Luka 15 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 15:1-32

Fanizo la Nkhosa Yotayika

1Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake. 2Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”

3Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili: 4“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza? 5Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe 6ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’ 7Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”

Fanizo la Ndalama Yotayika

8“Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza? 9Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’ 10Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”

Fanizo la Mwana Wolowerera

11Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri. 12Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.

13“Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko. 14Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka. 15Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba. 16Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.

17“Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala! 18Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu. 19Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’ 20Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake.

“Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.

21“Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’

22“Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato. 23Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera. 24Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.

25“Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina. 26Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika. 27Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’

28“Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira. 29Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga. 30Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’ ”

31Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako. 32Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 15:1-32

داستان گوسفند گمشده

1بسياری از مأمورين باج و خراج و ساير مطرودين جامعه، اغلب گرد می‌آمدند تا سخنان عيسی را بشنوند. 2اما فريسيان و علمای دين از او ايراد گرفتند كه چرا با مردمان بدنام و پست، نشست و برخاست می‌كند و بر سر يک سفره می‌نشيند. 3پس عيسی اين مثل را برای ايشان آورد: 4«اگر يكی از شما، صد گوسفند داشته باشد و يكی از آنها از گله دور بيفتد و گم شود، چه می‌كند؟ يقيناً آن نود و نه گوسفند را می‌گذارد و به جستجوی آن گمشده می‌رود تا آن را پيدا كند. 5وقتی آن را يافت با شادی بر دوش می‌گذارد، 6و به خانه می‌آيد و دوستان و همسايگان را جمع می‌كند تا برای پيدا شدن گوسفند گمشده با او شادی كنند.

7«به همين صورت، با توبه يک گناهكار گمراه و بازگشت او به سوی خدا، در آسمان شادی بيشتری رخ می‌دهد تا برای نود و نه نفر ديگر كه گمراه و سرگردان نشده‌اند.

داستان سکه گمشده

8«يا مثلاً اگر زنی ده سكهٔ نقره داشته باشد و يكی را گم كند، آيا چراغ روشن نمی‌كند و با دقت تمام گوشه و كنار خانه را نمی‌گردد و همه جا را جارو نمی‌كند تا آن را پيدا كند؟ 9و وقتی آن را پيدا كرد، آيا تمام دوستان و همسايگان خود را جمع نمی‌كند تا با او شادی كنند؟ 10به همين‌سان، فرشتگان خدا شادی می‌كنند از اينكه يک گناهكار توبه كند و به سوی خدا بازگردد.»

داستان پسر گمشده

11برای آنكه موضوع بيشتر روشن شود، عيسی اين داستان را نيز بيان فرمود: «مردی دو پسر داشت. 12روزی پسر كوچک به پدرش گفت: پدر، بهتر است سهمی كه از دارايی تو بايد به من به ارث برسد، از هم اكنون به من بدهی. پس پدر موافقت نمود و دارايی خود را بين دو پسرش تقسيم كرد.

13«چندی نگذشت كه پسر كوچكتر، هر چه داشت جمع كرد و به سرزمينی دور دست رفت. در آنجا تمام ثروت خود را در عياشی‌ها و راههای نادرست بر باد داد. 14از قضا، در همان زمان كه تمام پولهايش را خرج كرده بود، قحطی شديدی در آن سرزمين پديد آمد، طوری كه او سخت در تنگی قرار گرفت و نزديک بود از گرسنگی بميرد. 15پس به ناچار رفت و به بندگی يكی از اهالی آن منطقه درآمد. او نيز وی را به مزرعه خود فرستاد تا خوكهايش را بچراند. 16آن پسر به روزی افتاده بود كه آرزو می‌كرد بتواند با خوراک خوكها، شكم خود را سير كند؛ كسی هم به او كمک نمی‌كرد.

17«سرانجام روزی به خود آمد و فكر كرد: در خانه پدرم، خدمتكاران نيز خوراک كافی و حتی اضافی دارند، و من اينجا از گرسنگی هلاک می‌شوم! 18پس برخواهم خاست و نزد پدر رفته، به او خواهم گفت: ای پدر، من در حق خدا و در حق تو گناه كرده‌ام، 19و ديگر لياقت اين را ندارم كه مرا پسر خود بدانی، خواهش می‌كنم مرا به نوكری خود بپذير!

20«پس بی‌درنگ برخاست و به سوی خانهٔ پدر به راه افتاد. اما هنوز از خانه خيلی دور بود كه پدرش او را ديد و دلش به حال او سوخت و به استقبالش دويد و او را در آغوش گرفت و بوسيد.

21«پسر به او گفت: پدر، من در حق خدا و در حق تو گناه كرده‌ام، و ديگر لياقت اين را ندارم كه مرا پسر خود بدانی.

22«اما پدرش به خدمتكاران گفت: عجله كنيد! بهترين جامه را از خانه بياوريد و به او بپوشانيد! انگشتری به دستش و كفش به پايش كنيد! 23و گوساله پرواری را بياوريد و سر ببريد تا جشن بگيريم و شادی كنيم! 24چون اين پسر من، مرده بود و زنده شد؛ گم شده بود و پيدا شده است!

«پس ضيافت مفصلی بر پا كردند.

25«در اين اثنا، پسر بزرگ در مزرعه مشغول كار بود. وقتی به خانه باز می‌گشت، صدای ساز و رقص و پايكوبی شنيد. 26پس يكی از خدمتكاران را صدا كرد و پرسيد: چه خبر است؟

27«خدمتكار جواب داد: برادرت بازگشته و پدرت چون او را صحيح و سالم بازيافته، گوساله پرواری را سر بريده و جشن گرفته است!

28«برادر بزرگ عصبانی شد و حاضر نشد وارد خانه شود. تا اينكه پدرش بيرون آمد و به او التماس كرد كه به خانه بيايد. 29اما او در جواب گفت: سالهاست كه من همچون يک غلام به تو خدمت كرده‌ام و حتی يک بار هم از دستوراتت سرپيچی نكرده‌ام. اما در تمام اين مدت به من چه دادی؟ حتی يک بزغاله هم ندادی تا سر ببُرم و با دوستانم به شادی بپردازم! 30اما اين پسرت كه ثروت تو را با فاحشه‌ها تلف كرده، حال كه بازگشته است، بهترين گوساله پرواری را كه داشتيم، سر بريدی و برايش جشن گرفتی!

31«پدرش گفت: پسر عزيزم، تو هميشه در كنار من بوده‌ای؛ و هر چه من دارم، در واقع به تو تعلق دارد و سهم ارث توست! 32اما حالا بايد جشن بگيريم و شادی كنيم، چون اين برادر تو، مرده بود و زنده شده است؛ گم شده بود و پيدا شده است!»