهيد!»